< Genesis 13 >

1 Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
So Abram and Sarai left Egypt, and they took along all his possessions, and Lot went with them to the Negev [Desert].
2 Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
Abram was very rich. He owned a lot of livestock, silver and gold.
3 Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
They continued traveling from place to place from the Negev [Desert] toward Bethel [town] to the place between Bethel and Ai where they had previously set up their tents,
4 ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
and where Abram had made a stone altar and worshiped Yahweh.
5 Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
Lot, who was traveling with Abram, also had flocks of sheep and goats and herds of cattle, and tents.
6 Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
But they had so many animals that they could not all stay in the same area. There was not enough land to provide water and food for all their animals.
7 Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
Furthermore, the descendants of Canaan and Perizzi were also living in that area, and the land really belonged to them. And the men who took care of Abram’s animals started quarreling with the men who took care of Lot’s animals.
8 Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
So Abram said to Lot, “Since we are close relatives, it is not good for us two to quarrel, or for the men who take care of your animals to quarrel with the men who take care of my animals.
9 Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
There is plenty of land for both of us. So we should separate. You can choose whatever part you want [RHQ]. If you want the area over there, I will stay here. If you want the area here, I will go over there.”
10 Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
Lot looked around toward Zoar [town], and saw that there was plenty of water all over the plain near the Jordan [River]. It was like the park/garden in Eden, and like the land in Egypt. [That was before Yahweh destroyed [the cities of] Sodom and Gomorrah which were on that plain.]
11 Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
So Lot chose the land in the plain of the Jordan [River]. He left his uncle, Abram, and moved east.
12 Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
Abram stayed in the Canaan area, and Lot started to live near the cities in the plain of the Jordan [River], and he set up his tents near Sodom [city].
13 Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
[You need to know that] people who lived there were extremely wicked.
14 Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
After Abram and Lot separated, Yahweh said to Abram, “Look around at this whole area where you are. Look north and south, look east and west.
15 Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
I will give to you and your descendants all the land that you see; I will give it to you forever.
16 Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
I will cause your descendants to be as numerous as particles of dust! [It will be easier] to count the particles of dust than it will be to count your descendants [HYP].
17 Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
Walk through the land in every direction, because I am going to give it all to you.”
18 Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.
So Abram [and his men] took down their tents and moved to Hebron and started to live by the huge trees [at the town] Mamre. He placed a stone altar there to [make sacrifices to] Yahweh.

< Genesis 13 >