< Genesis 15 >

1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
And so, these things having been transacted, the word of the Lord came to Abram by a vision, saying: “Do not be afraid, Abram, I am your protector, and your reward is exceedingly great.”
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
And Abram said: “Lord God, what will you give to me? I may go without children. And the son of the steward of my house is this Eliezer of Damascus.”
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
And Abram added: “Yet to me you have not given offspring. And behold, my servant born in my house will be my heir.”
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
And immediately the word of the Lord came to him, saying: “This one will not be your heir. But he who will come from your loins, the same will you have for your heir.”
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
And he brought him outside, and he said to him, “Take in the heavens, and number the stars, if you can.” And he said to him, “So also will your offspring be.”
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
Abram believed God, and it was reputed to him unto justice.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
And he said to him, “I am the Lord who led you away from Ur of the Chaldeans, so as to give you this land, and so that you would possess it.”
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
But he said, “Lord God, in what way may I be able to know that I will possess it?”
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
And the Lord responded by saying: “Take for me a cow of three years, and a she-goat of three years, and a ram of three years, also a turtle-dove and a pigeon.”
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
Taking all these, he divided them through the middle, and placed both parts opposite one another. But the birds he did not divide.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
And birds descended upon the carcasses, but Abram drove them away.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
And when the sun was setting, a deep sleep fell upon Abram, and a dread, great and dark, invaded him.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
And it was said to him: “Know beforehand that your future offspring will be sojourners in a land not their own, and they will subjugate them in servitude and afflict them for four hundred years.
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
Yet truly, I will judge the nation that they will serve, and after this they will depart with great substance.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
But you will go to your fathers in peace and be buried at a good old age.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
But in the fourth generation, they will return here. For the iniquities of the Amorites are not yet completed, even to this present time.”
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
Then, when the sun had set, there came a dark mist, and there appeared a smoking furnace and a lamp of fire passing between those divisions.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
On that day, God formed a covenant with Abram, saying: “To your offspring I will give this land, from the river of Egypt, even to the great river Euphrates:
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
the land of the Kenites and the Kenizzites, the Kadmonites
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
and the Hittites, and the Perizzites, likewise the Rephaim,
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
and the Amorites, and the Canaanites, and the Girgashites, and the Jebusites.”

< Genesis 15 >