< Genesis 19 >

1 Angelo awiri aja anafika ku Sodomu madzulo ndipo Loti anali atakhala pansi pa chipata cha mzindawo. Loti atawaona, anayimirira ndi kukakumana nawo ndipo anaweramitsa mutu wake pansi mwaulemu.
and to come (in): come two [the] messenger: angel Sodom [to] in/on/with evening and Lot to dwell in/on/with gate Sodom and to see: see Lot and to arise: rise to/for to encounter: meet them and to bow face land: soil [to]
2 Iye anati, “Ambuye wanga, chonde patukirani ku nyumba kwa mtumiki wanu. Mukhoza kusambitsa mapazi anu ndi kugona usiku uno kenaka nʼkumapitirira ndi ulendo wanu mmamawa.” Iwo anati, “Ayi, tigona panja.”
and to say behold please lord my to turn aside: turn aside please to(wards) house: home servant/slave your and to lodge and to wash: wash foot your and to rise (and to go: went *LAH(b)*) to/for way: journey your and to say not for in/on/with street/plaza to lodge
3 Koma iye anawawumiriza kwambiri kotero kuti anapita naye pamodzi ku nyumba kwake. Anawakonzera chakudya buledi wopanda yisiti ndipo anadya.
and to press in/on/with them much and to turn aside: turn aside to(wards) him and to come (in): come to(wards) house: home his and to make to/for them feast and unleavened bread to bake and to eat
4 Alendo aja asanapite kogona, amuna onse achinyamata ndi achikulire ochokera mbali zonse za mzinda wa Sodomu anazinga nyumba ya Loti.
before to lie down: lay down and human [the] city human Sodom to turn: surround upon [the] house: home from youth and till old all [the] people from end
5 Iwo anayitana Loti namufunsa kuti, “Ali kuti amuna aja amene afika kuno usiku womwe uno? Atulutse, utipatse kuti tigone nawo malo amodzi.”
and to call: call out to(wards) Lot and to say to/for him where? [the] human which to come (in): come to(wards) you [the] night to come out: send them to(wards) us and to know [obj] them
6 Loti anatuluka panja kukakumana nawo natseka chitseko
and to come out: come to(wards) them Lot [the] entrance [to] and [the] door to shut after him
7 ndipo anati, “Ayi anzanga, musachite zinthu zoyipa zotere.
and to say not please brother: male-sibling my be evil
8 Taonani, ine ndili ndi ana anga akazi awiri amene sanagonepo ndi mwamuna. Mundilole ndikutulutsireni amenewo ndipo muchite nawo zimene mungafune. Koma musachite chilichonse ndi anthuwa, pakuti iwowa ndi alendo anga ndipo ndiyenera kuwatchinjiriza.”
behold please to/for me two daughter which not to know man to come out: send please [obj] them to(wards) you and to make: do to/for them like/as pleasant in/on/with eye: appearance your except to/for human [the] these not to make: do word: thing for as that: since as as to come (in): come in/on/with shadow beam my
9 Iwo anayankha kuti, “Tachoka apa tidutse.” Ndipo anati, “Munthu uyu anabwera kuno ngati mlendo chabe, tsono lero akufuna kuti akhale wotiweruza! Tikukhawulitsa kuposa iwowa.” Anapitiriza kumuwumiriza Loti uja nʼkumasunthira kutsogolo kuti athyole chitseko.
and to say to approach: approach further and to say [the] one to come (in): come to/for to sojourn and to judge to judge now be evil to/for you from them and to press in/on/with man in/on/with Lot much and to approach: approach to/for to break [the] door
10 Koma anthu aja anali mʼkatiwa anasuzumira namukokera Loti uja mʼkati mwa nyumba nʼkutseka chitseko.
and to send: reach [the] human [obj] hand their and to come (in): bring [obj] Lot to(wards) them [the] house: home [to] and [obj] [the] door to shut
11 Kenaka anawachititsa khungu anthu amene anali panja pa nyumba aja, aangʼono ndi aakulu omwe, kuti asaone pa khomo.
and [obj] [the] human which entrance [the] house: home to smite in/on/with blindness from small and till great: large and be weary to/for to find [the] entrance
12 Anthu awiri aja anati kwa Loti, “Kodi uli ndi wina aliyense pano, kaya ndi akamwini ako, kaya ndi ana ako aamuna kapena aakazi, kapena aliyense mu mzindamu amene ndi anzako? Atulutse onse muno,
and to say [the] human to(wards) Lot still who? to/for you here son-in-law and son: child your and daughter your and all which to/for you in/on/with city to come out: send from [the] place
13 chifukwa tiwononga malo ano. Yehova waona kuti kuyipa kwa anthu a mu mzindawu kwakulitsa. Choncho watituma kuti tiwuwononge.”
