< Genesis 19 >
1 Angelo awiri aja anafika ku Sodomu madzulo ndipo Loti anali atakhala pansi pa chipata cha mzindawo. Loti atawaona, anayimirira ndi kukakumana nawo ndipo anaweramitsa mutu wake pansi mwaulemu.
So the two messengers went in towards Sodom at eventide, Lot, being seated in the gate of Sodom, —so Lot beheld and rose up to meet them, and bowed himself with his face to the earth.
2 Iye anati, “Ambuye wanga, chonde patukirani ku nyumba kwa mtumiki wanu. Mukhoza kusambitsa mapazi anu ndi kugona usiku uno kenaka nʼkumapitirira ndi ulendo wanu mmamawa.” Iwo anati, “Ayi, tigona panja.”
And he said Behold, I pray you my lords turn aside, I pray you, into the house of your servant, —and tarry the night and bathe your feet, so shall ye rise early, and go on your way. And they said, Nay, but, in the broad way, will we tarry the night.
3 Koma iye anawawumiriza kwambiri kotero kuti anapita naye pamodzi ku nyumba kwake. Anawakonzera chakudya buledi wopanda yisiti ndipo anadya.
But he became exceeding urgent with them, so they turned aside unto him and entered into his house, —and he made for them a banquet, unleavened cakes, also did he bake, and they did eat.
4 Alendo aja asanapite kogona, amuna onse achinyamata ndi achikulire ochokera mbali zonse za mzinda wa Sodomu anazinga nyumba ya Loti.
Ere yet they lay down, the men of the city—the men of Sodom, had come round against the house, from youth even unto age, —all the people from every quarter,
5 Iwo anayitana Loti namufunsa kuti, “Ali kuti amuna aja amene afika kuno usiku womwe uno? Atulutse, utipatse kuti tigone nawo malo amodzi.”
And they called unto Lot and said to him, Where are the men who have come in unto thee tonight? Bring them forth unto us, and let us know them!
6 Loti anatuluka panja kukakumana nawo natseka chitseko
And Lot went forth unto them to the entrance; but the door, closed he behind him.
7 ndipo anati, “Ayi anzanga, musachite zinthu zoyipa zotere.
And he said, —Do not I pray you my brethren act wickedly.
8 Taonani, ine ndili ndi ana anga akazi awiri amene sanagonepo ndi mwamuna. Mundilole ndikutulutsireni amenewo ndipo muchite nawo zimene mungafune. Koma musachite chilichonse ndi anthuwa, pakuti iwowa ndi alendo anga ndipo ndiyenera kuwatchinjiriza.”
Behold, I pray you, I, have two daughters who have not known man, I must needs now bring, them, forth unto you, and do ye to them, as may be good in your eyes, —Only to these men, ye may do nothing; for on this account, have they come under the shade of my roof.
9 Iwo anayankha kuti, “Tachoka apa tidutse.” Ndipo anati, “Munthu uyu anabwera kuno ngati mlendo chabe, tsono lero akufuna kuti akhale wotiweruza! Tikukhawulitsa kuposa iwowa.” Anapitiriza kumuwumiriza Loti uja nʼkumasunthira kutsogolo kuti athyole chitseko.
And they said, Stand back, And they said, This one, by himself, hath come in to sojourn and must always be acting the judge, Now, will we do more wickedly to thee, than to them. So they pressed sore upon the man—upon Lot—exceedingly, and drew near to break open the door.
10 Koma anthu aja anali mʼkatiwa anasuzumira namukokera Loti uja mʼkati mwa nyumba nʼkutseka chitseko.
And the men thrust forth their hand, and brought Lot in unto them into the house—and, the door, they closed:
11 Kenaka anawachititsa khungu anthu amene anali panja pa nyumba aja, aangʼono ndi aakulu omwe, kuti asaone pa khomo.
the men also who were at the entrance of the house, smote they with blindness, from small even unto great, so that they wearied themselves to find the entrance.
