< Genesis 19 >
1 Angelo awiri aja anafika ku Sodomu madzulo ndipo Loti anali atakhala pansi pa chipata cha mzindawo. Loti atawaona, anayimirira ndi kukakumana nawo ndipo anaweramitsa mutu wake pansi mwaulemu.
I przyszli dwaj Aniołowie do Sodomy w wieczór, a Lot siedział w bramie Sodomskiej. Gdy je tedy ujrzał Lot, wstawszy szedł przeciwko nim, i skłonił się twarzą ku ziemi, i rzekł:
2 Iye anati, “Ambuye wanga, chonde patukirani ku nyumba kwa mtumiki wanu. Mukhoza kusambitsa mapazi anu ndi kugona usiku uno kenaka nʼkumapitirira ndi ulendo wanu mmamawa.” Iwo anati, “Ayi, tigona panja.”
Oto proszę panowie moi, wstąpcie teraz do domu sługi swego, a bądźcie tu na noc, i umyjcie nogi swe; potem rano wstawszy pójdziecie w drogę waszę. Którzy odpowiedzieli: Bynajmniej; ale na ulicy będziemy nocowali.
3 Koma iye anawawumiriza kwambiri kotero kuti anapita naye pamodzi ku nyumba kwake. Anawakonzera chakudya buledi wopanda yisiti ndipo anadya.
Ale on przymuszał ich bardzo, iż się skłonili do niego, i weszli w dom jego; zaczem sprawił im ucztę, i napiekł chleba przaśnego, i jedli.
4 Alendo aja asanapite kogona, amuna onse achinyamata ndi achikulire ochokera mbali zonse za mzinda wa Sodomu anazinga nyumba ya Loti.
Lecz pierwej niż oni poszli spać, oto obywatele miasta, mężowie Sodomscy, obstąpili dom, od młodego aż do starego, wszystek lud zewsząd.
5 Iwo anayitana Loti namufunsa kuti, “Ali kuti amuna aja amene afika kuno usiku womwe uno? Atulutse, utipatse kuti tigone nawo malo amodzi.”
I wołali na Lota, i rzekli mu: Gdzie są mężowie, którzy przyszli do ciebie w nocy? wywiedź je do nas, abyśmy je poznali.
6 Loti anatuluka panja kukakumana nawo natseka chitseko
Tedy wyszedł do nich Lot ze drzwi, i zamknął drzwi za sobą.
7 ndipo anati, “Ayi anzanga, musachite zinthu zoyipa zotere.
I rzekł: Nie czyńcie proszę, bracia moi, nic złego.
8 Taonani, ine ndili ndi ana anga akazi awiri amene sanagonepo ndi mwamuna. Mundilole ndikutulutsireni amenewo ndipo muchite nawo zimene mungafune. Koma musachite chilichonse ndi anthuwa, pakuti iwowa ndi alendo anga ndipo ndiyenera kuwatchinjiriza.”
Oto teraz mam dwie córki, które nie poznały męża; wywiodę je teraz do was, a czyńcie z niemi, co się wam podoba, tylko mężom tym nic nie czyńcie; bo dlatego weszli pod cień dachu mego.
9 Iwo anayankha kuti, “Tachoka apa tidutse.” Ndipo anati, “Munthu uyu anabwera kuno ngati mlendo chabe, tsono lero akufuna kuti akhale wotiweruza! Tikukhawulitsa kuposa iwowa.” Anapitiriza kumuwumiriza Loti uja nʼkumasunthira kutsogolo kuti athyole chitseko.
A oni rzekli: Pójdźże tam; i mówili: Ten sam przyszedł, aby tu gościem był, a miałby nas sądzić? przetoż gorzej uczynimy tobie, niż onym i czynili gwałt wielki mężowi onemu Lotowi, i przystąpili, aby drzwi wyłamali.
10 Koma anthu aja anali mʼkatiwa anasuzumira namukokera Loti uja mʼkati mwa nyumba nʼkutseka chitseko.
Ale mężowie oni, wyciągnąwszy rękę swoję, wwiedli Lota do siebie w dom, i zamknęli drzwi.
11 Kenaka anawachititsa khungu anthu amene anali panja pa nyumba aja, aangʼono ndi aakulu omwe, kuti asaone pa khomo.
A męże one, którzy byli u drzwi domu, pozarażali ślepotą, od najmniejszego, aż do największego; tak, iż się spracowali, szukając drzwi.
