< Genesis 15 >

1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
Efter at dette var sket, kom Herrens Ord til Abram i et Syn, og sagde: Frygt ikke, Abram, jeg er dit Skjold og din meget store Løn.
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
Og Abram sagde: Herre, Herre, hvad vil du give mig? og jeg gaar hen uden Børn, og den, der forestaar mit Hus, er Elieser af Damaskus.
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
Og Abram sagde: Se, mig har du intet Afkom givet, og se, min vornede arver mig.
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
Og se, Herrens Ord skete til ham og sagde: Denne, han skal ikke arve dig; men den, som skal udkomme af dit Liv, han skal arve dig.
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
Og han førte ham udenfor og sagde: Kære, se til Himmelen, og tæl Stjernerne, om du kan tælle dem; og han sagde til ham: Saa skal dit Afkom vorde.
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
Og han troede paa Herren, og han regnede ham det til Retfærdighed.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
Og han sagde til ham: jeg er Herren, som udførte dig fra Ur i Kaldæa for at give dig dette Land til at eje det.
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
Da sagde han: Herre, Herre, hvorpaa skal jeg kende, at jeg skal eje det?
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
Og han sagde til ham: Tag mig en tre Aar gammel Kvie og en tre Aar gammel Ged og en tre Aar gammel Vædder og en Turteldue og en Dueunge.
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
Og han tog ham alt dette og delte det midt over og lagde den ene Del deraf tvært overfor den anden; men Fuglene delte han ikke.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
Og Rovfugle sloge ned paa de døde Kroppe; men Abram jog dem derfra.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
Og det skete, der Solen vilde gaa ned, da faldt en dyb Søvn paa Abram, og se, der faldt Forfærdelse og stort Mørke over ham.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
Da sagde han til Abram: du skal visseligen vide, at dit Afkom skal være fremmed i et Land, som ikke er deres, og de skulle trælle for dem, der skulle plage dem, fire Hundrede Aar.
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
Men jeg vil ogsaa dømme det Folk, som de skulle tjene; og derefter skulle de udgaa med meget Gods.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
Men du skal fare til dine Fædre med Fred, og du skal blive begravet i en god Alderdom.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
Og i den fjerde Slægt skulle de komme hid igen; thi Amoritens Ondskab er endnu ikke fuld.
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
Og det skete, der Solen var nedgangen, og der var stort Mørke, se, da var der en rygende Ovn og Ilds Blus, som for hen imellem disse Stykker.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
Paa den samme Dag gjorde Herren en Pagt med Abram og sagde: Dit Afkom har jeg givet dette Land, fra Ægyptens Flod indtil den store Flod, den Flod Frat,
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
Keniter og Kenisiter og Kadmoniter
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
og Hethiter og Feresiter og Refaiter
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
og Amoriter og Kananiter og Girgasiter og Jebusiter.

< Genesis 15 >