< Genesis 24 >

1 Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
Now Abraham was very old and Yahweh had blessed Abraham in all things.
2 Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
Abraham said to his servant, the one who was the oldest of his household and who was in charge of all that he had, “Put your hand under my thigh
3 Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
and I will make you swear by Yahweh, the God of heaven and the God of the earth, that you will not get a wife for my son from the daughters of the Canaanites, among whom I make my home.
4 koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
But you will go to my country, and to my relatives, and get a wife for my son Isaac.”
5 Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
The servant said to him, “What if the woman will not be willing to follow me to this land? Must I take your son back to the land from which you came?”
6 Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
Abraham said to him, “Make sure that you do not take my son back there!
7 Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
Yahweh, the God of heaven, who took me from my father's house and from the land of my relatives, and who promised me with a solemn oath saying, 'To your offspring I will give this land,' he will send his angel before you, and you will get a wife for my son from there.
8 Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
But if the woman is not willing to follow you, then you will be free from this oath of mine. Only you are not to take my son back there.”
9 Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
So the servant put his hand under the thigh of Abraham his master, and swore to him concerning this matter.
10 Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
The servant took ten of his master's camels and departed. He also took with him all kinds of gifts from his master. He departed and went to the region of Aram Naharaim, to the city of Nahor.
11 Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
He made the camels kneel down outside the city by the well of water. It was evening, the time that women go out to draw water.
12 Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
Then he said, “Yahweh, God of my master Abraham, grant me success today and show covenant faithfulness to my master Abraham.
13 Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
Look, here I am standing by the spring of water, and the daughters of the men of the city are coming out to draw water.
14 Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
Let it happen like this. When I say to a young woman, 'Please lower your pitcher so that I may drink,' and she says to me, 'Drink, and I will water your camels too,' then let her be the one that you have appointed for your servant Isaac. By this I will know that you have shown covenant faithfulness to my master.”
15 Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
It came about that even before he had finished speaking, behold, Rebekah came out with her water pitcher on her shoulder. Rebekah was born to Bethuel son of Milkah, the wife of Nahor, Abraham's brother.
16 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
The young woman was very beautiful and a virgin. No man had slept with her. She went down to the spring and filled her pitcher, and came up.
17 Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
Then the servant ran to meet her and said, “Please give me a little drink of water from your pitcher.”
18 Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
She said, “Drink, my master,” and she quickly let down her pitcher on her hand, and gave him a drink.
19 Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
When she had finished giving him a drink, she said, “I will draw water for your camels also, until they have finished drinking.”
20 Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
So she hurried and emptied her pitcher into the trough, then ran again to the well to draw water, and drew water for all his camels.
21 Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
The man watched her in silence to see whether Yahweh had prospered his journey or not.
22 Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
As the camels finished drinking, the man brought out a gold nose ring weighing half a shekel, and two gold bracelets for her arms weighing ten shekels,
23 Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
and asked, “Whose daughter are you? Tell me please, is there room in your father's house for us to spend the night?”
24 Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
She said to him, “I am the daughter of Bethuel son of Milkah, whom she bore to Nahor.”
25 Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
She also said to him, “We have plenty of both straw and feed, and also room for you to spend the night.”
26 Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
Then the man bowed down and worshiped Yahweh.
27 nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
He said, “Blessed be Yahweh, the God of my master Abraham, who has not forsaken his covenant faithfulness and his trustworthiness toward my master. As for me, Yahweh has led me directly to the house of my master's relatives.”
28 Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
Then the young woman ran and told her mother's household about all of these things.
29 Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
Now Rebekah had a brother, and his name was Laban. Laban ran to the man who was out at the road by the spring.
30 Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
When he had seen the nose ring and the bracelets on his sister's arms, and when he had heard the words of Rebekah his sister, “This is what the man said to me,” he went to the man, and, behold, he was standing by the camels at the spring.
31 Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
Then Laban said, “Come, you blessed of Yahweh. Why are you standing outside? I have prepared the house, and a place for the camels.”
32 Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
So the man came to the house and he unloaded the camels. The camels were given straw and feed, and water was provided to wash his feet and the feet of the men who were with him.
33 Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
They set food before him to eat, but he said, “I will not eat until I have said what I have to say.” So Laban said, “Speak on.”
34 Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
He said, “I am Abraham's servant.
