< Genesis 13 >
1 Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
Abram monta donc de l’Égypte, lui, sa femme et tout ce qu’il avait, et Lot avec lui, vers la région australe.
2 Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
Or Abram était très riche en possession d’or et d’argent.
3 Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
Il s’en retourna par le même chemin qu’il était venu, du midi à Béthel, jusqu’au lieu où auparavant il avait planté sa tente, entre Béthel et Haï;
4 ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
Au lieu où il avait fait d’abord un autel, et il invoqua là le nom du Seigneur.
5 Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
Mais Lot qui était avec Abram, avait aussi des troupeaux de brebis et de gros bétail, et des tentes.
6 Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
Et ce pays ne leur permettait pas de demeurer ensemble; car leurs biens étaient nombreux, et ils ne pouvaient habiter en commun.
7 Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
De là il s’éleva une querelle entre les pasteurs des troupeaux d’Abram et de Lot. Or en ce temps-là les Chananéens et les Phéréséens habitaient en ce pays.
8 Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
Abram dit donc à Lot: Je te prie, qu’il n’y ait pas de débat entre moi et toi, ni entre mes pasteurs et tes pasteurs; car nous sommes frères.
9 Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
Voici que tout le pays est devant toi: sépare-toi de moi, je te conjure; si tu vas à gauche, j’irai à droite, et si tu choisis la droite, je prendrai la gauche.
10 Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
C’est pourquoi Lot, les yeux levés, vit toute la contrée qui s’étendait le long du Jourdain, et qui, avant que le Seigneur eût détruit Sodome et Gomorrhe, était toute arrosée, comme le paradis du Seigneur, et comme l’Égypte, en venant vers Ségor.
11 Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
Lot choisit pour lui les environs du Jourdain, et s’éloigna de l’orient: c’est ainsi qu’ils se séparèrent l’un de l’autre.
12 Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
Abram habita dans la terre de Chanaan, et Lot demeura dans les villes qui étaient aux environs du Jourdain, et il habita dans Sodome.
13 Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
Or les habitants de Sodome étaient très méchants, et très grands pécheurs devant le Seigneur.
14 Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
Et le Seigneur dit à Abram, après que Lot fut séparé de lui: Lève les yeux et regarde du lieu où tu es maintenant, vers l’aquilon et le midi, vers l’orient et l’occident.
15 Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
Tout le pays que tu aperçois, je te le donnerai, à toi et à ta postérité pour toujours.
16 Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
Je ferai ta postérité comme la poussière de la terre; si quelqu’un d’entre les hommes peut nombrer la poussière de la terre, il pourra aussi nombrer ta postérité.
17 Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
Lève-toi, et parcours le pays en sa longueur et en sa largeur, parce que c’est à toi que je le dois donner.
18 Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.
Levant donc sa tente, Abram vint et habita près de la vallée de Mambré, qui est en Hébron, et il bâtit là un autel au Seigneur.