< Genesis 13 >

1 Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
Avram [Exalted father] went up out of Egypt [Abode of slavery]— he, his wife, all that he had, and Lot [Veil, Covering] with him— into the South.
2 Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
Avram [Exalted father] was very rich in livestock, in silver, and in gold.
3 Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
He went on his journeys from the South even to Beth-el [House of God], to the place where his tent had been at the beginning, between Beth-el [House of God] and Ai,
4 ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
to the place of the altar, which he had made there at the first. There Avram [Exalted father] called on Adonai’s name.
5 Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
Lot [Veil, Covering] also, who went with Avram [Exalted father], had flocks, herds, and tents.
6 Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
The land was not able to bear them, that they might live together; for their substance was great, so that they could not live together.
7 Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
There was strife between the herdsmen of Avram [Exalted father]’s livestock and the herdsmen of Lot [Veil, Covering]’s livestock. The Canaanites [Descendants of Humbled] and the Perizzites [Descendants of Belonging to village] lived in the land at that time.
8 Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
Avram [Exalted father] said to Lot [Veil, Covering], “Please, let there be no strife between you and me, and between your herdsmen and my herdsmen; for we are relatives.
9 Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
Is not the whole land before you? Please separate yourself from me. If you go to the left hand, then I will go to the right. Or if you go to the right hand, then I will go to the left.”
10 Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
Lot [Veil, Covering] lifted up his eyes, and saw all the plain of the Jordan [Descender], that it was well-watered everywhere, before Adonai destroyed Sodom [Burning] and Gomorrah [Rebellious people, Tyrants], like the garden of Adonai, like the land of Egypt [Abode of slavery], as you go to Zoar [Small].
11 Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
So Lot [Veil, Covering] chose the Plain of the Jordan [Descender] for himself. Lot [Veil, Covering] traveled east, and they separated themselves the one from the other.
12 Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
Avram [Exalted father] lived in the land of Canaan [Humbled], and Lot [Veil, Covering] lived in the 'Ieyr HaKikar [Cities of the Round], and moved his tent as far as Sodom [Burning].
13 Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
Now the men of Sodom [Burning] were exceedingly wicked and people who sin ·intentionally miss the mark goal· against Adonai.
14 Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
Adonai said to Avram [Exalted father], after Lot [Veil, Covering] was separated from him, “Now, lift up your eyes, and look from the place where you are, northward and southward and eastward and westward,
15 Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
for all the land which you see, I will give to you, and to your offspring forever.
16 Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
I will make your offspring as the dust of the earth, so that if a man can count the dust of the earth, then your offspring may also be counted.
17 Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
Arise, walk through the land in its length and in its width; for I will give it to you.”
18 Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.
Avram [Exalted father] moved his tent, and came and lived by the oaks of Mamre [Bitter, Fatness], which are in Hebron, and built an altar there to Adonai.

< Genesis 13 >