< Genesis 11 >

1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
Es hatte aber alle Welt einerlei Zunge und Sprache.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
Da sie nun zogen gen Morgen, fanden sie ein eben Land im Lande Sinear und wohneten daselbst,
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
und sprachen untereinander: Wohlauf, laßt uns Ziegel streichen und brennen! Und nahmen Ziegel zu Stein und Ton zu Kalk
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
und sprachen: Wohlauf, laßt uns eine Stadt und Turm bauen, des Spitze bis an den Himmel reiche, daß wir uns einen Namen machen; denn wir werden vielleicht zerstreuet in alle Länder.
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
Da fuhr der HERR hernieder, daß er sähe die Stadt und Turm, die die Menschenkinder baueten.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
Und der HERR sprach: Siehe, es ist einerlei Volk und einerlei Sprache unter ihnen allen, und haben das angefangen zu tun; sie werden nicht ablassen von allem, das sie vorgenommen haben zu tun.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Wohlauf, laßt uns herniederfahren und ihre Sprache daselbst verwirren, daß keiner des andern Sprache vernehme.
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
Also zerstreuete sie der HERR von dannen in alle Länder, daß sie mußten aufhören, die Stadt zu bauen.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
Daher heißt ihr Name Babel, daß der HERR daselbst verwirret hatte aller Länder Sprache und sie zerstreuet von dannen in alle Länder.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
Dies sind die Geschlechter Sems: Sem war hundert Jahre alt und zeugete Arphachsad, zwei Jahre nach der Sintflut;
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach fünfhundert Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
Arphachsad war fünfunddreißig Jahre alt und zeugete Salah;
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach vierhundertunddrei Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
Salah war dreißig Jahre alt und zeugete Eber;
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach vierhundertunddrei Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
Eber war vierunddreißig Jahre alt und zeugete Peleg;
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach vierhundertunddreißig Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
Peleg war dreißig Jahre alt und zeugete Regu;
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach zweihundertundneun Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
Regu war zweiunddreißig Jahre alt und zeugete Serug;
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach zweihundertundsieben Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
Serug war dreißig Jahre alt und zeugete Nahor;
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach zweihundert Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
Nahor war neunundzwanzig Jahre alt und zeugete Tharah;
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
und lebte danach hundertundneunzehn Jahre und zeugete Söhne und Töchter.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
Tharah war siebenzig Jahre alt und zeugete Abram, Nahor und Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
Dies sind die Geschlechter Tharahs: Tharah zeugete Abram, Nahor und Haran. Aber Haran zeugete Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
Haran aber starb vor seinem Vater Tharah in seinem Vaterland zu Ur in Chaldäa.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
Da nahmen Abram und Nahor Weiber. Abrams Weib hieß Sarai und Nahors Weib Milka, Harans Tochter, der ein Vater war der Milka und der Jiska.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
Aber Sarai war unfruchtbar und hatte kein Kind.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
Da nahm Tharah seinen Sohn Abram und Lot, seines Sohns Harans Sohn, und seine Schnur Sarai, seines Sohns Abrams Weib, und führete sie von Ur aus Chaldäa, daß er ins Land Kanaan zöge; und sie kamen gen Haran und wohneten daselbst.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
Und Tharah ward zweihundertundfünf Jahre alt und starb in Haran.

< Genesis 11 >