< Genesis 15 >
1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
Après ces événements, la parole de Yahweh fut adressée à Abram en vision: « Ne crains point, Abram; je suis ton bouclier; ta récompense sera très grande. »
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
Abram répondit: « Seigneur Yahweh, que me donnerez-vous? Je m’en vais sans enfants, et l’héritier de ma maison, c’est Eliézer de Damas. »
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
Et Abram dit: « Voici, vous ne m’avez pas donné de postérité, et un homme attaché à ma maison sera mon héritier. »
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
Alors la parole de Yahweh lui fut adressée en ces termes: « Ce n’est pas lui qui sera ton héritier, mais celui qui sortira de tes entrailles sera ton héritier. »
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
Et, l’ayant conduit dehors, il dit: « Lève ton regard vers le ciel et compte les étoiles, si tu peux les compter. » Et il lui dit: « Telle sera ta postérité. »
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
Abram eut foi à Yahweh, et Yahweh le lui imputa à justice.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
Et il lui dit: « Je suis Yahweh, qui t’ai fait sortir d’Ur des Chaldéens, afin de te donner ce pays pour le posséder. »
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
Abram répondit: « Seigneur Yahweh, à quoi connaîtrai-je que je le posséderai? »
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
Et Yahweh lui dit: « Prends une génisse de trois ans, une chèvre de trois ans, un bélier de trois ans, une tourterelle et un jeune pigeon. »
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
Abram lui amena tous ces animaux et, les ayant partagés par le milieu, il mit chaque moitié vis-à-vis de l’autre; mais il ne partagea pas les oiseaux.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
Les oiseaux de proie s’abattirent sur les cadavres, et Abram les chassa.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
Comme le soleil se couchait, un profond sommeil tomba sur Abram; une terreur, une obscurité profonde tombèrent sur lui.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
Yahweh dit à Abram: « Sache bien que tes descendants seront étrangers dans un pays qui ne sera pas à eux; ils y seront en servitude et on les opprimera pendant quatre cents ans.
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
Mais je jugerai la nation à laquelle ils auront été asservis, et ensuite ils sortiront avec de grands biens.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
Toi, tu t’en iras en paix vers tes pères; tu seras mis en terre dans une heureuse vieillesse.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
A la quatrième génération ils reviendront ici; car jusqu’à présent l’iniquité de l’Amorrhéen n’est pas à son comble. »
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
Lorsque le soleil fut couché et qu’une profonde obscurité fut venue, voici qu’un four fumant et un brandon de feu passaient entre les animaux partagés.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
En ce jour-là, Yahweh fit alliance avec Abram, en disant: « Je donne à ta postérité ce pays, depuis le fleuve d’Égypte jusqu’au grand fleuve, au fleuve de l’Euphrate:
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
le pays des Cinéens, des Cénézéens, des Cadmonéens,
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
des Hittites, des Phéréséens, des Rephaïm,
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
des Amorrhéens, des Chananéens, des Gergéséens et des Jébuséens.