12 Anthu awiri aja anati kwa Loti, “Kodi uli ndi wina aliyense pano, kaya ndi akamwini ako, kaya ndi ana ako aamuna kapena aakazi, kapena aliyense mu mzindamu amene ndi anzako? Atulutse onse muno,
And the men said unto Lot, Whom besides hast thou here? Son-in-law and thy sons and thy daughters, and all that thou hast in the city, bring thou forth out of the place;
13 chifukwa tiwononga malo ano. Yehova waona kuti kuyipa kwa anthu a mu mzindawu kwakulitsa. Choncho watituma kuti tiwuwononge.”
For we are about to destroy this place, —for, great, is the outcry of them unto the face of Yahweh, so that Yahweh hath sent us to destroy it.
14 Choncho Loti anatuluka nayankhula ndi akamwini ake amene anali kuyembekezera kukwatira ana ake akazi nati, “Fulumirani, tiyeni tichoke pa malo ano chifukwa Yehova watsala pangʼono kuwononga mzindawu.” Koma akamwini akewo ankayesa kuti akungoselewula.
And Lot went forth and spake unto his sons-in-law who were about to take his two daughters and said Arise come forth out of this place, for Yahweh is about to destroy the city. And it came to pass, that he was as one that laughed, in the eyes of his sons-in-law.
15 Mmene kumacha, angelo aja anamufulumizitsa Loti nati, “Nyamuka, tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwo, ndipo mutuluke mu mzindawo kuopa kuti mungaphedwe pamodzi nawo.”
But as soon as, the dawn had sprung up, the messengers hastened Lot saying, —Arise! take thy wife and thy two daughters that are at hand, lest thou be swept away in the punishment of the city.
16 Koma Loti ankakayikabe. Koma Yehova anawachitira chifundo motero kuti anthu aja anagwira mkazi wake ndi ana ake aakazi aja nawatsogolera bwinobwino kuwatulutsa mu mzindawo.
And he lingered—so the men laid hold of his hand and of the hand of his wife and of the hand of his two daughters, in the tenderness of Yahweh towards him, —and they brought him out and led him forth outside the city.
17 Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”
And it came to pass when they had brought them forth outside, that they said, Escape for thy life, Look not behind thee, neither stand still in all the vale, —To the mountain, escape thou lest thou be swept away.
18 Koma Loti anawawuza kuti, “Ayi, ambuye anga chonde musatero!
And Lot said unto them, —No, I pray thee, My Lord!
19 Taonani, Inu mwachitira mtumiki wanu chifundo, ndipo mwaonetsa kukoma mtima kwanu pondipulumutsa. Sindingathawire ku mapiri chifukwa chiwonongekochi chikhoza kundipeza ndisanafike ku mapiriko ndipo ndingafe.
Behold, I pray thee thy servant hath found favour in thine eyes, so that thou hast magnified thy lovingkindness which thou hast performed with me in keeping alive my soul.—But, I, cannot escape to the mountain, lest calamity overtake me so shall I die.
20 Koma, chapafupi pomwepa pali mudzi woti ndikhoza kuthamanga nʼkukafikako. Mundilole ndithawireko, ndi waungʼono kwambiri, si choncho? Mukatero, moyo wanga upulumuka.”
Behold, I pray thee, this city, is near for fleeing thither And, it, is a little one, let me I pray thee, escape thither—is it not a, little, one? That my soul may live!
21 Mngeloyo anati kwa iye, “Chabwino, ndavomeranso pempho lako, sindiwononga mudzi ukunenawo.
And he said unto him, Behold! I have lifted up thy countenance, even as to this thing, —so that I will not overthrow the city, of which thou hast spoken.
22 Koma uthawireko mofulumira chifukwa sindichita kena kalikonse mpaka utafikako.” (Nʼchifukwa chake mudziwo unatchedwa Zowari).
Haste thee escape thither, for I cannot do anything, until thou have come in thither. For this cause: was the name of the city called Zoar.
23 Pamene Loti amafika ku Zowari, nʼkuti dzuwa litatuluka.
When, the sun, had come forth on the earth, Lot had entered into Zoar.
