< Genesis 13 >

1 Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
Y Abram subió de Egipto con su mujer y todo lo que tenía, y Lot con él, y vinieron a Neguev.
2 Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
Y Abram tenía grandes riquezas de ganado y plata y oro.
3 Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
Y viajando de Neguev, vino a Bet-el, al lugar donde antes estaba su tienda, entre Bet-el y Hai;
4 ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
al lugar donde había hecho su primer altar, y allí Abram adoró el nombre del Señor.
5 Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
Y Lot, que iba con él, tuvo rebaños, vacas y tiendas;
6 Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
Así que la tierra no era lo suficientemente amplia para ellos dos: su propiedad era tan grande que no había lugar para ellos juntos.
7 Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
Hubo una discusión entre los guardianes del ganado de Abram y los guardianes del ganado de Lot: en aquel tiempo los cananeos y los ferezeos aún vivían en la tierra.
8 Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
Entonces Abram dijo a Lot: No haya discusión entre tú y yo, y entre mis pastores y tus pastores, porque somos hermanos.
9 Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
¿No está toda la tierra delante de ti? luego sigamos nuestros caminos por separado: si vas a la izquierda, iré a la derecha; o si tomas el derecho, iré a la izquierda.
10 Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
Y Lot, levantando los ojos y mirando el valle del Jordán, vio que estaba bien regado en todas partes, antes que el Señor enviará destrucción sobre Sodoma y Gomorra; era como el jardín del Señor, como la tierra de Egipto, en el camino a Zoar.
11 Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
Entonces Lot tomó todo el valle del Jordán, y se fue al oriente, y se separaron unos de otros.
12 Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
Abram vivió en la tierra de Canaán, y Lot fue a las ciudades de las tierras bajas, y se mudó de su tienda hasta Sodoma.
13 Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
Y los hombres de Sodoma eran malos, y pecadores en gran manera delante del Señor.
14 Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
Y el Señor le dijo a Abram, después de que Lot se separó de él, desde este lugar donde miras hacia el norte y hacia el sur, hacia el este y hacia el oeste:
15 Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
Porque toda la tierra que ves te daré a ti y a tu descendencia para siempre.
16 Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
Y haré tus hijos como el polvo de la tierra, para que si el polvo de la tierra se numera, tus hijos serán contados.
17 Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
Ven, recorre toda la tierra de un extremo al otro porque yo te lo daré.
18 Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.
Y Abram, moviendo su tienda, vino e hizo su morada junto al árbol santo de Mamre, que está en Hebrón, e hizo allí un altar para el Señor.

< Genesis 13 >