< Genesis 20 >
1 Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
And Abraham journeys from there toward the land of the south, and dwells between Kadesh and Shur, and sojourns in Gerar;
2 ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
and Abraham says concerning his wife Sarah, “She is my sister”; and Abimelech king of Gerar sends and takes Sarah.
3 Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
And God comes to Abimelech in a dream of the night and says to him, “Behold, you [are] a dead man, because of the woman whom you have taken—and she married to a husband.”
4 Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
And Abimelech has not drawn near to her, and he says, “Lord, do you also slay a righteous nation?
5 Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
Has he not himself said to me, She [is] my sister! And she, even she herself, said, He [is] my brother; in the integrity of my heart, and in the innocence of my hands, I have done this.”
6 Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
And God says to him in the dream, “Indeed, I have known that in the integrity of your heart you have done this, and I withhold you, even I, from sinning against Me, therefore I have not permitted you to come against her;
7 Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
and now send back the man’s wife, for he [is] inspired, and he prays for you, and you live; and if you do not send back, know that dying you die, you and all that you have.”
8 Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
And Abimelech rises early in the morning, and calls for all his servants, and speaks all these words in their ears; and the men fear exceedingly;
9 Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
and Abimelech calls for Abraham and says to him, “What have you done to us? And what have I sinned against you, that you have brought on me, and on my kingdom, a great sin? Works which are not done you have done with me.”
10 Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
Abimelech also says to Abraham, “What have you seen that you have done this thing?”
11 Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
And Abraham says, “Because I said, Surely the fear of God is not in this place, and they have slain me for the sake of my wife;
12 Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
and also, she is truly my sister, daughter of my father, only not daughter of my mother, and she becomes my wife;
13 Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
and it comes to pass, when God has caused me to wander from my father’s house, that I say to her, This [is] your kindness which you do with me: at every place to where we come, say of me, He [is] my brother.”
14 Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
And Abimelech takes sheep and oxen, and servants and handmaids, and gives to Abraham, and sends back his wife Sarah to him;
15 Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
and Abimelech says, “Behold, my land [is] before you, where it is good in your eyes, dwell”;
16 Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
and to Sarah he has said, “Behold, I have given one thousand pieces of silver to your brother; behold, it is to you a covering of eyes, to all who are with you”; and by all this she is reasoned with.
17 Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
And Abraham prays to God, and God heals Abimelech and his wife, and his handmaids, and they bear:
18 Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.
for YHWH restraining had restrained every womb of the house of Abimelech, because of Sarah, Abraham’s wife.