< Genesis 15 >

1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
After these things the word of the LORD came to Abram in a vision, saying, Fear not, Abram: I am thy shield, and thy exceeding great reward.
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
And Abram said, LORD God, what wilt thou give me, seeing I go childless, and the heir of my house is this Eliezer of Damascus?
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
And Abram said, Behold, to me thou hast given no seed: and, lo, one born in my house is my heir.
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
And, behold, the word of the LORD came to him, saying, This shall not be thy heir; but he that shall come forth out of thy own loins shall be thy heir.
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
And he brought him forth abroad, and said, Look now toward heaven, and count the stars, if thou art able to number them: and he said to him, So shall thy seed be.
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
And he believed in the LORD; and he counted it to him for righteousness.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
And he said to him, I am the LORD that brought thee out of Ur of the Chaldees, to give thee this land to inherit it.
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
And he said, Lord GOD, by what shall I know that I shall inherit it?
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
And he said to him, Take me an heifer of three years old, and a female goat of three years old, and a ram of three years old, and a turtledove, and a young pigeon.
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
And he took to him all these, and divided them in the midst, and laid each piece one against another: but the birds he did not divide.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
And when the fowls came down upon the carcases, Abram drove them away.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
And when the sun was going down, a deep sleep fell upon Abram; and, lo, an horror of great darkness fell upon him.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
And he said to Abram, Know certainly that thy seed shall be a stranger in a land that is not theirs, and shall serve them; and they shall afflict them four hundred years;
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
And also that nation, which they shall serve, will I judge: and afterward shall they come out with great substance.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
And thou shalt go to thy fathers in peace; thou shalt be buried in a good old age.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
But in the fourth generation they shall come here again: for the iniquity of the Amorites is not yet full.
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
And it came to pass, that, when the sun had gone down, and it was dark, behold a smoking furnace, and a burning lamp that passed between those pieces.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
In that same day the LORD made a covenant with Abram, saying, To thy seed have I given this land, from the river of Egypt to the great river, the river Euphrates:
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
The Kenites, and the Kenizzites, and the Kadmonites,
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
And the Hittites, and the Perizzites, and the Rephaims,
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
And the Amorites, and the Canaanites, and the Girgashites, and the Jebusites.

< Genesis 15 >