< Genesis 24 >

1 Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
Ibrahim noseti kendo hike noniangʼ, kendo Jehova Nyasaye nosegwedhe e yore duto.
2 Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
Nowacho ne jatichne maduongʼ mane rito gige ode duto niya, “Ket lweti e kind ema.
3 Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
Adwaro mondo ikwongʼrina gi nying Jehova Nyasaye, Nyasach polo kod piny ni ok ibi yudone wuoda dhako koa kuom nyi Kanaan ma an jadak e kindgini,
4 koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
to ibiro dhi thurwa kendo ir wedena mondo iyudne wuoda Isaka dhako.”
5 Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
Jatichne nopenje niya, “Datim angʼo ka nyakono ok oyie biro koda e pinyni? Dadwok wuodi thuru kumane iayeno?”
6 Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
Ibrahim nowachone niya, “Nyaka ine ni ok idwoko wuoda kuno.
7 Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
Jehova Nyasaye, ma Nyasach polo mane ogola thurwa e dala wuora kendo nowuoyo koda kotimo koda singruok ni, ‘To ne nyikwayi nami pinyni’ kendo en owuon ema obiro oro malaikane nyimi mondo mi iyudne wuoda dhako kuno.
8 Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
To ka nyakono ok dwar biro kodi, eka inibed thuolo kuom singruok ma atimo kodini. Ne mana ni ok idwoko wuoda kuno.”
9 Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
Omiyo jatijeno noketo lwete e kind em ruodhe Ibrahim kendo notimo singruok kode e wachni.
10 Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
Eka jatijeno nokawo ngamia apar mag ruodhe, kod chiwo duto mabeyo mochako wuoth kodhi Aram-Naharaim (tiende ni, Mesopotamia) koluwo yo madhi dala matin mar Nahor.
11 Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
Noketo ngamia onindo piny machiegni gi soko but dala; ne en kar angʼich welo, seche mamon dhi umbo.
12 Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
Eka nolemo niya, “Yaye Jehova Nyasaye Nyasach ruodha Ibrahim, gwedha kawuono, kendo nyis ngʼwononi ne ruodha Ibrahim.
13 Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
Ne, koro eri achungo e bath sokoni, kama nyi dalani biro umboe pi.
14 Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
Mad timreni ka awachone nyako moro ni, ‘Asayi, yie dapigi piny mondo mi amodhie,’ kendo ka dowachna ni, ‘modhi kendo abiro chiwo pi ni ngamia-gi duto’ to en ema mondo obed nyako ma iseyierone Isaka jatichni. Kamano anangʼe ni isenyiso ngʼwononi ne ruodha.”
15 Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
Kane pok otieko lemo, Rebeka notucho kotingʼo dapige e goke. Ne en nyar Bethuel wuod Milka, mane chi Nahor owadgi Ibrahim.
16 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
Nyakoni ne en jaber man-gi chia, mapok ongʼeyo dichwo! Nolor e soko, motwomo pi eka odwogo.
17 Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
Jatich Ibrahim noringo kadhi romone mi owachone niya, “Akwayi, yie imiyae pi mondo amodhi.”
18 Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
Eka nowacho niya, “Modhi, ruodha” kendo mapiyo nono noloro dapi e lwete momiye pi omodho.
19 Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
Bangʼ kane osemiye pi modho, nowachone niya, “Abiro dhi umbo pi ne ngamia magi bende, nyaka gitiek modho.”
20 Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
Omiyo noloko pi mapiyo nono e besen, moringo odok e soko omo pi kendo noomo moromo ngamiagego duto.
21 Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
Jatich Ibrahim nolingʼ thi ma ok owuoyo, karange lingʼ-lingʼ mondo one ane ka Jehova Nyasaye osegwedho wuodhe.
22 Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
Kane ngamia-go osetieko modho, ngʼatno nogolo tere mar um mar dhahabu ma pekne romo achiel kuom apar mar kilo kod bangli ariyo mag dhahabu mapekgi oromo nus kilo.
23 Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
Eka nopenje niya, “In nyar ngʼa? Yie inyisa bende dwayudie kar nindo dalau?”
