< Genesis 12 >
1 Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.
Now the LORD had said to Abram, Depart from thy country, and from thy kindred, and from thy father's house, to a land that I will show thee:
2 “Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu ndipo ndidzakudalitsa; ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.
And I will make of thee a great nation, and I will bless thee, and make thy name great; and thou shalt be a blessing:
3 Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe, ndi kutemberera amene adzatemberera iwe; ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iwe.”
And I will bless them that bless thee, and curse him that curseth thee: and in thee shall all families of the earth be blessed.
4 Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75.
So Abram departed, as the LORD had spoken to him, and Lot went with him: and Abram [was] seventy and five years old when he departed from Haran.
5 Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.
And Abram took Sarai his wife, and Lot his brother's son, and all their substance that they had gathered, and the souls that they had gotten in Haran; and they went to go forth into the land of Canaan; and into the land of Canaan they came.
6 Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo.
And Abram passed through the land to the place of Sichem, to the plain of Moreh. And the Canaanite [was] then in the land.
7 Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.
And the LORD appeared to Abram, and said, To thy seed will I give this land: and there he erected an altar to the LORD, who appeared to him.
8 Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo.
And he removed from thence to a mountain on the east of Beth-el, and pitched his tent, [having] Beth-el on the west, and Hai on the east: and there he erected an altar to the LORD, and called upon the name of the LORD.
9 Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.
And Abram journeyed, going on still towards the south.
10 Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri.
And there was a famine in the land: and Abram went down into Egypt to dwell there; for the famine [was] grievous in the land.
11 Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri.
And it came to pass, when he had come near to enter into Egypt, that he said to Sarai his wife, Behold now, I know that thou [art] a fair woman to look upon:
12 Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo.
Therefore it will come to pass, when the Egyptians shall see thee, that they will say, This [is] his wife: and they will kill me, but they will save thee alive.
13 Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”
Say, I pray thee, thou [art] my sister: that it may be well with me for thy sake; and my soul shall live because of thee.
14 Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi.
And it came to pass, that when Abram had come into Egypt, the Egyptians beheld the woman that she [was] very fair.
15 Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao.
The princes also of Pharaoh saw her, and commended her before Pharaoh: and the woman was taken into Pharaoh's house.
16 Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.
And he treated Abram well for her sake: and he had sheep, and oxen, and he-asses, and men-servants, and maid-servants, and she-asses, and camels.
17 Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu.
And the LORD afflicted Pharaoh and his house with great plagues, because of Sarai, Abram's wife.
18 Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako?
And Pharaoh called Abram, and said, What [is] this [that] thou hast done to me? why didst thou not tell me that she [is] thy wife?
19 Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!”
Why saidst thou, She [is] my sister? so I might have taken her to me for a wife: now therefore behold thy wife, take [her], and go thy way.
20 Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.
And Pharaoh commanded [his] men concerning him: and they sent him away, and his wife, and all that he had.