< Genesis 18 >
1 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
І явився до нього Господь між дубами Мамре́, а він сидів при вході в намет під час денної спеки.
2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
І він ізвів очі свої та й побачив: ось три Мужі стоять біля нього. І побачив, і вибіг із входу намету назустріч Їм, і вклонився до землі,
3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
та й промовив: „Господи, коли тільки знайшов я милість в очах Твоїх, — не проходь повз Свойо́го раба!
4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
Принесуть трохи води, — і ноги Свої помийте, і спочиньте під деревом.
5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
І хай хліба шматок принесу я, а Ви підкріпіть серце Ваше. Потому пі́дете, бо на те Ви йдете повз свойо́го раба“. І сказали вони: “Зроби так, як сказав“.
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
І Авраам поспішив до намету до Сарри й сказав: „Візьми швидко три міри пшеничної муки, заміси́, і зроби коржі“.
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
І побіг Авраам до товару, і взяв молоде та добре теля, і дав слузі, а той швидко його пригото́вив.
8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
І взяв масла й молока, та теля приготовлене, та й поклав перед Ними, а сам став біля Них під деревом. І їли Вони.
9 Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
І сказали до нього: „Де Сарра, жінка твоя?“А він відказав: „Ось у наметі“.
10 Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
І сказав один з Них: „Я напевно вернуся до тебе за рік цього самого ча́су. І ось буде син у Сарри, жінки твоєї...“А Сарра це чула при вході намету, що був за Ним.
11 Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
Авраам же та Сарра старі були, віку похилого. У Сарри перестало бувати звичайне жіноче.
12 Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
І засміялася Сарра в нутрі своїм, говорячи: „Коли я зів'яла, то як станеться розкіш мені? Таж пан мій старий!“
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
І сказав Господь до Авраама: „Чого то сміялася Сарра отак: Чи ж справді вроджу, коли я зоста́рілась?
14 Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
Чи для Господа є річ занадто трудна? На означений час Я вернуся до тебе за рік цього самого часу, — Сарра ж тоді матиме сина“.
15 Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
А Сарра відріклася, говорячи: „Не сміялася я“, бо боялась. Але Він відказав: „Ні, — таки сміялася ти!“
16 Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
І повставали звідти ті Мужі, і поглянули на Содом, а Авраам пішов з Ними, щоб Їх відпровадити.
17 Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
А Господь сказав: „Чи Я від Авраама втаю, що Я маю зробити?
18 Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
Бож Авраам справді стане народом великим та дужим, і в ньому поблагословляться всі народи землі!
19 Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
Бо ви́брав Я його, щоб він наказав синам своїм і домові своєму по собі. І будуть вони дотримуватися дороги Господньої, щоб чинити справедливість та право, а то для того, щоб Господь здійснив на Авраамові, що сказав був про нього“.
20 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
І промовив Господь: „Через те, що крик Содому й Гомори великий, і що гріх їхній став дуже тяжкий,
21 choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
зійду́ ж Я та й побачу, чи не вчинили вони так, як крик про них, що доходить до Мене, — тоді їм загибіль, а як ні — то побачу“.
22 Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
І повернулися звідти ті Мужі, і пішли до Содому, а Авраам — усе ще стоя́в перед Господнім лицем.
23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
І Авраам підійшов та й промовив: „Чи погубиш також праведного з нечестивим?
24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
Може є п'ятдесят праведних у цьому місті, — чи також вигубиш і не пробачиш цій місцевості ради п'ятидесяти тих праведних, що в ньому є?
25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
Не можна Тобі чинити так, щоб убити праведного з нечестивим, бо стане праведний як нечестивий, — цього ж не можна Тобі! Чи ж Той, Хто всю землю судить, не вчинить правди?“
26 Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
І промовив Господь: „Коли Я в Содомі, у цьому місті, знайду́ п'ятдесят праведних, то вибачу цілій місцевості ради них“.
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
І відповів Авраам та й промовив: „Оце я осмілився був говорити до Господа свого, а я порох та попіл.
28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
Може п'ятдесят тих праведних не матиме п'яти, чи Ти знищиш ціле місто через п'ятьох?“І промовив Господь: „Не знищу, коли там знайду сорок і п'ять!“
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
І промовив до Нього він ще, та й сказав: „Може сорок там зна́йдеться?“А Господь відказав: „Не зроблю́ й ради сорока́!“
30 Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
І сказав Авраам: „Хай не гніває це мого Го́спода, і нехай я скажу́: „Може тридцять там зна́йдеться?“А Господь відказав: „Не зроблю́, коли й тридцять знайду́ там!“
31 Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
І сказав Авраам: „Оце я осмі́лився був говорити до Господа мого: Може двадцять там знайдеться?“А Господь відказав: „Не зроблю й ради двадцяти!“
32 Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
І сказав Авраам: „Хай не гніває це мого Го́спода, і нехай я скажу́ тільки ра́зу цього: Може хоч десять там зна́йдеться?“А Господь відказав: „Не знищу й ради десятьох!“
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.
І пішов Господь, як скінчив говорити до Авраама. А Авраам вернувся до свого місця.