< Genesis 23 >
1 Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
Or Sara vécut cent vingt-sept ans.
2 Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
Et elle mourut dans la ville d’Arbée, qui est Hébron, dans la terre de Chanaan; et Abraham vint pour faire le deuil et pour la pleurer.
3 Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
Et lorsqu’il se fut levé après les devoirs funéraires, il parla aux fils de Heth, disant:
4 “Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
Je suis parmi vous étranger et voyageur: donnez-moi le droit de sépulture chez vous, afin que j’ensevelisse mon mort.
5 Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
Les fils de Heth répondirent, disant:
6 “Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
Ecoute-nous, seigneur, tu es un prince de Dieu au milieu de nous; ensevelis ton mort dans le plus beau de nos sépulcres; nul ne pourra t’empêcher d’ensevelir ton mort dans son tombeau.
7 Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
Abraham se leva, et se prosterna devant le peuple de ce pays, c’est-à-dire, les fils de Heth;
8 nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
Et il leur dit: S’il plaît à votre âme que j’ensevelisse mon mort, écoutez-moi et intercédez pour moi auprès d’Ephron, fils de Séor,
9 kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
Afin qu’il me donne la caverne double qu’il a à l’extrémité de son champ; que pour un prix convenable, il me la livre devant vous, afin que j’y possède un sépulcre.
10 Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
Or, Ephron habitait au milieu des fils de Heth. Ephron répondit donc à Abraham, devant tous ceux qui entraient à la porte de la ville, disant:
11 nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
Non, il n’en sera pas ainsi, mon seigneur; mais toi, écoute plutôt ce que je dis: Je te livre le champ et la caverne qui est dans ce champ, en présence des fils de mon peuple; ensevelis ton mort.
12 Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
Abraham se prosterna devant le peuple de ce pays,
13 ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
Et dit à Ephron, le peuple l’environnant: Je te prie de m’écouter; je donnerai l’argent pour le champ; prends-le, et ainsi j’y ensevelirai mon mort.
14 Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
Et Ephron répondit:
15 “Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
Mon seigneur, écoute-moi: la terre que tu demandes vaut quatre cents sicles d’argent; c’est le prix entre moi et toi; mais qu’est-ce que cela? ensevelis ton mort.
16 Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
Ce qu’Abraham ayant entendu, il fit peser l’argent qu’Ephron avait demandé, en présence des fils de Heth, quatre cents sicles d’argent en monnaie de bon aloi et ayant cours.
17 Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
Et le champ jadis d’Ephron, dans lequel était une caverne double, en face de Mambré, aussi bien que la caverne et tous les arbres qui bordaient le champ de tous côtés, fut assuré
18 kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
A Abraham comme propriété sous les yeux des fils de Heth et de tous ceux qui entraient à la porte de la ville.
19 Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
Et ainsi Abraham ensevelit Sara sa femme dans la caverne double du champ, en face de Mambré; c’est Hébron, dans la terre de Chanaan.
20 Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.
Le champ donc et la caverne qui étaient dans le champ furent assurés à Abraham comme propriété de tombeau, par les fils de Heth.