< Genesis 17 >
1 Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
İbramıqa yüç'əle yüçüd sennang'a mang'us Rəbb gyagu uvhuyn: – Gırgın əxəna Allah (El-Şadday) Zı vorna. Yizde yəqqı'n hohre, məttın yik'nana ixhe.
2 Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
Mugaavile Yizdeyiy yiğne yı'q'neeqa gyuvxhu, vake g'abıynbı geeb xəp qaa'as.
3 Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
İbram aq'vahiyna ç'iyelqa dizyaraççe. Allahee mang'uk'le eyhen:
4 “Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
– Yizde suralyna mugaavile vakana haane: Ğu geedne milletbışda dek ixhes.
5 Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
Zı vake geedne milletbışda dek ha'asva, g'iyniyle yiğın do İbram (xərna dek) deş, İbrahim (xəppananbışda dek) ixhes.
6 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
Yiğna nasıl geeb xəp qaa'as. Vake milletbı g'ales. Yiğne nasıle paççaharıb vuxhesınbı.
7 Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
Zı vakayiy vale qihnane yiğne nasılıka hammaşiysda mugaavile haa'a. Zı ixhes, yiğnayiy vale qihnane yiğne nasılbışda Allah.
8 Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
Vasiy vale qiyğiyne nasılbışis hammaşiys ğu alycaxhvana Kana'anna ölka huvu, manbışda Allah ixhes.
9 Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
Qiyğa Allahee İbrahimık'le uvhuyn: – Yiğne suraleb, ğunay vale qiyğiyne nasılbışe mugaavilee nəxüdiy eyhe, həməxüd he'e.
10 Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
Vakayiy vale qiyğiyne nasılbışika hav'uyne mugaavileyn işaarat in vod: Gırgın adamer sunnat hav'u vuxhes.
11 Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
Sunnatın çürüx g'ats'ak'vne. Sunnat Yizdeyiy vuşde mugaavileyn işaarat ixhes.
12 Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
Vuşde xaa yedike ıxhanar, menne milletbışiker alişşunar adameeşina insan molyulle yiğ ıxhamee sunnat he'e.
13 Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
Yiğne xaa yedike vuxhaynbıb, menne milletbışike alivşuynbıb sunnat hidyav'u g'ılymaa'a. Sunnat vuşde tanılin Yizde hammaşiyste mugaavileyn işaarat ixhes.
14 Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
Sunnat hidi'ına adameeşina insan mugaavile havaakal hav'uva, milletne yı'q'nee meexhecen.
15 Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
Allahee İbrahimık'le meed eyhen: – Xhunaşşeyk'le Sarayva immeyhe. G'iynike şaqa məng'ı'n do Sarra (printsesa) ixhes.
16 Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
Zı məng'ı's xayir-düə hevles: məng'ı'ker vas dix heles. Qiyğa məng'ı's sayib xayir-düə hevles: mana milletbışda yed yixhes, milletbışin paççahar məng'ı'ne nasılençe qığepç'es.
17 Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
İbrahim aq'vahiyna gizerçu, əqəna ha'u, culed alqa uvhuyn: – Vəş sennane insanıs uşax eyxheye? Yüç'əl sennane Sarraysse uxas əxəye?
18 Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
Qiyğa İbrahimee Allahık'le eyhen: – Hasre saccu I'smı'ı'l xheyir Yiğne xayir-düəyka üç'ürra axhvecen!
19 Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
Allahemee uvhuyn: – Sarree, yiğne xhunaşşe vas dix uxas, doyud I'saq' (əqəna) gixhxhe. Zı mugaavile mang'ukab, mang'ule qihniyne nasılıkab hammaşe havaacesda.
20 Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
Ğu I'smı'ı'lil-alla uvhuyn Zak'le g'ayxhıyn. Mang'usub Zı xayir-düə hevles, mang'uke g'abıynbı geeb xəp qaa'as. Mang'uke yits'ıq'öyre paççah g'avaales. Zı mang'uke xədın millet ha'as.
21 Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
Mugaavilemee Zı qööne sen ine gahıl Sarree vas uxasde I'saq'ıka haa'as.
22 Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
Allahee man İbrahimık'le uvhu ooqa ts'ıts'xha.
23 Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
Hamanicab yiğıl İbrahimee cune xaabın gırgın adamer: dix I'smı'ı'l, cune xaa yedike vuxhayn gırgın nukarar, menne milletbışike alivşuynbıb sacigeeqa sav'u, Allahee cuk'le uvhuyn xhinne, sunnat hav'u.
24 Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
İbrahim sunnat hı'iyng'a mang'uqa yüç'əle yüç'üd senniy vod.
25 ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
I'smı'ı'l sunnat ha'ang'a mang'uqa yits'ıxhebad senniy vod.
26 Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
İbrahimiy I'smı'ı'l sa yiğıl sunnat hav'u.
27 Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.
Cuka sa yiğıl, cune xaabın gırgın adamer, menne milletbışike alivşuynbı, cune xaa yedike vuxhaynbı gırgınbı sunnat haa'anbı.