35 Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
Yahweh has blessed my master very much and he has become great. He has given him flocks and herds, silver and gold, male servants and female servants, and camels and donkeys.
36 Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
Sarah, my master's wife, bore a son to my master when she was old, and he has given everything that he owns to him.
37 Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
My master made me swear, saying, 'You must not get a wife for my son from the daughters of the Canaanites, in whose land I make my home.
38 koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
Instead, you must go to my father's family, and to my relatives, and get a wife for my son.'
39 “Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
I said to my master, 'Perhaps the woman will not follow me.'
40 “Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
But he said to me, 'Yahweh, before whom I walk, will send his angel with you and he will prosper your way, so that you will get a wife for my son from among my relatives and from my father's family line.
41 Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
But you will be free from my oath if you come to my relatives and they will not give her to you. Then you will be free from my oath.'
42 “Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
So I arrived today at the spring, and said, 'O Yahweh, God of my master Abraham, please, if you do indeed intend to make my journey successful—
43 taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
here I am, standing by the spring of water—let the young woman who comes out to draw water, the woman to whom I say, “Please give me a little water from your pitcher to drink,”
44 ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
the woman who says to me, “Drink, and I will also draw water for your camels”—let her be the woman whom you, Yahweh, have chosen for my master's son.'
45 “Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
Even before I had finished speaking in my heart, behold, Rebekah came out with her pitcher on her shoulder and she went down to the spring and drew water. So I said to her, 'Please give me a drink.'
46 “Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
She quickly lowered her pitcher from her shoulder and said, 'Drink, and I will give your camels water also.' So I drank, and she watered the camels also.
47 “Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
I asked her and said, 'Whose daughter are you?' She said, 'The daughter of Bethuel, Nahor's son, whom Milkah bore to him.' Then I put the ring in her nose and the bracelets on her arms.
48 kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
Then I bowed down and worshiped Yahweh, and blessed Yahweh, the God of my master Abraham, who had led me by the right way to find the daughter of my master's relative for his son.
49 Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
Now therefore, if you are prepared to show covenant faithfulness and trustworthiness to my master, tell me. But if not, tell me, so that I may turn to the right hand or to the left.”
50 Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
Then Laban and Bethuel answered and said, “The thing has come from Yahweh; we cannot speak to you either bad or good.
51 Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
Look, Rebekah is before you. Take her and go, so she may be the wife of your master's son, as Yahweh has spoken.”
52 Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
When Abraham's servant heard their words, he bowed himself down to the ground to Yahweh.
53 Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
The servant brought out articles of silver and articles of gold, and clothing, and gave them to Rebekah. He also gave precious gifts to her brother and to her mother.
54 Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
Then he and the men who were with him ate and drank. They stayed there overnight, and when they arose in the morning, he said, “Send me away to my master.”
55 Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
Her brother and her mother said, “Let the young woman stay with us for a few more days, at least ten. After that she may go.”
56 Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
But he said to them, “Do not hinder me, since Yahweh has prospered my way. Send me on my way so that I may go to my master.”
57 Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
They said, “We will call the young woman and ask her.”
58 Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
So they called Rebekah and asked her, “Will you go with this man?” She replied, “I will go.”
59 Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
So they sent their sister Rebekah, along with her female servant, on her journey with Abraham's servant and his men.
60 Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
They blessed Rebekah, and said to her, “Our sister, may you be the mother of thousands of ten thousands, and may your descendants possess the gate of those who hate them.”
61 Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
Then Rebekah arose, and she and her servant girls mounted the camels, and followed the man. Thus the servant took Rebekah, and went his way.
62 Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
Now Isaac was living in the Negev, and had just returned from Beer Lahai Roi.
63 Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
Isaac went out to meditate in the field in the evening. When he looked up and saw, behold, there were camels coming!
64 Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
Rebekah looked, and when she saw Isaac, she jumped down from the camel.
65 nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
She said to the servant, “Who is that man who is walking in the field to meet us?” The servant said, “It is my master.” So she took her veil, and covered herself.
66 Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
The servant recounted to Isaac all the things that he had done.
67 Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.
Then Isaac brought her into his mother Sarah's tent and took Rebekah, and she became his wife, and he loved her. So Isaac was comforted after his mother's death.

< Genesis 24 >