24 Ndiye Yehova anathira sulufule wamoto wochokera kumwamba kwa Yehova pa Sodomu ndi Gomora.
And, Yahweh, rained, upon Sodom and upon Gomorrah, brimstone and fire, —from Yahweh, out of the heavens:
25 Kotero, anawononga mizindayo, chigwa chonse pamodzi ndi onse okhala mʼmizindayo. Anawononganso zomera zonse za mʼdzikolo.
so he overthrew these cities, and all the circuit, —and all the inhabitants of the cities, and the produce of the ground.
26 Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.
But his wife looked from behind him, —and became—a pillar of salt.
27 Mmawa mwake, Abrahamu ananyamuka nabwerera kumalo kumene anakumana ndi Yehova kuja.
And Abraham gat up early in the morning, unto the place where he had stood before Yahweh;
28 Anayangʼana kumunsi ku Sodomu, Gomora ndi ku dziko lonse la ku chigwa, ndipo anaona chiwutsi chikufuka mʼdzikolo ngati chikuchokera mʼngʼanjo.
and he looked out over the face of Sodom and Gomorrah, and over all the face of the land of the circuit, and beheld and lo! the smoke of the land went up, like the smoke of a furnace.
29 Choncho Mulungu anawononga mizinda ya ku chigwa, koma anakumbukira pemphero la Abrahamu natulutsa Loti ku sulufule ndi moto zimene zinawononga mizinda ya kumene Loti amakhalako.
And it came to pass when God destroyed the cities of the circuit, that God remembered Abraham, and sent forth Lot out of the midst of the overthrow, when he overthrew the cities wherein Lot had dwelt.
30 Loti ndi ana ake awiri aakazi anachoka ku Zowari nakakhala ku mapiri, chifukwa amachita mantha kukhala ku Zowari. Iye ndi ana ake awiri ankakhala mʼphanga.
And Lot went up out of Zoar, and dwelt in the mountain and his two daughters with him. for he feared to dwell in Zoar, so he dwelt in a cave, he, and his two daughters.
31 Tsiku lina mwana wake wamkazi wamkulu anawuza mngʼono wake kuti, “Abambo athu ndi wokalamba ndipo palibe mwamuna aliyense pano woti atikwatire ndi kubereka ana monga mwa chikhalidwe cha pa dziko lonse lapansi.
And the firstborn said unto the younger. Our father is old, —and, a man, there is not in the earth to come in unto us, after the way of all the earth.
32 Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”
Come on! let us cause our father to drink wine and let us lie with him, that we may keep alive from our father, a seed.
33 Usiku umenewo analedzeretsa vinyo abambo awo, ndipo wamkuluyo analowa nagona naye. Abambo awo samadziwa kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
So they caused their father to drink wine that night, —and the firstborn went in. and lay with her father, but he noticed not her lying down nor her rising up.
34 Tsiku linali mwana wamkazi wamkulu uja anati kwa mngʼono wake, “Usiku wathawu ine ndinagona ndi abambo anga. Tiye tiwaledzeretsenso vinyo usiku uno ndipo iwe upite ndi kugona nawo ndipo mtundu wathu udzakhalapobe.”
And it came to pass on the morrow, that the firstborn said unto the younger, Lo! I lay, last night with my father, let us cause him to drink wine this night also, and go thou in—lie with him, that we may keep alive from our father, a seed.
35 Choncho analedzeranso vinyo abambo awo usiku umenewonso, ndipo mwana wamkazi wamngʼono anapita nagona nawo. Abambo awo sanadziwenso kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
So they caused their father, on that night also to drink wine, and the younger arose, and lay with him, but he noticed not her lying down, nor her rising up.
36 Choncho ana onse awiri a Loti aja anatenga pathupi pa abambo awo.
Thus did, the two daughters of Lot conceive from their father.
37 Mwana wamkazi wamkulu uja anabereka mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Mowabu. Iyeyo ndiye kholo la Amowabu onse.
And the firstborn bare a son, and called his name Moab, —the same, is the father of Moab, unto this day.
38 Mwana wamkazi wamngʼono naye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha iye Beni-Ammi. Iyeyu ndiye kholo la Aamoni onse.
And the younger she also bare a son, and called his name Ben-ammi, —the same, is the father of the sons of Ammon—unto this day.