< Genesis 23 >

1 Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
Sara was an hundred and. xxvij. yere olde (for so longe lyued she)
2 Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
and than dyed in a heade cyte called Hebron in the londe of Canaan. Than Abraham came to morne Sara and to wepe for her.
3 Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
And Abraham stode vp from the coorse and talked with the sonnes of heth saynge:
4 “Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
I am a straunger ad a foryner amonge yow geue me a possession to bury in with you that I may bury my dead oute of my sighte.
5 Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
And the children of heth answered Abraham saynge vnto him:
6 “Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
heare vs lorde thou art a prynce of God amonge vs. In the chefest of oure sepulchres bury thy dead: None of vs shall forbydd ye his sepulchre yt thou shuldest not bury thy deade therein.
7 Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
Abraha stode vp and bowed hi selfe before ye people of ye lade ye childre of heth.
8 nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
And he comoned with them saynge: Yf it be youre myndes yt I shall bury my deade oute of my sighte heare me ad speke for me to Ephron the sonne of Zoar:
9 kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
and let him geue me the dubill caue which he hath in the end of his felde for as moch money as it is worth let him geue it me in the presence of you for a possession to bury in.
10 Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
For Hephron dwelled amoge ye childern of heth. Than Ephron the Hethite answered Abraham in the audyece of the childern of Heth and of all that went in at the gates of his cyte saynge:
11 nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
Not so my lorde but heare me: The felde geue I the and the caue that therein is geue I the also And even in the presence of the sonnes of my people geve I it the to bury thy deede in.
12 Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
Than Abraham bowed himselfe before the people of the lade
13 ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
and spake vnto Ephro in the audyence of the people of the contre saynge: I praye the heare me I will geue sylver for the felde take it of me ad so will I bury my deed there.
14 Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
Ephron answered Abraha saynge vnto him
15 “Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
My lorde harken vnto me. The lande is worth iiij. hundreth sycles of syluer: But what is that betwixte the and me? bury thy deede.
16 Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
And Abraham harkened vnto Ephron and weyde him the sylver which he had sayde in the audyence of the sonnes of Heth. Euen. iiij. hudred syluer sycles of currant money amonge marchauntes
17 Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
Thus was the felde of Ephron where in the dubbill caue is before Mamre: euen the felde and the caue that is therein and all the trees of the felde which growe in all the borders rounde aboute made sure
18 kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
vnto Abraham for a possession in the syghte of the childern of Heth and of all that went in at the gates of the cyte.
19 Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
And then Abraham buried Sara his wyfe in the double caue of the felde that lyeth before Mare otherwise called Ebron in the lande of Canaan.
20 Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.
And so both the felde ad the caue that is therein was made vnto Abraham a sure possession to bury in of the sonnes of Heth.

< Genesis 23 >