< Genesis 12 >
1 Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.
Now God had said to Abram, "Go out from your country, and from your relatives, and from your father's house, to the land that I will show you.
2 “Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu ndipo ndidzakudalitsa; ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.
And I will make of you a great nation. And I will bless you and make your name great. And you will be a blessing.
3 Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe, ndi kutemberera amene adzatemberera iwe; ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iwe.”
And I will bless those who bless you, and I will curse those who treat you with contempt, and through you all the families of the earth will be blessed."
4 Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75.
So Abram left, as God had told him, and Lot went with him. Abram was seventy-five years old when he departed from Haran.
5 Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.
Abram took Sarai his wife, Lot his brother's son, and all their possessions that they had accumulated, and the people whom they had acquired in Haran, and they left to go to the land of Canaan. And they came to the land of Canaan,
6 Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo.
and Abram passed through the land to the place of Shechem, to the oak of Moreh. At that time the Canaanites were in the land.
7 Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.
Then God appeared to Abram and said to him, "I will give this land to your offspring." He built an altar there God, who appeared to him.
8 Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo.
He left from there to the mountain on the east of Bethel, and pitched his tent, having Bethel on the west, and Ai on the east. There he built an altar and called on the name of God.
9 Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.
And Abram traveled on, continuing toward the Negev.
10 Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri.
There was a famine in the land, so Abram went down into Egypt to sojourn there, because the famine was severe in the land.
11 Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri.
It happened, when he had come near to enter Egypt, that he said to Sarai his wife, "Look, I know what a beautiful woman you are.
12 Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo.
It will happen, when the Egyptians will see you, that they will say, 'This is his wife.' And they will kill me, but they will let you live.
13 Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”
Please say that you are my sister, that it may be well with me for your sake, and that I may live because of you."
14 Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi.
It happened that when Abram had come into Egypt, the Egyptians saw that the woman was very beautiful.
15 Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao.
The princes of Pharaoh saw her, and praised her to Pharaoh; and the woman was taken into the household of Pharaoh.
16 Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.
He dealt well with Abram for her sake, and he acquired sheep, cattle, male donkeys, male servants, female servants, female donkeys, and camels.
17 Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu.
But God plagued Pharaoh and his house with great and grievous plagues because of Sarai, Abram's wife.
18 Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako?
Pharaoh summoned Abram and said, "What is this that you have done to me? Why did you not tell me that she was your wife?
19 Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!”
Why did you say, 'She is my sister,' so that I took her to be my wife? Now therefore, look, your wife is before you. Take, and go."
20 Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.
Pharaoh commanded men concerning him, and they sent him away with his wife and all his possessions.