< Genesis 16 >

1 Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara;
Therfor Sarai, wijf of Abram, hadde not gendrid fre children; but sche hadde a seruauntesse of Egipt, Agar bi name, and seide to hir hosebonde, Lo!
2 ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.” Abramu anamvera Sarai.
the Lord hath closid me, that Y schulde not bere child; entre thou to my seruauntesse, if in hap Y schal take children, nameli of hir. And whanne he assentide to hir preiynge, sche took Agar Egipcian,
3 Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi.
hir seruauntesse, after ten yeer aftir that thei begunne to enhabite in the lond of Chanaan, and sche yaf Agar wiif to hir hosebonde.
4 Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba. Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai.
And Abram entride to Agar; and Agar seiy that sche hadde conseyued, and sche dispiside hir ladi.
5 Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”
And Saray seide to Abram, Thou doist wickidli ayens me; I yaf my seruauntesse in to thi bosum, which seeth, that sche conseyuede, and dispisith me; the Lord deme betwixe me and thee.
6 Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.
And Abram answerde and seide to hir, Lo! thi seruauntesse is in thin hond; vse thou hir as `it likith. Therfor for Sarai turmentide hir, sche fledde awei.
7 Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri.
And whanne the aungel of the Lord hadde founde hir bisidis a welle of watir in wildernesse, which welle is in the weie of Sur in deseert,
8 Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?” Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”
he seide to hir, Fro whennus comest thou Agar, the seruauntesse of Sarai, and whidur goist thou? Which answerde, Y fle fro the face of Sarai my ladi.
9 Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere.
And the aungel of the Lord seide to hir, Turne thou ayen to thi ladi, and be thou mekid vndur hir hondis.
10 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”
And eft he seide, Y multipliynge schal multiplie thi seed, and it schal not be noumbrid for multitude.
11 Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti, “Ndiwe woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna. Udzamutcha dzina lake Ismaeli, pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.
And aftirward he seide, Lo! thou hast conseyued, and thou schalt bere a sone, and thou schalt clepe his name Ismael, for the Lord hath herd thi turment;
12 Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala; adzadana ndi aliyense ndipo anthu onse adzadana naye, adzakhala mwaudani pakati pa abale ake onse.”
this schal be a wielde man; his hond schal be ayens alle men, and the hondis of alle men schulen be ayens him; and he schal sette tabernaclis euene ayens alle his britheren.
13 Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.”
Forsothe Agar clepide the name of the Lord that spak to hir, Thou God that seiyest me; for sche seide, Forsothe here Y seiy the hynderere thingis of him that siy me.
14 Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.
Therfor sche clepide thilke pit, the pit of hym that lyueth and seeth me; thilk pit is bitwixe Cades and Barad.
15 Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli.
And Agar childide a sone to Abram, which clepide his name Ismael.
16 Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.
Abram was of `eiyti yeere and sixe, whanne Agar childide Ysmael to hym.

< Genesis 16 >