< Genesis 11 >
1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
And all the world was of one tonge and one language.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
And as they came from the east they founde a playne in the lande of Synear and there they dwelled.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
And they sayd one to a nother: come on let us make brycke ad burne it wyth fyre. So brycke was there stone and slyme was there morter
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
And they sayd: Come on let vs buylde vs a cyte and a toure that the toppe may reach vnto heauen. And let vs make us a name for perauenture we shall be scatered abrode over all the erth.
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
And the LORde came downe to see the cyte and the toure which the childern of Ada had buylded.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
And the LORde sayd: See the people is one and haue one tonge amonge them all. And thys haue they begon to do and wyll not leaue of from all that they haue purposed to do.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Come on let vs descende and myngell theire tonge even there that one vnderstonde not what a nother sayeth.
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
Thus ye LORde skatered them from thence vppon all the erth. And they left of to buylde the cyte.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
Wherfore the name of it is called Babell because that the LORDE there confounded the tonge of all the world. And because that the LORde from thence skatered them abrode vppon all the erth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
These are the generations of Sem: Se was an hundred yere olde and begat Arcphachsad ij. yere after the floude.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Se lyved after he had begot Arphachsad. v. hundred yere an begat sonnes and doughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
And Arphacsad lyued. xxxv. yere and begat Sala
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
and lyved after he had begot Sala iiij. hudred yere and. iij and begat sonnes and doughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
And Sala was. xxx. yere old and begat Eber
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
ad lyued after he had begot Eber. iiij. hudred and thre yere ad begat sonnes and doughters
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
When Eber was. xxxiiij. yere olde he begat Peleg
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
and lyued after he had begot Peleg foure hundred and. xxx. yere and begat sonnes and doughters.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
And Peleg when he was. xxx. yere olde begat Regu
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
and lyued after he had begot Regu. ij. hundred and. ix. yere and begat sonnes and doughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
And Regu when he had lyued. xxxij. yere begat Serug
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
and lyued after he had begot Serug. ij. hundred and. vij. yere and begat sonnes and doughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
And when Serug was. xxx. yere olde he begat Nahor
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
and lyued after he had begot Nahor. ij. hundred yere and begat sonnes and doughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
And Nahor when he was. xxix. yere olde begat Terah
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
and lyved after he had begot Terah an hundred and. xix. yere and begat sonnes and doughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
And when Terah was. lxx. yere olde he begat Abram Nahor and Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
And these are the generations of Terah. Terah begat Abram Nahor and Haran. And Haran begat Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
And Haran dyed before Terah his father in the londe where he was borne at Vr in Chaldea.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
And Abram and Nahor toke them wyves. Abras wyfe was called Sarai. And Nahors wyfe Mylca the doughter of Haran which was father of Milca ad of Iisca.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
But Sarai was baren and had no childe.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
Than toke Terah Abram his sonne and Lot his sonne Harans sonne and Sarai his doughter in lawe his sone Abrams wyfe. And they went wyth hym from Vr in Chaldea to go in to the lade of Chanaan. And they came to Haran and dwelled there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
And when Terah was ij. hundred yere old and. v. he dyed in Haran.