12 Anthu awiri aja anati kwa Loti, “Kodi uli ndi wina aliyense pano, kaya ndi akamwini ako, kaya ndi ana ako aamuna kapena aakazi, kapena aliyense mu mzindamu amene ndi anzako? Atulutse onse muno,
Tedy rzekli mężowie oni do Lota: Maszli tu jeszcze kogo, zięcia, albo syny twe, albo córki twoje, i wszystko, co masz w mieście, wyprowadź z miejsca tego.
13 chifukwa tiwononga malo ano. Yehova waona kuti kuyipa kwa anthu a mu mzindawu kwakulitsa. Choncho watituma kuti tiwuwononge.”
Skazimy bowiem to miejsce, przeto, że się wzmógł krzyk ich przed Panem, i posłał nas Pan, abyśmy je skazili.
14 Choncho Loti anatuluka nayankhula ndi akamwini ake amene anali kuyembekezera kukwatira ana ake akazi nati, “Fulumirani, tiyeni tichoke pa malo ano chifukwa Yehova watsala pangʼono kuwononga mzindawu.” Koma akamwini akewo ankayesa kuti akungoselewula.
Tedy wyszedłszy Lot mówił do zięciów swoich, którzy mieli pojąć córki jego, i rzekł: Wstańcie, wynijdźcie z miejsca tego, bo skazi Pan to miasto; ale się zdało w oczach zięciów jego, jakoby żartował.
15 Mmene kumacha, angelo aja anamufulumizitsa Loti nati, “Nyamuka, tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwo, ndipo mutuluke mu mzindawo kuopa kuti mungaphedwe pamodzi nawo.”
A gdy weszła zorza, przymuszali Aniołowie Lota, mówiąc: Wstań, weźmij żonę twoję, i dwie córki twoje, które tu są, byś snać nie zginął w nieprawości miasta tego.
16 Koma Loti ankakayikabe. Koma Yehova anawachitira chifundo motero kuti anthu aja anagwira mkazi wake ndi ana ake aakazi aja nawatsogolera bwinobwino kuwatulutsa mu mzindawo.
A gdy się ociągał, ujęli mężowie oni rękę jego, i rękę żony jego, i rękę dwóch córek jego, ( albowiem mu Pan folgował, ) i wywiedli go, i postawili go przed miastem.
17 Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”
I gdy je wywiedli precz, rzekł jeden: Jeźli chcesz, zachowaj duszę twoję, a nie oglądaj się nazad, ani stawaj na tej wszystkiej równinie; uchodź na górę, byś snać nie zginął.
18 Koma Loti anawawuza kuti, “Ayi, ambuye anga chonde musatero!
A Lot rzekł do nich: Nie tak, proszę, panowie moi;
19 Taonani, Inu mwachitira mtumiki wanu chifundo, ndipo mwaonetsa kukoma mtima kwanu pondipulumutsa. Sindingathawire ku mapiri chifukwa chiwonongekochi chikhoza kundipeza ndisanafike ku mapiriko ndipo ndingafe.
Oto teraz znalazł sługa twój łaskę w oczach twoich, i okazałeś obficie miłosierdzie twoje, któreś uczynił ze mną, zachowawszy duszę moję; aleć ja nie będę mógł ujść na tę górę, by mię snać nie zachwyciło to złe, i umarłbym.
20 Koma, chapafupi pomwepa pali mudzi woti ndikhoza kuthamanga nʼkukafikako. Mundilole ndithawireko, ndi waungʼono kwambiri, si choncho? Mukatero, moyo wanga upulumuka.”
Ale oto tu jest miasto nie daleko, do którego bym uciekł, małeć jest; proszę niech tam ujdę, ( wszak małe jest, ) a będzie żywa dusza moja.
21 Mngeloyo anati kwa iye, “Chabwino, ndavomeranso pempho lako, sindiwononga mudzi ukunenawo.
Tedy rzekł do niego: Oto, i wtem wysłuchałem cię, abym nie wywrócił miasta tego, o któremeś mówił.
22 Koma uthawireko mofulumira chifukwa sindichita kena kalikonse mpaka utafikako.” (Nʼchifukwa chake mudziwo unatchedwa Zowari).
Śpieszże się a uchodź tam, bo nie będę mógł nic uczynić, aż ty tam dojdziesz; przetoż nazwane jest imię miasta onego Zoar.
23 Pamene Loti amafika ku Zowari, nʼkuti dzuwa litatuluka.
Wtem słońce weszło na ziemię, a Lot wszedł do Zoar.
24 Ndiye Yehova anathira sulufule wamoto wochokera kumwamba kwa Yehova pa Sodomu ndi Gomora.
Tedy Pan spuścił jako deszcz na Sodomę i na Gomorrę siarkę i ogień, od Pana z nieba.
