< Genesis 22 >
1 Nthawi ina zitatha izi, Mulungu anamuyesa Abrahamu. Iye anati, “Abrahamu!” Ndipo iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
Efter disse Begivenheder satte Gud Abraham på Prøve og sagde til ham: "Abraham!" Han svarede: "Se, her er jeg!"
2 Ndipo Mulungu anati, “Tenga Isake, mwana wako yekhayo amene umamukonda ndi kupita naye ku dziko la Moriya. Ukamupereke iye ngati nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri a kumeneko limene ndidzakuwuza.”
Da sagde han: "Tag din Søn Isak, din eneste, ham, du elsker, og drag hen til Morija Land. og bring ham der som Brændoffer på et af Bjergene, som jeg vil vise dig!"
3 Abrahamu anadzuka mmamawa wake namangirira chokhalira pa bulu. Atadula nkhuni zokwanira zowotchera nsembe yopsereza, Abrahamu, antchito ake awiri pamodzi ndi Isake ananyamuka kupita kumalo kumene Mulungu anamuwuza Abrahamu.
Da sadlede Abraham tidligt næste Morgen sit Æsel, tog to af sine Drenge og sin Søn Isak med sig, og efter at have kløvet Offerbrænde gav han sig på Vandring; til det Sted, Gud havde sagt ham.
4 Pa tsiku lachitatu, Abrahamu anakweza maso ake ndipo anaona malowo chapatali.
Da Abraham den tredje Dag så. op, fik han Øje på Stedet langt borte.
5 Ndipo Abrahamu anati kwa antchito ake aja, “Bakhalani pano ndi buluyu. Ine ndi mnyamatayu tipita uko kukapemphera, koma tibweranso.”
Så sagde Abraham til sine Drenge: "Bliv her med Æselet, medens jeg og Drengen vandrer der. hen for at tilbede; så kommer vi tilbage til eder."
6 Abrahamu anatenga nkhuni za nsembe yopsereza zija namusenzetsa mwana wake Isake, ndipo iye mwini anatenga moto ndi mpeni. Pamene awiriwo amayendera pamodzi,
Abraham tog da Brændet til Brændofferet og lagde, det på sin Søn Isak; selv tog han Ilden og Offerkniven, og så gik de to sammen.
7 Isake anati kwa abambo ake Abrahamu, “Abambo?” Abrahamu anayankha, “Ee mwana wanga.” Isake anafunsa, “Moto ndi nkhuni zilipo, koma nanga mwana wankhosa wa nsembe yopsereza ali kuti?”
Da sagde Isak til sin Fader Abraham: "Fader!" Han svarede: "Ja. min Søn!" Da sagde han: "Her er Ilden og Brændet, men hvor er Dyret til Brændofferet?"
8 Abrahamu anayankha, “Mwana wanga, Mulungu adzipezera yekha mwana wankhosa wa nsembe yopsereza.” Ndipo awiriwo anapitiriza ulendo.
Abraham svarede: "Gud vil selv udse sig Dyret til Brændofferet, min Søn!" Og så gik de to sammen.
9 Atafika pamalo pamene Mulungu anamuwuza paja, Abrahamu anamangapo guwa lansembe nayika nkhuni pamwamba pa guwapo. Kenaka anamumanga mwana wake Isake namugoneka paguwapo, pamwamba pa nkhuni paja.
Da de nåede det Sted, Gud havde sagt ham, byggede Abraham der et Alter og lagde Brændet til Rette; så bandt han sin Søn Isak og lagde ham på Alteret oven på Brændet.
10 Kenaka Abrahamu anatambasula dzanja lake natenga mpeni kuti aphe mwana wake.
Og Abraham greb Kniven og rakte Hånden ud for at slagte sin Søn.
11 Koma mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba nati, “Abrahamu! Abrahamu!” Iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
Da råbte HERRENs Engel til ham fra Himmelen: "Abraham, Abraham!" Han svarede: "Se, her er jeg!"
