< Genesis 12 >

1 Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.
Now the Lord had said unto Abram, Get thee out of thy country, and out of thy birthplace, and from thy father's house, unto the land that I will show thee.
2 “Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu ndipo ndidzakudalitsa; ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.
And I will make of thee a great nation, and I will bless thee, and make thy name great; and thou shalt be a blessing:
3 Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe, ndi kutemberera amene adzatemberera iwe; ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iwe.”
And I will bless those that bless thee, and him that curseth thee, will I curse; and in thee shall all families of the earth be blessed.
4 Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75.
So Abram departed, as the Lord had spoken unto him, and Lot went with him; and Abram was seventy and five years old at his departure out of Charan.
5 Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.
And Abram took Sarai his wife, and Lot his brother's son, and all their substance that they had acquired, and the persons that they had obtained in Charan; and they went forth to go into the land of Canaan; and they came into the land of Canaan.
6 Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo.
And Abram passed through the land unto the place of Shechem, unto the plain of Moreh; and the Canaanite was then in the land.
7 Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.
And the Lord appeared unto Abram, and said, Unto thy seed will I give this land. And he built there an altar unto the Lord, who had appeared unto him.
8 Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo.
And he removed from there unto the mountain on the east of Beth-el, and pitched his tent, having Beth-el on the west, and 'Ai on the east; and he built there an altar unto the Lord, and called upon the name of the Lord.
9 Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.
And Abram journeyed farther, still going on toward the south.
10 Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri.
And there arose a famine in the land: and Abram went down into Egypt to sojourn there; for the famine was grievous in the land.
11 Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri.
And it came to pass, when he was come near to enter into Egypt, that he said unto Sarai his wife, Behold now, I know that thou art a woman of handsome appearance:
12 Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo.
And it may come to pass, when the Egyptians shall see thee, that they will say, This is his wife; and they may kill me, but thee they will save alive.
13 Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”
Say then, I pray thee, thou art my sister, that it may go well with me for thy sake, and my soul live because of thee.
14 Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi.
And it came to pass, when Abram was come into Egypt, that the Egyptians beheld the woman that she was very fair.
15 Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao.
The princes also of Pharaoh saw her, and commended her to Pharaoh; and the woman was taken into Pharaoh's house.
16 Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.
And he did well to Abram for her sake; and he received sheep, and oxen, and he-asses, and men-servants, and maid-servants, and she-asses, and camels.
17 Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu.
But the Lord plagued Pharaoh and his house with great plagues because of Sarai, Abram's wife.
18 Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako?
And Pharaoh called Abram, and said, What is this thou hast done unto me? Why didst thou not tell me that she is thy wife?
19 Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!”
Why saidst thou, She is my sister? and so I took her to me for a wife; now, therefore, behold, here is thy wife, take her, and go thy way.
20 Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.
And Pharaoh commanded some men concerning him, who accompanied him and his wife, and all that he had.

< Genesis 12 >