< Genesis 20 >

1 Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
Te phoeiah Abraham loh Negev kho la puen uh tih Kadesh neh Shur laklo ah kho a sak vaengkah Gerar ah bakuep.
2 ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
Te vaengah Abraham loh a yuu Sarah te ka ngannu ni a ti dongah Gerar manghai Abimelek a tah tih Sarah te a loh.
3 Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
Tedae Abimelek te khoyin a mang ah Pathen loh a paan tih a taengah, “Rhukom tangtae hlang yuu te na rhawt dongah na duek coeng ne,” a ti nah.
4 Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
Te dongah Abimelek loh anih te ben pawh. Tedae, “Boeipa namtom loh dueng cakhaw na ngawn aya?
5 Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
Amah loh kai taengah, 'Anih ka ngannu a ti tih he long khaw ka nganpa ni, ' a ti moenih a? Ka thinko thincaknah neh, ka kut cimcaihnah nen ni he khaw ka saii,” a ti nah.
6 Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
Te dongah anih te a mang ah Pathen loh, “Ue hekah he nang loh thinko thincaknah neh na saii tila ka ming. Tedae anih taek sak ham nang kam paek pawt dongah kai taengah tholh khui lamloh nang te kan tuem kan soem.
7 Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
Tahae ah hlang yuu te mael laeh. Anih te tonghma tih nang ham a thangthui daengah ni na hing eh. Na mael pawt atah na taengkah boeih neh namah khaw na duek rhoe na duek ni tila ming laeh,” a ti nah.
8 Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
Te dongah Abimelek te mincang ah thoo tih a sal boeih te a khue. Te phoeiah hekah olka boeih he amih hna ah a thui hatah hlang boeih loh a rhih uh.
9 Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
Abimelek loh Abraham te a khue tih, “Kaimih ham balae na saii, nang taengah metlam ka tholh tih kamah so neh ka ram ah tholh muep nan khuen. Kai taengah na saii bibi te a saii uh noek moenih,” a ti nah.
10 Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
Te dongah Abimelek loh Abraham te, “Hekah dumlai he na saii vaengah balae na hmuh,” a ti nah.
11 Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
Tedae Abraham loh, “Hekah hmuen ah Pathen hinyahnah om pawt tih ka yuu kah olka ah kai n'ngawn uh ve ka ti dongah ni.
12 Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
Tedae anih te a pa canu ka ngannu rhep ni. A nu canu pawt dae ka yuu lam khaw om ngawn.
13 Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
Te dongah a pa im lamkah Pathen loh kai kho m'hmang sak vaengah anih taengah, 'Nang kah sitlohnah he kai taengah na saii ham atah mekah hmuen boeih ah m'pha cakhaw, 'Anih he ka nganpa ni, 'ti ne tila kamah loh pahoi ka ti nah coeng,” a ti nah.
14 Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
Te vaengah Abimelek loh tu neh saelhung khaw, sal tongpa neh salnu khaw a loh tih Abraham te a paek. A yuu Sarah te khaw amah taengah a mael.
15 Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
Te phoeiah Abimelek loh, “Na mikhmuh kah ka khohmuen aka om he namah mik ah then na ti bangla khosa ngawn ne,” a ti nah.
16 Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
Sarah taengah khaw, “Na nganpa taengah tangka thawngkhat nang ham hmaithennah ka paek coeng tih namah taengkah aka om boeih neh hlang boeih hmaiah na tang uh coeng he,” a ti nah.
17 Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
Tedae Abraham te Pathen taengah thangthui. Pathen loh Abimelek khaw, a yuu khaw, a salnu rhoek khaw a hoeih sak dongah ca a sak uh.
18 Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.
Abraham yuu Sarah kah lai ah Abimelek im kah hlang bung boeih te BOEIPA loh a khaih rhoela a khaih pah.

< Genesis 20 >