< Genesis 17 >
1 Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
Or, après qu’Abram eut commencé sa quatre-vingt-dix-neuvième année, le Seigneur lui apparut, et lui dit: Je suis le Dieu tout-puissant: marche devant moi, et sois parfait.
2 Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
J’établirai mon alliance entre moi et toi, et je te multiplierai prodigieusement.
3 Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
Abram tomba incliné sur sa face.
4 “Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
Et Dieu lui dit: C’est moi, et mon alliance sera avec toi, et tu seras père de beaucoup de nations.
5 Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
Et on ne t’appellera plus du nom d’Abram, mais tu te nommeras Abraham; car je t’ai établi père de beaucoup de nations.
6 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
Et je te ferai croître prodigieusement, et je t’établirai chef de nations; et des rois sortiront de toi.
7 Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
Ainsi j’établirai mon alliance entre moi et toi, et entre ta postérité après toi dans ses générations, par un pacte éternel; afin que je sois ton Dieu et le Dieu de ta postérité après toi.
8 Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
Et je te donnerai et à ta postérité la terre de ton pèlerinage, toute la terre de Chanaan, en possession éternelle; et je serai leur Dieu.
9 Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
Dieu dit encore à Abraham: Tu garderas mon alliance, toi et ta postérité après toi dans ses générations.
10 Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
Voici mon alliance que vous observerez entre moi et vous, et ta postérité après toi: Tout mâle d’entre vous sera circoncis.
11 Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
Et vous circoncirez votre chair, afin que ce soit là un signe d’alliance entre moi et vous.
12 Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
L’enfant de huit jours sera circoncis parmi vous; tout mâle en vos générations, tant le serviteur né dans votre maison, que le serviteur acheté, sera circoncis, et même celui qui ne sera pas de votre race.
13 Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
Ainsi mon pacte en votre chair sera une alliance éternelle.
14 Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
Le mâle dont la chair n’aura pas été circoncise, cette âme sera exterminée du milieu de son peuple, parce qu’il aura rendu vaine mon alliance.
15 Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
Dieu dit aussi à Abraham: Tu n’appelleras pas ta femme Saraï, mais Sara.
16 Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
Je la bénirai, et d’elle je te donnerai un fils que je dois bénir aussi; et il sera chef de nations; et des rois de peuples sortiront de lui.
17 Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
Abraham tomba sur sa face, et rit, disant en son cœur: Pensez-vous qu’à un centenaire naîtra un fils, et que Sara nonagénaire enfantera?
18 Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
Et il dit à Dieu: Plaise à Dieu qu’Ismaël vive devant vous!
19 Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
Et Dieu répondit à Abraham: Sara ta femme t’enfantera un fils, et tu l’appelleras du nom d’Isaac, et je ferai de mon pacte avec lui et avec sa postérité après lui une alliance éternelle.
20 Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
Pour Ismaël, je t’ai aussi exaucé: voilà que je le bénirai, que je le ferai croître et que je le multiplierai grandement; il donnera naissance à douze chefs, et je le ferai père d’une grande nation.
21 Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
Mais mon alliance, je l’établirai avec Isaac, que t’enfantera Sara en ce même temps, l’année prochaine.
22 Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
Et lorsque fut fini le discours de Dieu qui lui parlait, Dieu disparut de devant Abraham.
23 Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
Abraham donc prit Ismaël son fils, tous les serviteurs nés dans sa maison et tous ceux qu’il avait achetés, tous mâles d’entre les hommes de sa maison, et il les circoncit aussitôt ce jour-là même, comme Dieu lui avait ordonné.
24 Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
Or Abraham avait quatre-vingt-dix-neuf ans, quand il circoncit sa chair.
25 ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
Et Ismaël son fils avait accompli treize ans au moment de sa circoncision.
26 Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
Dans le même jour fut circoncis Abraham et Ismaël son fils.
27 Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.
Et tous les hommes de sa maison, tant les serviteurs nés chez lui, que ceux qui avaient été achetés, et les étrangers furent pareillement circoncis.