< Genesis 15 >
1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
По цих-о подіях було слово Господнє Аврамові в видінні таке: „Не бійся, Авраме, — Я тобі щит, нагорода твоя вельми велика“.
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
А Аврам відізвався: „Господи, Господи, — що́ даси Ти мені, коли я бездітний ходжу́, а керівник мого господарства — він Елі-Езер із Дамаску“.
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
І сказав Аврам: „Отож, Ти не дав нащадка мені, і ото мій керівник — спадкоє́мець мені“.
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
І ось слово Господнє до нього таке: „Він не бу́де спадкоє́мець тобі, але той, хто вийде з твойого нутра, — він буде спадкоє́мець тобі“.
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
І Господь його вивів надвір та й сказав: „Подивися на небо, та зорі злічи, коли тільки потрапиш ти їх полічити“. І до нього прорік: „Таким буде потомство твоє!“
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
І ввірував Аврам Господе́ві, а Він залічив йому те в праведність.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
І промовив до нього: „Я Господь, що вивів тебе з Уру халдейського, щоб дати тобі землю оцю, щоб став ти спадкоє́мець її“.
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
І промовив Аврам: „Господи, Господи, — з чого я довідаюся, що буду спадкоє́мець її?“
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
Він же промовив до нього: „Візьми трилітнє теля, і трилітню козу, і трилітнього барана, і горлицю, і пташеня голубине“.
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
І взяв він для Нього все те, і розсік його пополовині, і дав кожну частину його відповідно до другої, але птаства не розсік.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
І зліталося хиже птаство на трупи, та Аврам відганяв його.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
Коли ж сонце схилялось на захід, то спав сон на Аврама. І ось спадає на нього жах темний, великий.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
І промовив Господь до Аврама: „Добре знай, що потомство твоє буде прихо́дьком в землі не своїй. І будуть служити вони, і будуть їх мучити чотири сотні літ.
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
Але наро́д, якому служити вони будуть, Я засуджу́; та вони потім вийдуть з великим маєтком.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
А ти до своєї рідні при́йдеш у мирі, у старості добрій похований будеш.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
А покоління четверте повернеться сюди, бо досі не повний ще гріх амореянина“.
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
І сталось, коли зайшло сонце й була те́мрява, то ось появилась мов димуюча піч, та смолоскип огняни́й перейшов поміж тими кусками жертви.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
І того дня склав Господь заповіта з Аврамом, говорячи: „Насінню твоєму Я дав оцю землю від річки Єгипту аж до річки великої, до річки Ефрата:
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
хенеянина, і кенізеянина, і кадмонеянина,
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
і хіттеянина, і періззеянина, і рефаеянина,
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
і амореянина, і ханаанеянина, і ґірґашеянина, і евусеянина“.