< Genesis 11 >
1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
The whole earth was of one language and of one speech.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
As they traveled east, they found a plain in the land of Shinar, and they lived there.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
They said to one another, “Come, let’s make bricks, and burn them thoroughly.” They had brick for stone, and they used tar for mortar.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
They said, “Come, let’s build ourselves a city, and a tower whose top reaches to the sky, and let’s make a name for ourselves, lest we be scattered abroad on the surface of the whole earth.”
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
The LORD came down to see the city and the tower, which the children of men built.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
The LORD said, “Behold, they are one people, and they all have one language, and this is what they begin to do. Now nothing will be withheld from them, which they intend to do.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Come, let’s go down, and there confuse their language, that they may not understand one another’s speech.”
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
So the LORD scattered them abroad from there on the surface of all the earth. They stopped building the city.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
Therefore its name was called Babel, because there the LORD confused the language of all the earth. From there, the LORD scattered them abroad on the surface of all the earth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
This is the history of the generations of Shem: Shem was one hundred years old when he became the father of Arpachshad two years after the flood.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Shem lived five hundred years after he became the father of Arpachshad, and became the father of more sons and daughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
Arpachshad lived thirty-five years and became the father of Shelah.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Arpachshad lived four hundred three years after he became the father of Shelah, and became the father of more sons and daughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
Shelah lived thirty years, and became the father of Eber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Shelah lived four hundred three years after he became the father of Eber, and became the father of more sons and daughters.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
Eber lived thirty-four years, and became the father of Peleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Eber lived four hundred thirty years after he became the father of Peleg, and became the father of more sons and daughters.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
Peleg lived thirty years, and became the father of Reu.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Peleg lived two hundred nine years after he became the father of Reu, and became the father of more sons and daughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
Reu lived thirty-two years, and became the father of Serug.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Reu lived two hundred seven years after he became the father of Serug, and became the father of more sons and daughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
Serug lived thirty years, and became the father of Nahor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Serug lived two hundred years after he became the father of Nahor, and became the father of more sons and daughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
Nahor lived twenty-nine years, and became the father of Terah.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
Nahor lived one hundred nineteen years after he became the father of Terah, and became the father of more sons and daughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
Terah lived seventy years, and became the father of Abram, Nahor, and Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
Now this is the history of the generations of Terah. Terah became the father of Abram, Nahor, and Haran. Haran became the father of Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
Haran died in the land of his birth, in Ur of the Chaldees, while his father Terah was still alive.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
Abram and Nahor married wives. The name of Abram’s wife was Sarai, and the name of Nahor’s wife was Milcah, the daughter of Haran, who was also the father of Iscah.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
Sarai was barren. She had no child.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
Terah took Abram his son, Lot the son of Haran, his son’s son, and Sarai his daughter-in-law, his son Abram’s wife. They went from Ur of the Chaldees, to go into the land of Canaan. They came to Haran and lived there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
The days of Terah were two hundred five years. Terah died in Haran.