25 Kotero, anawononga mizindayo, chigwa chonse pamodzi ndi onse okhala mʼmizindayo. Anawononganso zomera zonse za mʼdzikolo.
I wywrócił miasta one, i wszystkę onę równinę, wszystkie obywatele miast onych, i urodzaje onej ziemi.
26 Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.
I obejrzała się żona jego idąc za nim, a obróciła się w słup solny.
27 Mmawa mwake, Abrahamu ananyamuka nabwerera kumalo kumene anakumana ndi Yehova kuja.
Wstawszy tedy Abraham rano, pospieszył się na ono miejsce, kędy stał przed Panem.
28 Anayangʼana kumunsi ku Sodomu, Gomora ndi ku dziko lonse la ku chigwa, ndipo anaona chiwutsi chikufuka mʼdzikolo ngati chikuchokera mʼngʼanjo.
I spojrzał ku Sodomie i Gomorze, i ku wszystkiej ziemi onej równiny, i obaczył, a oto wychodził dym z onej ziemi, jako dym z pieca.
29 Choncho Mulungu anawononga mizinda ya ku chigwa, koma anakumbukira pemphero la Abrahamu natulutsa Loti ku sulufule ndi moto zimene zinawononga mizinda ya kumene Loti amakhalako.
A gdy wywracał Bóg miasta onej równiny, wspomniał Bóg na Abrahama i wybawił Lota z pośrodku wywrócenia, gdy wywracał one miasta, w których Lot mieszkał.
30 Loti ndi ana ake awiri aakazi anachoka ku Zowari nakakhala ku mapiri, chifukwa amachita mantha kukhala ku Zowari. Iye ndi ana ake awiri ankakhala mʼphanga.
Potem wyszedł Lot z Zoar, i mieszkał na górze, i dwie córki jego z nim, albowiem się bał mieszkać w Zoar; ale mieszkał w jaskini, on i dwie córki jego.
31 Tsiku lina mwana wake wamkazi wamkulu anawuza mngʼono wake kuti, “Abambo athu ndi wokalamba ndipo palibe mwamuna aliyense pano woti atikwatire ndi kubereka ana monga mwa chikhalidwe cha pa dziko lonse lapansi.
Tedy rzekła starsza do młodszej: Ojciec nasz stary a nie masz męża na ziemi, który by wszedł do nas, według zwyczaju wszystkiej ziemi.
32 Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”
Pójdź, upójmy ojca naszego winem, a śpijmy z nim, abyśmy zachowały z ojca naszego nasienie.
33 Usiku umenewo analedzeretsa vinyo abambo awo, ndipo wamkuluyo analowa nagona naye. Abambo awo samadziwa kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
Dały tedy pić ojcu swemu wina onej nocy. I wszedłszy starsza spała z ojcem swym; ale on nie czuł ani kiedy się układła, ani kiedy wstała.
34 Tsiku linali mwana wamkazi wamkulu uja anati kwa mngʼono wake, “Usiku wathawu ine ndinagona ndi abambo anga. Tiye tiwaledzeretsenso vinyo usiku uno ndipo iwe upite ndi kugona nawo ndipo mtundu wathu udzakhalapobe.”
I stało się nazajutrz, że rzekła starsza do młodszej: Otom ja spała przeszłej nocy z ojcem swym, dajmyż mu pić wina jeszcze tej nocy, i wnijdziesz, i będziesz spała z nim, a zachowamy z ojca naszego nasienie.
35 Choncho analedzeranso vinyo abambo awo usiku umenewonso, ndipo mwana wamkazi wamngʼono anapita nagona nawo. Abambo awo sanadziwenso kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
Tedy dały pić i onej nocy ojcu swemu wina; i przyszedłszy młodsza spała z nim; ale on nie czuł, ani kiedy się układła, ani kiedy wstała.
36 Choncho ana onse awiri a Loti aja anatenga pathupi pa abambo awo.
A tak poczęły obie córki Lotowe z ojca swego.
37 Mwana wamkazi wamkulu uja anabereka mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Mowabu. Iyeyo ndiye kholo la Amowabu onse.
I urodziła starsza syna, a nazwała imię jego Moab; ten jest ojcem Moabitów, aż do dnia tego.
38 Mwana wamkazi wamngʼono naye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha iye Beni-Ammi. Iyeyu ndiye kholo la Aamoni onse.
Młodsza też urodziła syna, i nazwała imię jego Benammi; ten jest ojcem synów Ammonowych, aż do dnia tego.