for to ruin we [obj] [the] place [the] this for to magnify cry their with face: before LORD and to send: depart us LORD to/for to ruin her
14 Choncho Loti anatuluka nayankhula ndi akamwini ake amene anali kuyembekezera kukwatira ana ake akazi nati, “Fulumirani, tiyeni tichoke pa malo ano chifukwa Yehova watsala pangʼono kuwononga mzindawu.” Koma akamwini akewo ankayesa kuti akungoselewula.
and to come out: come Lot and to speak: speak to(wards) son-in-law his to take: marry daughter his and to say to arise: rise to come out: come from [the] place [the] this for to ruin LORD [obj] [the] city and to be like/as to laugh in/on/with eye: appearance son-in-law his
15 Mmene kumacha, angelo aja anamufulumizitsa Loti nati, “Nyamuka, tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwo, ndipo mutuluke mu mzindawo kuopa kuti mungaphedwe pamodzi nawo.”
and like [the] dawn to ascend: dawn and to hasten [the] messenger: angel in/on/with Lot to/for to say to arise: rise to take: take [obj] woman: wife your and [obj] two daughter your [the] to find lest to snatch in/on/with iniquity: punishment [the] city
16 Koma Loti ankakayikabe. Koma Yehova anawachitira chifundo motero kuti anthu aja anagwira mkazi wake ndi ana ake aakazi aja nawatsogolera bwinobwino kuwatulutsa mu mzindawo.
and to delay and to strengthen: hold [the] human in/on/with hand his and in/on/with hand woman: wife his and in/on/with hand two daughter his in/on/with compassion LORD upon him and to come out: send him and to rest him from outside to/for city
17 Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”
and to be like/as to come out: send they [obj] them [the] outside [to] and to say to escape upon soul: life your not to look after you and not to stand: stand in/on/with all [the] talent [the] mountain: mount [to] to escape lest to snatch
18 Koma Loti anawawuza kuti, “Ayi, ambuye anga chonde musatero!
and to say Lot to(wards) them not please Lord
19 Taonani, Inu mwachitira mtumiki wanu chifundo, ndipo mwaonetsa kukoma mtima kwanu pondipulumutsa. Sindingathawire ku mapiri chifukwa chiwonongekochi chikhoza kundipeza ndisanafike ku mapiriko ndipo ndingafe.
behold please to find servant/slave your favor in/on/with eye: seeing your and to magnify kindness your which to make: do with me me to/for to live [obj] soul: life my and I not be able to/for to escape [the] mountain: mount [to] lest to cleave me [the] distress: harm and to die
20 Koma, chapafupi pomwepa pali mudzi woti ndikhoza kuthamanga nʼkukafikako. Mundilole ndithawireko, ndi waungʼono kwambiri, si choncho? Mukatero, moyo wanga upulumuka.”
behold please [the] city [the] this near to/for to flee there [to] and he/she/it little to escape please there [to] not little he/she/it and to live soul: life my
21 Mngeloyo anati kwa iye, “Chabwino, ndavomeranso pempho lako, sindiwononga mudzi ukunenawo.
and to say to(wards) him behold to lift: kindness face: kindness your also to/for word: thing [the] this to/for lest to overturn I [obj] [the] city which to speak: speak
22 Koma uthawireko mofulumira chifukwa sindichita kena kalikonse mpaka utafikako.” (Nʼchifukwa chake mudziwo unatchedwa Zowari).
to hasten to escape there [to] for not be able to/for to make: do word: thing till to come (in): come you there [to] upon so to call: call by name [the] city Zoar
23 Pamene Loti amafika ku Zowari, nʼkuti dzuwa litatuluka.
[the] sun to come out: (sun)rise upon [the] land: country/planet and Lot to come (in): come Zoar [to]
24 Ndiye Yehova anathira sulufule wamoto wochokera kumwamba kwa Yehova pa Sodomu ndi Gomora.
and LORD to rain upon Sodom and upon Gomorrah brimstone and fire from with LORD from [the] heaven
25 Kotero, anawononga mizindayo, chigwa chonse pamodzi ndi onse okhala mʼmizindayo. Anawononganso zomera zonse za mʼdzikolo.
