< Genesis 15 >

1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
Nogen Tid efter kom HERRENS Ord til Abram i et Syn saaledes: »Frygt ikke, Abram, jeg er dit Skjold; din Løn skal blive saare stor!«
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
Men Abram svarede: »Herre, HERRE, hvad kan du give mig, naar jeg dog gaar barnløs bort, og en Mand fra Damaskus, Eliezer, skal arve mit Hus.«
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
Og Abram sagde: »Du har jo intet Afkom givet mig, og se, min Hustræl kommer til at arve mig!«
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
Og se, HERRENS Ord kom til ham saaledes: »Han kommer ikke til at arve dig, men den, der udgaar af dit Liv, han skal arve dig.«
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
Derpaa førte han ham ud i det fri og sagde: »Se op mod Himmelen og prøv, om du kan tælle Stjernerne!« Og han sagde til ham: »Saaledes skal dit Afkom blive!«
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
Da troede Abram HERREN, og han regnede ham det til Retfærdighed.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
Derpaa sagde han til ham: »Jeg er HERREN, som førte dig bort fra Ur-Kasdim for at give dig dette Land i Eje!«
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
Men han svarede: »Herre, HERRE, hvorpaa kan jeg kende, at jeg skal faa det i Eje?«
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
Da sagde han til ham: »Tag mig en treaars Kvie, en treaars Ged og en treaars Væder, en Turteldue og en Smaafugl!«
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
Saa tog han alle disse Dyr skar dem midt over og lagde Halvdelene over for hinanden; dog skar han ikke Fuglene over.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
Da slog der Rovfugle ned paa de døde Kroppe, men Abram skræmmede dem bort.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
Da Solen saa var ved at gaa ned, faldt der Dvale over Abram, og se, Rædsel faldt over ham, et stort Mørke.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
Og han sagde til Abram: »Vide skal du, at dit Afkom skal bo som fremmede i et Land, der ikke er deres eget; de skal trælle for dem og mishandles af dem i 400 Aar.
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
Dog vil jeg ogsaa dømme det Folk, de kommer til at trælle for, og siden skal de vandre ud med meget Gods.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
Men du skal fare til dine Fædre i Fred og blive jordet i en god Alderdom.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
I fjerde Slægtled skal de vende tilbage hertil; thi endnu er Amoriternes Syndeskyld ikke fuldmoden.«
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
Da Solen var gaaet ned og Mørket faldet paa, viste der sig en rygende Ovn med en flammende Ildslue, der skred frem mellem de sønderskaarne Kroppe.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
Paa den Dag sluttede HERREN Pagt med Abram, idet han sagde: »Dit Afkom giver jeg dette Land fra Ægyptens Bæk til den store Flod, Eufratfloden,
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
det er Keniterne, Kenizziterne, Kadmoniterne,
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
Hetiterne, Perizziterne, Refaiterne,
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
Amoriterne, Kana'anæerne, Girgasjiterne, Hivviterne og Jebusiterne.«

< Genesis 15 >