< Genesis 17 >
1 Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
Když pak Abram byl v devadesáti devíti letech, ukázal se mu Hospodin, a řekl jemu: Já jsem Bůh silný všemohoucí; chodiž ustavičně přede mnou a budiž dokonalým.
2 Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
A učiním smlouvu svou mezi sebou a tebou a rozmnožím tě náramně velmi.
3 Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
Padl pak Abram na tvář svou; i mluvil Bůh s ním, řka:
4 “Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
Jáť jsem, aj, smlouva má s tebou, a budeš otcem národů mnohých.
5 Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
Aniž více slouti bude jméno tvé Abram, ale bude jméno tvé Abraham; nebo otcem mnohých národů učinil jsem tě.
6 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
A učiním, abys se rozplodil náramně velmi, a rozšířím tě v národy; i králové z tebe vyjdou.
7 Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
Utvrdím také smlouvu svou mezi sebou a tebou, i mezi semenem tvým po tobě, po rodech jejich, za smlouvu věčnou, totiž abych byl Bohem tvým i semene tvého po tobě.
8 Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
Nadto dám tobě i semeni tvému po tobě zemi, v nížto obýváš pohostinu, všecku zemi Kananejskou k vládařství věčnému; a budu jejich Bohem.
9 Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
Řekl ještě Bůh Abrahamovi: Ty pak ostříhati budeš smlouvy mé, ty i símě tvé po tobě, po rodech svých.
10 Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
Tatoť jest smlouva má mezi mnou a mezi vámi, i mezi semenem tvým po tobě, kteréž ostříhati budete: Aby obřezán byl mezi vámi každý pohlaví mužského.
11 Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
Obřežete pak tělo hanby své; a to bude znamením smlouvy mezi mnou a mezi vámi.
12 Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
Každý tedy pohlaví mužského osmého dne obřezán bude mezi vámi po rodech vašich, doma narozený i koupený za stříbro, z kterých by koli cizozemců byl, jenž není z semene tvého.
13 Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
Konečně ať jest obřezán narozený v domě tvém, i koupený za peníze tvé; a budeť smlouva má na těle vašem za smlouvu věčnou.
14 Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
Neobřezaný pak pacholík, kterýž by neobřezal těla neobřízky své, vyhlazena zajisté bude duše ta z lidu svého; nebo smlouvu mou zrušil.
15 Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
Řekl také Bůh Abrahamovi: Sarai manželce své nebudeš říkati Sarai, ale Sára bude jméno její.
16 Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
Nebo požehnám jí a dámť z ní syna; požehnámť jí, a bude v národy; králové národů z ní vyjdou.
17 Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
Tedy padl Abraham na tvář svou, a zasmáv se, řekl v srdci svém: Zdali stoletému narodí se syn? A zdali Sára v devadesáti letech porodí?
18 Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
I řekl Abraham Bohu: Ó byť jen Izmael živ byl před tebou!
19 Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
Jemužto řekl Bůh: Nýbrž Sára manželka tvá porodí tobě syna, a nazůveš jméno jeho Izák; i utvrdím smlouvu svou s ním za smlouvu věčnou, i s semenem jeho po něm.
20 Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
Také o Izmaele uslyšel jsem tě; a aj, požehnám jemu, a učiním to, aby se rozplodil, a rozmnožím ho náramně velmi; dvanáctero knížat zplodí, a rozšířím jej v národ veliký.
21 Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
Ale smlouvu svou utvrdím s Izákem, kteréhožť porodí Sára po roce, při tomto času.
22 Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
A když dokonal Bůh řeč svou s ním, vstoupil od Abrahama.
23 Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
Vzal tedy Abraham Izmaele syna svého, i všecky zrozené v domě svém, i všecky koupené za stříbro své, každého, kdož byl pohlaví mužského, z domácích svých, a obřezal tělo neobřízky jejich hned v ten den, jakž s ním Bůh mluvil.
24 Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
A byl Abraham v devadesáti devíti letech, když obřezáno bylo tělo neobřízky jeho.
25 ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
Izmael pak syn jeho byl v třinácti letech, když obřezáno bylo tělo neobřízky jeho.
26 Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
Jednoho a téhož dne obřezáni jsou, Abraham a Izmael syn jeho.
27 Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.
I všickni domácí jeho, doma zrození i za stříbro od cizozemce koupení, obřezáni jsou s ním.