< Genesis 17 >

1 Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
Lorsque Abram fut arrivé à l’âge de quatre-vingt-dix-neuf ans, Yahweh lui apparut et lui dit: « Je suis le Dieu tout-puissant; marche devant ma face et sois irréprochable:
2 Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
j’établirai mon alliance entre moi et toi, et je te multiplierai à l’infini. »
3 Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
Abram tomba la face contre terre, et Dieu lui parla ainsi:
4 “Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
« Moi, voici mon alliance avec toi: tu deviendras père d’une multitude de nations.
5 Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
On ne te nommera plus Abram, mais ton nom sera Abraham, car je te fais père d’une multitude de nations.
6 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
Je te ferai croître extraordinairement, je ferai de toi des nations, et des rois sortiront de toi.
7 Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
J’établis mon alliance, entre moi et toi et tes descendants après toi, d’âge en âge, en une alliance perpétuelle, pour être ton Dieu et le Dieu de tes descendants après toi.
8 Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
Je te donnerai, à toi et à tes descendants après toi, le pays où tu séjournes comme étranger, tout le pays de Canaan, en possession perpétuelle, et je serai leur Dieu ».
9 Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
Dieu dit à Abraham: « Et toi, tu garderas mon alliance, toi et tes descendants après toi, d’âge en âge.
10 Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
Voici l’alliance que vous avez à garder, l’alliance entre moi et vous, et tes descendants après toi: tout mâle parmi vous sera circoncis.
11 Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
Vous vous circoncirez dans votre chair, et ce sera le signe de l’alliance entre moi et vous.
12 Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
Quand il aura huit jours, tout mâle parmi vous, d’âge en âge, sera circoncis, qu’il soit né dans la maison, ou qu’il ait été acquis à prix d’argent d’un étranger quelconque, qui n’est pas de ta race.
13 Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
On devra circoncire le mâle né dans la maison ou acquis à prix d’argent, et mon alliance sera dans votre chair comme alliance perpétuelle.
14 Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
Un mâle incirconcis, qui n’aura pas été circoncis dans sa chair, sera retranché de son peuple: il aura violé mon alliance. »
15 Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
Dieu dit à Abraham: « Tu ne donneras plus à Saraï, ta femme, le nom de Saraï, car son nom est Sara.
16 Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
Je la bénirai, et je te donnerai aussi d’elle un fils; je la bénirai, et elle deviendra des nations; des rois de peuples sortiront d’elle. »
17 Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
Abraham tomba la face contre terre, et il rit, disant dans son cœur: « Naîtra-t-il un fils à un homme de cent ans? Et Sara, une femme de quatre-vingt-dix ans, enfantera-t-elle? »
18 Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
Et Abraham dit à Dieu: « Oh! qu’Ismaël vive devant votre face! »
19 Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
Dieu dit: « Oui, Sara, ta femme, t’enfantera un fils; tu le nommeras Isaac, et j’établirai mon alliance avec lui comme une alliance perpétuelle pour ses descendants après lui.
20 Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
Quant à Ismaël, je t’ai entendu. Voici, je l’ai béni, je le rendrai fécond et je le multiplierai extrêmement; il engendrera douze princes, et je ferai de lui une grande nation.
21 Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
Mais mon alliance, je l’établirai avec Isaac, que Sara t’enfantera l’année prochaine, à cette époque. »
22 Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
Et ayant achevé de parler avec lui, Dieu remonta d’auprès d’Abraham.
23 Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
Abraham prit Ismaël, son fils, ainsi que tous les serviteurs nés dans sa maison et tous ceux qu’il avait acquis à prix d’argent, tous les mâles parmi les gens de sa maison, et il les circoncit en ce jour même, comme Dieu le lui avait commandé.
24 Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
Abraham était âgé de quatre-vingt-dix-neuf ans lorsqu’il fut circoncis;
25 ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
et Ismaël, son fils, avait treize ans lorsqu’il fut circoncis.
26 Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
Ce même jour, Abraham fut circoncis, ainsi qu’Ismaël, son fils;
27 Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.
et tous les hommes de sa maison, ceux qui étaient nés chez lui et ceux qui avaient été acquis des étrangers à prix d’argent, furent circoncis avec lui.

< Genesis 17 >