and to overturn [obj] [the] city [the] these and [obj] all [the] talent and [obj] all to dwell [the] city and branch [the] land: soil
26 Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.
and to look woman: wife his from after him and to be garrison salt
27 Mmawa mwake, Abrahamu ananyamuka nabwerera kumalo kumene anakumana ndi Yehova kuja.
and to rise Abraham in/on/with morning to(wards) [the] place which to stand: stand there with face: before LORD
28 Anayangʼana kumunsi ku Sodomu, Gomora ndi ku dziko lonse la ku chigwa, ndipo anaona chiwutsi chikufuka mʼdzikolo ngati chikuchokera mʼngʼanjo.
and to look upon face: before Sodom and Gomorrah and upon all face: before land: country/planet [the] talent and to see: see and behold to ascend: rise smoke [the] land: country/planet like/as smoke [the] kiln
29 Choncho Mulungu anawononga mizinda ya ku chigwa, koma anakumbukira pemphero la Abrahamu natulutsa Loti ku sulufule ndi moto zimene zinawononga mizinda ya kumene Loti amakhalako.
and to be in/on/with to ruin God [obj] city [the] talent and to remember God [obj] Abraham and to send: depart [obj] Lot from midst [the] overthrow in/on/with to overturn [obj] [the] city which to dwell in/on/with them Lot
30 Loti ndi ana ake awiri aakazi anachoka ku Zowari nakakhala ku mapiri, chifukwa amachita mantha kukhala ku Zowari. Iye ndi ana ake awiri ankakhala mʼphanga.
and to ascend: rise Lot from Zoar and to dwell in/on/with mountain: mount and two daughter his with him for to fear to/for to dwell in/on/with Zoar and to dwell in/on/with cave he/she/it and two daughter his
31 Tsiku lina mwana wake wamkazi wamkulu anawuza mngʼono wake kuti, “Abambo athu ndi wokalamba ndipo palibe mwamuna aliyense pano woti atikwatire ndi kubereka ana monga mwa chikhalidwe cha pa dziko lonse lapansi.
and to say [the] firstborn to(wards) [the] little father our be old and man nothing in/on/with land: country/planet to/for to come (in): come upon us like/as way: conduct all [the] land: country/planet
32 Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”
to go: come! [emph?] to water: drink [obj] father our wine and to lie down: have sex with him and to live from father our seed: children
33 Usiku umenewo analedzeretsa vinyo abambo awo, ndipo wamkuluyo analowa nagona naye. Abambo awo samadziwa kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
and to water: drink [obj] father their wine in/on/with night he/she/it and to come (in): come [the] firstborn and to lie down: have sex [obj] father her and not to know in/on/with to lie down: have sex she and in/on/with to arise: rise she
34 Tsiku linali mwana wamkazi wamkulu uja anati kwa mngʼono wake, “Usiku wathawu ine ndinagona ndi abambo anga. Tiye tiwaledzeretsenso vinyo usiku uno ndipo iwe upite ndi kugona nawo ndipo mtundu wathu udzakhalapobe.”
and to be from morrow and to say [the] firstborn to(wards) [the] little look! to lie down: have sex last night [obj] father my to water: drink him wine also [the] night and to come (in): come to lie down: have sex with him and to live from father our seed: children
35 Choncho analedzeranso vinyo abambo awo usiku umenewonso, ndipo mwana wamkazi wamngʼono anapita nagona nawo. Abambo awo sanadziwenso kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
and to water: drink also in/on/with night [the] he/she/it [obj] father their wine and to arise: rise [the] little and to lie down: have sex with him and not to know in/on/with to lie down: have sex she and in/on/with to arise: rise she
36 Choncho ana onse awiri a Loti aja anatenga pathupi pa abambo awo.
and to conceive two daughter Lot from father their
37 Mwana wamkazi wamkulu uja anabereka mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Mowabu. Iyeyo ndiye kholo la Amowabu onse.
and to beget [the] firstborn son: child and to call: call by name his Moab he/she/it father Moab till [the] day: today
38 Mwana wamkazi wamngʼono naye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha iye Beni-Ammi. Iyeyu ndiye kholo la Aamoni onse.
and [the] little also he/she/it to beget son: child and to call: call by name his Ben-ammi Ben-ammi he/she/it father son: descendant/people Ammon till [the] day: today

< Genesis 19 >