12 Mngeloyo anati, “Usatambasulire mwanayo dzanja lako kuti umuphe, pakuti tsopano ndadziwa kuti iwe umaopa Mulungu. Iwe sunandimane mwana wako mmodzi yekhayo.”
Da sagde Engelen: "Ræk ikke din Hånd ud mod Drengen og gør ham ikke noget; thi nu ved jeg, at du frygter Gud og end ikke sparer din Søn, din eneste, for mig!"
13 Abrahamu anatukula maso ake ndipo anaona nkhosa yamphongo itakoledwa ndi nyanga zake mu ziyangoyango. Iye anapita nakatenga nkhosa ija ndikuyipha ngati nsembe yopsereza mʼmalo mwa mwana wake.
Og da Abraham nu så op, fik han bag ved sig Øje på en Væder, hvis Horn havde viklet sig ind i de tætte Grene; og Abraham gik hen og tog Væderen og ofrede den som Brændoffer i sin Søns Sted.
14 Choncho Abrahamu anatcha malo amenewa kuti Yehova-Yire (Wopereka). Ndipo mpaka lero amatchula malowo kuti ndi “Pa phiri la Yehova wopereka.”
Derfor kaldte Abraham dette Sted: HERREN udser sig, eller, som man nu til dags siger: Bjerget, hvor HERREN viser sig.
15 Mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba kachiwiri
Men HERRENs Engel råbte atter til Abraham fra Himmelen:
16 ndipo anati, “Ndikulumbira mwa Ine ndekha kuti popeza wachita zimenezi, wosandikaniza mwana wako mmodzi yekhayu,
"Jeg sværger ved mig selv, lyder det fra HERREN: Fordi du har gjort dette og ikke sparet din Søn, din eneste, for mig,
17 ndidzakudalitsa ndithu ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati nyenyezi zamlengalenga komanso ngati mchenga wa mʼmphepete mwa nyanja. Zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo,
så vil jeg velsigne dig og gøre dit Afkom talrigt som Himmelens Stjerner og Sandet ved Havets Bred; og dit Afkom skal tage sine Fjenders Porte i Besiddelse;
18 ndipo kudzera mwa chidzukulu chako, mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi idzadalitsika, chifukwa iwe wandimvera.”
og i din Sæd skal alle Jordens Folk velsignes, fordi du adlød mig!"
19 Kenaka Abrahamu anabwerera kumene anasiya antchito ake kuja nanyamukira nawo pamodzi kupita ku Beeriseba. Ndipo Abrahamu anakhala ku Beeriseba.
Derpå vendte Abraham tilbage til sine Drenge, og de brød op og tog sammen til Be'ersjeba. Og Abraham blev i Be'ersjeba.
20 Patapita nthawi, Abrahamu anamva kuti, “Milika nayenso anaberekera Nahori, mʼbale wake ana.
Efter disse Begivenheder meldte man Abraham: "Også Milka har født din Broder Nakor Sønner:
21 Woyamba anali Huzi ndipo kenaka mʼbale wake Buzi. Anaberekanso Kemueli, amene anali abambo ake a Aramu.
Uz, hans førstefødte, dennes Broder Buz, Kemuel, Arams Fader,
22 Ana ena ndi Kesede Hazo, Pilidasi, Yidilafi ndi Betueli.”
Kesed, Hazo, Pildasj, Jidlaf og Betuel;
23 Betueli anabereka Rebeka. Milika anaberekera Nahori, mʼbale wake wa Abrahamu, ana aamuna asanu ndi atatu amenewa.
Betuel avlede Rebekka; disse otte har Milka født Abrahams Broder Nakor,
24 Mkazi wake wachiwiri, dzina lake Reuma, anamubaliranso Nahori ana awa: Teba, Gahamu, Tahasi ndi Maaka.
og desuden har hans Medhustru Re'uma født Teba, Gaham, Tahasj og Ma'aka."