< Genesis 15 >
1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
After these things, the word of the Lord came to Abram in a vision, saying, Have no fear, Abram: I will keep you safe, and great will be your reward.
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
And Abram said, What will you give me? for I have no child and this Eliezer of Damascus will have all my wealth after me.
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
And Abram said, You have given me no child, and a servant in my house will get the heritage.
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
Then said the Lord, This man will not get the heritage, but a son of your body will have your property after you.
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
And he took him out into the open air, and said to him, Let your eyes be lifted to heaven, and see if the stars may be numbered; even so will your seed be.
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
And he had faith in the Lord, and it was put to his account as righteousness.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
And he said to him, I am the Lord, who took you from Ur of the Chaldees, to give you this land for your heritage.
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
And he said, O Lord God, how may I be certain that it will be mine?
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
And he said, Take a young cow of three years old, and a she-goat of three years old, and a sheep of three years old, and a dove and a young pigeon.
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
All these he took, cutting them in two and putting one half opposite the other, but not cutting the birds in two.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
And evil birds came down on the bodies, but Abram sent them away.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
Now when the sun was going down, a deep sleep came on Abram, and a dark cloud of fear.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
And he said to Abram, Truly, your seed will be living in a land which is not theirs, as servants to a people who will be cruel to them for four hundred years;
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
But I will be the judge of that nation whose servants they are, and they will come out from among them with great wealth.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
As for you, you will go to your fathers in peace; at the end of a long life you will be put in your last resting-place.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
And in the fourth generation they will come back here; for at present the sin of the Amorite is not full.
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
Then when the sun went down and it was dark, he saw a smoking fire and a flaming light which went between the parts of the bodies.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
In that day the Lord made an agreement with Abram, and said, To your seed have I given this land from the river of Egypt to the great river, the river Euphrates:
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
The Kenite, the Kenizzite, and the Kadmonite,
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
And the Hittite, and the Perizzite, and the Rephaim,
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
And the Amorite, and the Canaanite, and the Girgashite, and the Jebusite.