24 Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
Nodwoke niya, “An nyar Bethuel, ma wuod Nahor gi Milka.”
25 Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
Kendo nomedo wacho niya, “Wan kod lum kod chiemb ngamia mangʼeny kaachiel gi ot ma unyalo nindoe.”
26 Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
Ngʼatno nopodho auma molamo Jehova Nyasaye,
27 nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
kowacho niya, “Duongʼ odogne Jehova Nyasaye, ma Nyasach ruodha Ibrahim, ma ok oseweyo nyiso adierane gi ngʼwonone ne ruodha. To an, Jehova Nyasaye osetelona e wuoth nyaka e od wede ruodha.”
28 Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
Nyakono noringo modhi onyiso joodgi duto gik mane osetimorene.
29 Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
Rebeka ne nigi owadgi miluongo ni Laban, kendo Laban noringo matek ka dhi ir ngʼatno mane ni e sokono.
30 Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
Kane Laban oseneno tere e um nyamin kod bangli ka ni e lwet nyamin kendo kane owinjo gima Rebeka wacho ni ngʼatno onyise, Laban nodhi ir ngʼatno moyude ka ochungʼ e bath ngamia-go machiegni gi soko.
31 Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
Laban nowachone niya, “Bi, in ngʼama Jehova Nyasaye ogwedho. Angʼo ma omiyo ichungʼ oko ka? Aseikoni ot kendo nitie kar ngamia bende.”
32 Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
Kuom mano ngʼatno nodonjo e ot kendo misike mane ngamia otingʼo nogol kuomgi. Nomigi lum kod chiembgi mi nokelo pi ne jatich Ibrahim kod joge mondo olwokgo tiendegi.
33 Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
Eka nokel chiemo ne jatich Ibrahim to nowachonegi niya, “Ok abi chiemo kapok anyisou gima onego awachnu.” Laban nowachone niya, “Kara nyiswa.”
34 Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
Kuom mano nowacho niya, “An jatich Ibrahim.
35 Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
Jehova Nyasaye osegwedho ruodha ahinya kendo osebedo jamoko. Osemiye rombe kod dhok, fedha kod dhahabu, jotich machwo kod mamon gi ngamia kod punde.
36 Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
Sara, jaod ruodha osenywolone wuowi ka hike oniangʼ kendo ruodha osemiyo wuodeno mwandune duto.
37 Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
Ruodha nomiyo akwongʼora kowacho ni, ‘Kik iyudne wuoda nyako kuom nyi Kanaan ma adakie lopgini,
38 koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
to dhi e dala wuora kendo ir anywolana kendo iyudne nyako ne wuoda.’
39 “Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
“Eka ne apenjo ruodha ni, ‘Datim nangʼo ka nyakono ok oyie biro koda?’
40 “Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
“Nodwoke ni, ‘Jehova Nyasaye, ma asebedo ka awuotho e nyime biro ori gi malaikane kendo obiro gwedho wuodhi, mondo mi iyudne wuoda nyako moa kuom anywolana kendo e od wuora.
41 Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
Ka idhi michopo ir jowa to singruogni ok nomaki, to bende ka gitamore miyi nyakono mondo ibigo, to kwongʼruokni ok nobed e wiyi.’
42 “Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
“Kane abiro e soko kawuono, nawacho ni, ‘Yaye Jehova Nyasaye, Nyasach ruodha Ibrahim, kalongʼoni, to gwedh wuodhani.
43 taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
Ne, koro eri achungo e bath sokoni, ka jatich ma nyako obiro omo pi kendo awachone niya, “Yaye miyae pi amodhi,”
44 ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
kendo ka owachona niya, “Modhi, kendo abiro omo pi nyaka ne ngamia-gi bende,” to en ema mondo obed nyako ma Jehova Nyasaye oseyiero ne wuod ruodha.’
45 “Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
“Kane pok atieko lemo e chunya, Rebeka nochopo ka otingʼo dapi e goke. Nolor e soko mondo otuom pi kendo nawachone ni, ‘Yaye miyae pi amodhi.’
