< Genesis 18 >
1 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
İbrahim günün sıcak saatlerinde Mamre meşeliğindeki çadırının önünde otururken, RAB kendisine göründü.
2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
İbrahim karşısında üç adamın durduğunu gördü. Onları görür görmez karşılamaya koştu. Yere kapanarak,
3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
“Ey efendim, eğer gözünde lütuf bulduysam, lütfen kulunun yanından ayrılma” dedi,
4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
“Biraz su getirteyim, ayaklarınızı yıkayın. Şu ağacın altında dinlenin.
5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
Madem kulunuza konuk geldiniz, bırakın size yiyecek bir şeyler getireyim. Biraz dinlendikten sonra yolunuza devam edersiniz.” Adamlar, “Peki, dediğin gibi olsun” dediler.
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
İbrahim hemen çadıra, Sara'nın yanına gitti. Ona, “Hemen üç sea ince un al, yoğurup pide yap” dedi.
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
Ardından sığırlara koştu. Körpe ve besili bir buzağı seçip uşağına verdi. Uşak buzağıyı hemen hazırladı.
8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
İbrahim hazırlanan buzağıyı yoğurt ve sütle birlikte götürüp konuklarının önüne koydu. Onlar yerken o da yanlarında, ağacın altında durdu.
9 Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
Konuklar, “Karın Sara nerede?” diye sordular. İbrahim, “Çadırda” diye yanıtladı.
10 Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
O, “Gelecek yıl bu zamanda kesinlikle yanına döneceğim” dedi, “O zaman karın Sara'nın bir oğlu olacak.” Sara onun arkasında, çadırın girişinde durmuş, dinliyordu.
11 Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
İbrahim'le Sara kocamışlardı, yaşları hayli ileriydi. Sara âdetten kesilmişti.
12 Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
İçin için gülerek, “Bu yaştan sonra bu sevinci tadabilir miyim?” diye düşündü, “Üstelik efendim de yaşlı.”
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
RAB İbrahim'e sordu: “Sara niçin, ‘Bu yaştan sonra gerçekten çocuk sahibi mi olacağım?’ diyerek güldü?
14 Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
RAB için olanaksız bir şey var mı? Belirlenen vakitte, gelecek yıl bu zaman yanına döndüğümde Sara'nın bir oğlu olacak.”
15 Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
Sara korktu, “Gülmedim” diyerek yalan söyledi. RAB, “Hayır, güldün” dedi.
16 Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
Adamlar oradan ayrılırken Sodom'a doğru baktılar. İbrahim onları yolcu etmek için yanlarında yürüyordu.
17 Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
RAB, “Yapacağım şeyi İbrahim'den mi gizleyeceğim?” dedi,
18 Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
“Kuşkusuz İbrahim'den büyük ve güçlü bir ulus türeyecek, yeryüzündeki bütün uluslar onun aracılığıyla kutsanacak.
19 Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
Doğru ve adil olanı yaparak yolumda yürümeyi oğullarına ve soyuna buyursun diye İbrahim'i seçtim. Öyle ki, ona verdiğim sözü yerine getireyim.”
20 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
Sonra İbrahim'e, “Sodom ve Gomora büyük suçlama altında” dedi, “Günahları çok ağır.
21 choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
Onun için inip bakacağım. Duyduğum suçlamalar doğru mu, değil mi göreceğim. Bunları yapıp yapmadıklarını anlayacağım.”
22 Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
Adamlar oradan ayrılıp Sodom'a doğru gittiler. Ama İbrahim RAB'bin huzurunda kaldı.
23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
RAB'be yaklaşarak, “Haksızla birlikte haklıyı da mı yok edeceksin?” diye sordu,
24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
“Kentte elli doğru kişi var diyelim. Orayı gerçekten yok edecek misin? İçindeki elli doğru kişinin hatırı için kenti bağışlamayacak mısın?
25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
Senden uzak olsun bu. Haklıyı, haksızı aynı kefeye koyarak haksızın yanında haklıyı da öldürmek senden uzak olsun. Bütün dünyayı yargılayan adil olmalı.”
26 Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
RAB, “Eğer Sodom'da elli doğru kişi bulursam, onların hatırına bütün kenti bağışlayacağım” diye karşılık verdi.
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
İbrahim, “Ben toz ve külüm, bir hiçim” dedi, “Ama seninle konuşma yürekliliğini göstereceğim.
28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
Kırk beş doğru kişi var diyelim, beş kişi için bütün kenti yok mu edeceksin?” RAB, “Eğer kentte kırk beş doğru kişi bulursam, orayı yok etmeyeceğim” dedi.
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
İbrahim yine sordu: “Ya kırk kişi bulursan?” RAB, “O kırk kişinin hatırı için hiçbir şey yapmayacağım” diye yanıtladı.
30 Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
İbrahim, “Ya Rab, öfkelenme ama, otuz kişi var diyelim?” dedi. RAB, “Otuz kişi bulursam, kente dokunmayacağım” diye yanıtladı.
31 Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
İbrahim, “Ya Rab, lütfen konuşma yürekliliğimi bağışla” dedi, “Eğer yirmi kişi bulursan?” RAB, “Yirmi kişinin hatırı için kenti yok etmeyeceğim” diye yanıtladı.
32 Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
İbrahim, “Ya Rab, öfkelenme ama, bir kez daha konuşacağım” dedi, “Eğer on kişi bulursan?” RAB, “On kişinin hatırı için kenti yok etmeyeceğim” diye yanıtladı.
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.
RAB İbrahim'le konuşmasını bitirince oradan ayrıldı, İbrahim de çadırına döndü.