< Genesis 21 >

1 Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera.
BAWIPA ni a dei tangcoung e patetlah Sarah koe a pai teh a lawkkam pouh e patetlah Sarah hanelah a sak pouh.
2 Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza.
Hahoi, ahni koe a dei pouh tangcoung e patetlah Cathut ni a khoe pouh e tueng navah Sarah ni camo a vawn teh, a matawng hnukkhu Abraham hanelah tongpa a khe pouh.
3 Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera.
Abraham ni hai a tawn e capa, Sarah ni a khe pouh e hah Isak telah min a phung.
4 Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira.
Hottelah, Cathut ni kâ a poe tangcoung e patetlah Abraham ni a capa Isak hah ataroe hnin navah vuensom a a pouh.
5 Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.
Abraham teh a capa Isak a khe navah kum 100 touh a pha toe.
6 Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.”
Sarah ni hai kai ka panuithainae Cathut ni na poe toe. Hete kamthang ka thai e pueng ni hai kai hoi cungtalah a panui van awh han doeh telah ati.
7 Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”
Sarah ni camo sanu a pânei han telah Abraham koe apinimaw ouk a dei pouh. A matawng torei kai ni ca tongpa ka khe pouh toe telah ati.
8 Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu.
Hottelah, camo a roung takhang teh sanu a pâphei. Sanu a pâphei nah hnin dawk Abraham ni buven pawi kalenpounge a sak.
9 Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka,
Izip tami Hagar capa, Abraham hanelah a khe pouh e ni a panuikhai e hah Sarah ni a hmu.
10 ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”
Hatdawkvah, Abraham koevah, Hete sannu hoi a capa pâlei leih, bangkongtetpawiteh sannu e capa ni ka capa e râw coe thai mahoeh telah atipouh.
11 Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake.
A capa lah ao kecu dawk Abraham hanelah hno ka ru poung lah ao.
12 Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
Hatei Cathut ni Abraham koe, camo hoi na sannu kong dawk hno ka ru lah pouk hanh. Sarah ni a dei e pueng tarawi loe. Bangkongtetpawiteh Isak dawk hoi na catoun telah kaw e lah ao han.
13 Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”
Na sannu e capa dawk hai miphun ka pungdaw sak han. Bangkongtetpawiteh ahni hai na ca doeh telah atipouh.
14 Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.
Hottelah amom vah Abraham a thaw teh vaiyei hoi tuium a la teh Hagar e aloung dawk a patue pouh hnukkhu, camo hoi a ceisak. A cei roi teh Beersheba kahrawngum vah yuengyoe a kâva roi.
15 Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba.
Tuium dawk e tui a baw hnukkhu camo hah buruk rahim a hruek.
16 Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.
Pala vai touh ka sittouh bang hane a cei teh, hnuklah a kangvawi laihoi a tahung hnukkhu, camo due e na hmawt sak hanh loe telah ati. Hottelah hnuklah a kangvawi laihoi a tahung teh puenghoi kacaipounglah a ka.
17 Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo.
Camo lawk Cathut ni a thai teh Cathut kalvantami ni kalvan lahoi Hagar a kaw teh, Hagar bangmaw runae na kâhmo. Taket hanh, camo e lawk Cathut ni a thai toe atipouh.
18 Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”
Thaw nateh camo hah na kut hoi pathaw leih, bangkongtetpawiteh miphun kalen poung lah kacoungsak han telah atipouh.
19 Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.
Cathut ni a mit ang sak teh tuikhu buet touh a hmu. A cei teh tuium dawk yikkawi a do hnukkhu camo a pânei.
20 Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta.
Cathut teh camo koe lah a o, ahni teh a roung takhang teh, kahrawngum vah kho a sak teh moikathaipounge lah ao.
21 Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.
Paran kahrawngum vah kho a sak teh a manu ni a yu lah Izip tami a la pouh.
22 Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita.
Hatnae tueng dawk Abimelek hoi ransahu kaukkung Phikhol ni Abraham koevah, na sak e hno pueng dawk Cathut ni na okhai.
23 Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”
Hatdawkvah Cathut minhmai khet lahoi kai hoi ka capa catoun totouh dumyennae awm laipalah na pahren e patetlah kai hoi na onae ram heh a hawinae ka hmu nahanelah lawk na kam pouh leih telah atipouh.
24 Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”
Abraham ni hai, lawkkam han atipouh.
25 Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda.
Abimelek e a sannaw ni tuikhu a lawp dawkvah Abraham ni Abimelek a yue.
26 Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”
Abimelek ni, hot patet hno ka sak e teh apimaw. Ka panuek hoeh, nang ni hai na dei hoeh. Kai ni hai sahnin totouh ka panuek hoeh atipouh.
27 Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano.
Hottelah, Abraham ni tu hoi maitotan a hrawi teh Abimelek a poe, hahoi kahni touh hoi lawkkamnae a sak roi.
28 Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina,
Abraham ni tuhu dawk e tulaca sari touh alouklah a kapek.
29 ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”
Abimelek ni Abraham koevah tulaca sari touh na ka pek e, bang hane maw atipouh.
30 Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”
Ahni ni hete tuikhu ka tai e heh kapanuekkhaikung lah tulaca sari touh e ka kut dawk e na la roeroe han telah atipouh.
31 Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.
Hote hmuen koe kahni touh hoi lawkkamnae a sak roi dawkvah Beersheba telah min a phung.
32 Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti.
Hottelah Beersheba vah lawkkamnae a sak roi hnukkhu Abimelek hoi ransabawi Phikhol tinaw a thaw awh teh Filistin ram lah a ban awh.
33 Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya.
Abraham ni Beersheba vah hmaicakung a ung teh haw vah BAWIPA yungyoe Cathut e min a kaw.
34 Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.
Hahoi, Abimelek teh Filistin ram dawk hnin moi kasawlah a cam.

< Genesis 21 >