< Genesis 2 >

1 Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
Aa le nifonitse ty tane toy naho o likerañeo naho ty fitozantoza’ iareo.
2 Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
Nifoniren’ Añahare ami’ty andro faha-fito i fitoloña’ey, le nitroatse ami’ty andro faha-fito amo hene tolon-draha nanoe’eo;
3 Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
Le nitahien’ Añahare ty andro faha-fito vaho nimasiñe’e, amy te ama’e ro nitroara’e amy ze nitsenèn’ Añahare iaby, hamokara’e ka.
4 Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
Inay ty fanoñonañe o like­rañeo naho ty tane toy amy fañamboarañe iareoy. Tamy sa namboare’ Iehovà Andria­ñahare ty tane toy naho o likerañeoy
5 zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
naho mbe tsy tan-tane ao ze hataen-kivoke naho taolo’ ty nitiria’ ze ahetse am-patrañe ao, vaho mboe tsy nampahavie’ Iehovà Andria­ñahare orañe ty tane, fa tsy teo ty ondaty hahava i taney;
6 koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
fe niboahan-jono ty tane ze nahatondra-drano ty ambone’ ty tane toy iaby;
7 Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
le namboare’ Iehovà Andrianañahare ami’ty lembon-tane t’indaty naho nikofo­ha’e tion-kaveloñe o lalam-pian­tsona’eo vaho ninjare fañova veloñe indatiy.
8 Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
Le nañalahala goloboñe maniñanañe e Edene ao t’Iehovà Andrianañahare, vaho navotra’e ao indaty namboare’ey.
9 Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
Le nampitirie’ Iehovà Andrianañahare boak’ an-tane ao ze karazan-katae soa am-pivazohoañe naho mafiry am-pikamañe, le añivo’ i goloboñey ao ty hataen-kaveloñe naho ty hataem-paharendrehañe ty soa naho ty raty.
10 Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
Nikavavàke boak’ Edene ao ty oñe handeñe i goloboñey, ie boak’ ao le nivaky efatse.
11 Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
Pisone ty añara’ ty valoha’e, mañariari’ i hene tane’ Kavilày, ie amam-bolamena;
12 (Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
soa ty volamena’ i taney; añe ty bedo­lake naho ty vato antsetra.
13 Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
Gihone ty añara’ i oñe faharoe mitsikarioke era’ i tane Kosiy.
14 Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
Hidiklà ty añara’ i fahateloy ze miary atiñana’ i Asore; vaho i Perate t’y oñe fah’efatse.
15 Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
Navotra’ Iehovà Andrianañahare an-Golobo’ i Edene ao indatiy hañalahala naho hañambeñ’ aze.
16 Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
Le hoe ty linili’ Iehovà Andrianañahare am’indatiy, Azo’o ikamañe ze hene hatae amy goloboñey ao;
17 koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
fe ko ikamà’o ty hataem-paharendrehañe ty soa naho ty raty, fa toe hivetrake irehe ami’ty andro ikama’o aze.
18 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
Le hoe t’Iehovà Andrianañahare, Tsy mahasoa indatiy te ho tokañe, hamboarako mpañimba mañeva.
19 Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
Aa le boak’ amo taneo ty namboare’ Iehovà Andrianañahare ze kila bibin-kivoke, naho ze hene voron-tioke vaho nen­dese’e am’ indatiy hivazoho ze sindre ho tokava’ indatiy aze; aa le ze nitokava’ indatiy ty raha veloñe, le izay ty añara’e.
20 Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
Nimea’ indatiy añarañe ze hene hare naho voron-tioke, vaho ze biby am-patrañe añe iaby; fa naho indatiy, tsy nioniñe ty mpañolotse mañeva aze.
21 Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
Aa le nampifetsaha’ Iehovà Andria­nañahare am’indatiy ty rotse miheotse, naho ie nirotse le nafaha’e ty pa’e raike vaho nakite’e amy toe’ey ty nofotse.
22 Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
Nitsene ampela t’Iehovà Andrianañahare amy rinambe’e añ’ila’ indatiy vaho nasese’e am’indatiy.
23 Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
Le hoe indatiy, Itoy henaneo ty taola’ o taolakoo naho ty nofo’ o nofokoo; le hatao Rakemba re amy te lahilahy ro nañakarañe aze.
24 Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
Aa le mienga ty rae’e naho i rene’e t’indaty le mipitek’ ami’ty vali’e vaho nofotse raike iereo.
25 Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.
Ie amy zay, songa nitanjaka indatiy naho i vali’ey fe tsy nimeñatse.

< Genesis 2 >