46 “Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
“Piyo piyo nono noyieyo pi piny mi owacho ni, ‘Modhi kendo abiro miyo ngamia magi bende pi.’ Kuom mano namodho, kendo ngamia bende nomodho.
47 “Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
“Napenje ni, ‘In nyar ngʼa?’ “En to nodwoka ni, ‘An nyar Bethuel, wuod Nahor gi Milka.’ “Eka ne aketo tere e ume gi bangli e lwete,
48 kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
kendo napodho auma kalamo Jehova Nyasaye. Namiyo Jehova Nyasaye ma Nyasach ruodha Ibrahim duongʼ, mane telona e yo maber mayudo nyako ma nyakwar owad gi ruodha ne wuode.
49 Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
Koro nyisauru kuyie timo ngʼwono kod adieri ne ruodha; to ka ok kamano to nyisa mondo mi angʼe kuma achomo.”
50 Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
Laban kod Bethuel nodwoke niya, “Ma-oa kuom Jehova Nyasaye ok wanyal wachoni gimoro amora.
51 Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
Rebeka eri; kawe mondo udhi, kendo obed chi wuod ruodhi, mana kaka Jehova Nyasaye osechiko.”
52 Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
Kane jatich Ibrahim owinjo gima negiwacho, nopodho auma e nyim Jehova Nyasaye.
53 Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
Eka jatich Ibrahim nogolo gik moko mag dhahabu kod mag fedha kod lewni mi nomiyogi Rebeka; kendo nochiwo mich ma nengogi tek ne owadgi kod min-gi.
54 Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
Eka jatich Ibrahim kod jogo mane ni kode nochiemo kendo ometho kendo ne ginindo kanyo. Kane gichiewo kinyne gokinyi nowacho niya, “Weuru adog ir ruodha.”
55 Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
To owad gi Rebeka kod min-gi nodwoke niya, “We nyakoni odongʼ kodwa kuom ndalo apar kata moloyo kanyo; eka udhi.”
56 Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
To jatich Ibrahim nowachonegi niya, “Kik ugengʼna, to weyauru adog ir ruodha, nikech Jehova Nyasaye osegwedho wuodha.”
57 Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
Eka negiwacho niya, “We waluong nyako mondo wapenje kuom wachni.”
58 Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
Kuom mano negiluongo Rebeka kendo gipenje niya, “Inyalo dhi gi ngʼatni?” Rebeka nodwokogi niya, “Abiro dhi.”
59 Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
Kuom mano ne giweyo Rebeka odhi kaachiel gi nyako mane opire kod jatich Ibrahim gi joge.
60 Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
Kendo negigwedho Rebeka kagiwachone niya, “Nyathiwa, bed min ji gana gi gana; mad nyikwayi medre ma kaw mier madongo mag wasikgi.”
61 Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
Eka Rebeka kod jotije ma nyiri noikore moidho ngamia-gi mi gidhi gi jatich Ibrahim. Kuom mano jatich Ibrahim nokawo Rebeka kendo gidhi.
62 Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
Noyudo ka koro Isaka oa Beer-Lahai-Roi, nikech noyudo odak Negev.
63 Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
Ka noyudo owuotho e pap godhiambo chiengʼ moro ka owuoyo gi Nyasaye, kendo kane orango malo, noneno ngamia kabiro.
64 Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
Rebeka bende norango malo moneno Isaka. Nolor piny koa ewi ngamia
65 nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
kendo nopenjo jatich Ibrahim niya, “Macha en ngʼa manie pap mabiro romonwa cha?” Jatich nodwoke niya, “En ruodha.” Eka nokawo nanga ma oumogo wangʼe.
66 Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
Eka jatich nonyiso Isaka gik moko duto mane osetimo.
67 Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.
Isaka notero Rebeka e hemb Sara min-gi, kendo Isaka nokendo Rebeka. Kuom mano Rebeka nobedo chi Isaka, kendo Isaka nohero Rebeka gihera mamalo; kendo Isaka ne ok obedo gi parruok bangʼ tho min mare.

< Genesis 24 >