< Genesis 23 >

1 Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
Sara levede 127 År, så mange var Saras Leveår.
2 Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
Sara døde i Kirjat Arba, det er Hebron, i Kana'ans Land. Så gik Abraham hen og holdt Klage over Sara og begræd hende.
3 Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
Og da han havde rejst sig fra sin døde, talte han således til Hetiterne:
4 “Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
"Jeg er Gæst og fremmed hos eder; men giv mig et Gravsted hos eder, så jeg kan jorde min døde og bringe hende bort fra mit Ansigt!"
5 Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
Da svarede Hetiterne Abraham:
6 “Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
"Hør os, Herre! En Guds Fyrste er du jo iblandt os; jord du din døde i en af vore bedste Grave! Ikke en af os vil nægte dig sin Grav og hindre dig i at jorde din døde."
7 Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
Men Abraham stod op og bøjede sig for Hetiterne, Folkene der på Stedet,
8 nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
og sagde til dem: "Hvis I samtykker i, at jeg jorder min døde og bringer hende bort fra mit Ansigt, så føj mig i at lægge et godt Ord ind for mig hos Efron, Zohars Søn,
9 kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
så han giver mig sin Klippehule i Makpela ved Udkanten af sin Mark; for fuld Betaling skal han i eders Nærværelse give mig den til Gravsted!"
10 Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
Men Efron sad blandt Hetiterne; og Hetiten Efron svarede Abraham i Hetiternes Påhør, så mange som gik ind gennem hans Bys Port:
11 nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
"Gid min Herre vilde høre mig! Marken giver jeg dig, og Hulen derpå giver jeg dig; i mit Folks Nærværelse giver jeg dig den; jord du kun din døde!"
12 Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
Da bøjede Abraham sig for Folkene der på Stedet
13 ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
og sagde til Efron i deres Påhør: "Om du blot - gid du dog vilde høre mig! Jeg giver dig, hvad Marken er værd; modtag det dog af mig, så jeg kan jorde min døde der."
14 Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
Da sagde Efron til Abraham:
15 “Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
"Gid min Herre vilde høre mig! Et Stykke Land til 400 Sekel Sølv, hvad har det at sige mellem mig og dig? Jord du kun din døde!"
16 Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
Og Abraham forstod Efron og tilvejede ham den Sum, han havde nævnet i Hetiternes Påhør, 400 Sekel Sølv i gangbar Mønt.
17 Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
Således gik Efrons Mark i Makpela over for Mamre i hele sin Udstrækning tillige med Klippehulen og alle Træerne på Marken
18 kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
over i Abrahams Eje i Hetiternes Næværelse, så mange som gik ind gennem hans Bys Port.
19 Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
Derefter jordede Abraham sin Hustru Sara i Klippehulen på Makpelas Mark over for Mamre, det er Hebron, i Kana'ans Land.
20 Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.
Og Marken med Klippehulen derpå gik fra Hetiterne over til Abraham som Gravsted.

< Genesis 23 >