< Genesis 18 >

1 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
Yahvé lui apparut près des chênes de Mamré, comme il était assis à l'entrée de la tente, dans la chaleur du jour.
2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
Il leva les yeux et regarda, et il vit que trois hommes se tenaient près de lui. Il courut à leur rencontre depuis l'entrée de la tente, se prosterna à terre
3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
etdit: « Seigneur, si j'ai trouvé grâce à tes yeux, ne te sépare pas de ton serviteur.
4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
Allez maintenant chercher un peu d'eau, lavez vos pieds, et reposez-vous sous l'arbre.
5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
Je vais chercher un morceau de pain pour que vous puissiez vous rafraîchir le cœur. Après cela, vous pourrez vous en aller, maintenant que vous êtes venus vers votre serviteur. » Ils ont dit: « Très bien, faites ce que vous avez dit. »
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
Abraham se précipita dans la tente vers Sara, et dit: « Prépare vite trois seahs de fleur de farine, pétris-la et fais des gâteaux. »
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
Abraham courut au troupeau, prit un veau tendre et bon, et le donna au serviteur. Celui-ci s'empressa de le panser.
8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
Il prit du beurre, du lait et le veau qu'il avait habillé, et il le mit devant eux. Il se tint près d'eux sous l'arbre, et ils mangèrent.
9 Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
Ils lui demandèrent: « Où est Sarah, ta femme? » Il a dit: « Là, dans la tente. »
10 Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
Il dit: « Je reviendrai certainement chez toi l'année prochaine à peu près à la même époque; et voici que Sarah, ta femme, aura un fils. » Sara entendit à la porte de la tente, qui était derrière lui.
11 Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
Or Abraham et Sara étaient vieux, d'un âge avancé. Sara avait dépassé l'âge de procréer.
12 Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
Sara riait en elle-même, disant: « Quand je serai vieille, aurai-je du plaisir, mon seigneur étant vieux aussi? »
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
Yahvé dit à Abraham: « Pourquoi Sarah a-t-elle ri en disant: « Aurai-je vraiment un enfant quand je serai vieille?
14 Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
Y a-t-il quelque chose de trop difficile pour Yahvé? Au temps fixé, je reviendrai vers toi, à la saison qui vient, et Sara aura un fils. »
15 Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
Alors Sarah le nia, disant: « Je n'ai pas ri », car elle avait peur. Il a dit: « Non, mais vous avez ri. »
16 Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
Les hommes se levèrent de là et regardèrent vers Sodome. Abraham alla avec eux pour les voir en chemin.
17 Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
Yahvé dit: « Est-ce que je cacherai à Abraham ce que je fais,
18 Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
puisque Abraham deviendra une nation grande et puissante, et que toutes les nations de la terre seront bénies en lui?
19 Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
Car je l'ai connu, afin qu'il commande à ses enfants et à sa famille après lui, pour qu'ils gardent la voie de l'Éternel, en pratiquant la justice et l'équité, afin que l'Éternel fasse venir sur Abraham ce qu'il a dit de lui. »
20 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
Yahvé dit: « Puisque le cri de Sodome et de Gomorrhe est grand, et que leur péché est très grave,
21 choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
je descendrai maintenant, et je verrai si leurs actes sont aussi mauvais que les rapports qui me sont parvenus. Si ce n'est pas le cas, je le saurai. »
22 Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
Les hommes se détournèrent de là et allèrent vers Sodome, mais Abraham se tenait encore devant Yahvé.
23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
Abraham s'approcha, et dit: Veux-tu consumer les justes avec les méchants?
24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
Et s'il y a cinquante justes dans la ville? Vas-tu consumer et ne pas épargner la place pour les cinquante justes qui s'y trouvent?
25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
Qu'il soit loin de toi de faire de telles choses, de tuer les justes avec les méchants, afin que les justes soient comme les méchants. Que cela soit loin de vous. Le Juge de toute la terre ne devrait-il pas faire ce qui est juste? »
26 Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
Yahvé dit: « Si je trouve à Sodome cinquante justes dans la ville, j'épargnerai tout le lieu à cause d'eux. »
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
Abraham répondit: « Voici, j'ai pris sur moi de parler au Seigneur, bien que je sois poussière et cendre.
28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
Et s'il manque cinq des cinquante justes? Détruiras-tu toute la ville par manque de cinq? » Il a dit: « Je ne la détruirai pas si j'y trouve quarante-cinq personnes. »
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
Il lui parla encore, et dit: « Et s'il y en a quarante qui se trouvent là? » Il a dit: « Je ne le ferai pas pour l'amour des quarante. »
30 Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
Il dit: « Oh, ne laissez pas le Seigneur se mettre en colère, et je parlerai. Et s'il y en a trente trouvés là? » Il a dit: « Je ne le ferai pas si j'en trouve trente là-bas. »
31 Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
Il dit: « Voici, j'ai pris sur moi de parler au Seigneur. Et s'il y en a vingt qui se trouvent là? » Il a dit: « Je ne la détruirai pas à cause des vingt. »
32 Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
Il dit: « Oh, que le Seigneur ne se mette pas en colère, et je ne parlerai qu'une fois de plus. Et si l'on en trouve dix là-bas? » Il a dit: « Je ne la détruirai pas à cause des dix. »
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.
Yahvé s'en alla dès qu'il eut fini de s'entretenir avec Abraham, et Abraham retourna à sa place.

< Genesis 18 >