< Genesis 18 >

1 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
Potem PAN ukazał mu się na równinie Mamre, a on siedział u wejścia do [swego] namiotu w najgorętszej porze dnia.
2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
I podniósł swe oczy, i zobaczył, że naprzeciwko niego stanęli trzej mężczyźni. Gdy ich ujrzał, pobiegł od wejścia do namiotu na ich spotkanie i skłonił się do ziemi.
3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
I powiedział: Mój Panie, jeśli znalazłem teraz łaskę w twoich oczach, nie omijaj, proszę, swego sługi.
4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
Pozwól, by przyniesiono trochę wody, abyście mogli obmyć sobie nogi, potem odpoczniecie pod drzewem.
5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
I przyniosę kęs chleba, abyście posilili swoje serca. Potem odejdziecie, po to bowiem przyszliście do [mnie], swego sługi. A oni powiedzieli: Uczyń tak, jak powiedziałeś.
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
Abraham pospieszył do namiotu, do Sary, i powiedział: Przygotuj szybko trzy miarki najlepszej mąki i zrób podpłomyki.
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
Abraham zaś poszedł do stada, wziął młode i wyborne cielę i dał je słudze, który szybko je przyrządził.
8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
Wziął też masło, mleko i cielę, które przyrządził, i postawił przed nimi. A gdy oni jedli, on stał przy nich pod drzewem.
9 Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
I zapytali go: Gdzie [jest] twoja żona Sara? A on odpowiedział: [Jest] w namiocie.
10 Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
Wtedy powiedział [PAN]: Na pewno wrócę do ciebie [za rok] o tej porze, a oto twoja żona Sara [będzie miała] syna. A Sara przysłuchiwała się u wejścia do namiotu, które było za nim.
11 Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
Abraham i Sara byli starzy, w podeszłym wieku. I przestało już u Sary bywać według zwyczaju kobiet.
12 Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
Sara roześmiała się więc w sobie, mówiąc: Teraz, gdy się zestarzałam i mój pan jest starcem, mam doznawać rozkoszy?
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
Wtedy PAN powiedział do Abrahama: Dlaczego Sara roześmiała się, mówiąc: Czy naprawdę urodzę, gdy się zestarzałam?
14 Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
Czy jakakolwiek rzecz jest za trudna dla PANA? W przyszłym roku o tej porze wrócę do ciebie, a Sara będzie miała syna.
15 Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
I Sara zaparła się, mówiąc: Nie śmiałam się – bo się bała. A on powiedział: Przeciwnie, śmiałaś się.
16 Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
Potem ci mężczyźni wstali stamtąd i skierowali wzrok ku Sodomie. Abraham zaś szedł z nimi, aby ich odprowadzić.
17 Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
Wtedy PAN powiedział: Czy mam zataić przed Abrahamem, co zamierzam uczynić?
18 Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
Przecież Abraham na pewno [rozmnoży się] w lud wielki i możny, a w nim będą błogosławione wszystkie narody ziemi.
19 Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
Znam go bowiem [i wiem], że będzie nakazywał swoim synom i swemu domowi po sobie, aby strzegli drogi PANA oraz czynili sprawiedliwość i sąd; aby PAN sprowadził na Abrahama to, co mu powiedział.
20 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
Potem PAN powiedział: Ponieważ okrzyk Sodomy i Gomory jest wielki i ich grzech jest bardzo ciężki;
21 choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
Zstąpię teraz i zobaczę, czy postępują według tego okrzyku, który doszedł do mnie. A jeśli nie, dowiem się.
22 Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
Wtedy ci mężczyźni odwrócili wzrok i poszli stamtąd do Sodomy, ale Abraham jeszcze stał przed PANEM.
23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
I Abraham zbliżył się, i powiedział: Czy wytracisz sprawiedliwego razem z niegodziwym?
24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
Jeśli będzie pięćdziesięciu sprawiedliwych w tym mieście, czy je wytracisz i nie oszczędzisz [tego] miejsca ze względu na pięćdziesięciu sprawiedliwych, którzy w nim [są]?
25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
Niech to będzie dalekie od ciebie, byś miał uczynić coś takiego i zabić sprawiedliwego z niegodziwym, żeby sprawiedliwy był jak niegodziwy. Niech to będzie dalekie od ciebie! Czy Sędzia całej ziemi nie postąpi sprawiedliwie?
26 Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
Wtedy PAN odpowiedział: Jeśli znajdę w Sodomie pięćdziesięciu sprawiedliwych w samym mieście, oszczędzę całe miejsce ze względu na nich.
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
A Abraham odpowiedział: Oto ośmielam się teraz mówić do mojego Pana, choć jestem prochem i popiołem.
28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
Gdyby do tych pięćdziesięciu sprawiedliwych zabrakło pięciu, czy z powodu braku tych pięciu zniszczysz całe miasto? I odrzekł: Nie zniszczę, jeśli znajdę tam czterdziestu pięciu.
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
Odezwał się ponownie do niego i powiedział: A gdyby znalazło się tam czterdziestu? I odpowiedział: Nie uczynię [tego] ze względu na tych czterdziestu.
30 Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
I [Abraham] powiedział: Niech się nie gniewa mój Pan, że zapytam: A gdyby znalazło się tam trzydziestu? Odpowiedział: Nie uczynię [tego], jeśli znajdę tam trzydziestu.
31 Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
Rzekł [jeszcze]: Oto ośmielam się teraz mówić do mego Pana: [A] gdyby znalazło się tam dwudziestu? Odpowiedział: Nie zniszczę [go] ze względu na tych dwudziestu.
32 Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
Powiedział: Niech się nie gniewa mój Pan, że jeszcze tylko raz przemówię: A gdyby znalazło się tam dziesięciu? Odpowiedział: Nie zniszczę [go] ze względu na tych dziesięciu.
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.
Gdy PAN skończył rozmowę z Abrahamem, odszedł. Abraham zaś wrócił do siebie.

< Genesis 18 >