< Genesis 11 >
1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
And the whole earth is of one language, and of the same words,
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
and it comes to pass, in their journeying from the east, that they find a valley in the land of Shinar and dwell there;
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
and they each say to his neighbor, “Give help, let us make bricks, and burn [them] thoroughly”: and the brick is to them for stone, and the bitumen has been to them for mortar.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
And they say, “Give help, let us build for ourselves a city and tower with its head in the heavens, and make for ourselves a name, lest we be scattered over the face of all the earth.”
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
And YHWH comes down to see the city and the tower which the sons of men have built;
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
and YHWH says, “Behold, the people [is] one, and one language [is] to them all, and this it has dreamed of doing; and now, nothing is restrained from them of that which they have purposed to do.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Give help, let us go down there and confuse their language, so that a man will not understand the language of his companion.”
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
And YHWH scatters them from there over the face of all the earth, and they cease to build the city;
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
therefore [one] has called its name Babel, for there YHWH has confused the language of all the earth, and from there YHWH has scattered them over the face of all the earth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
These [are] the generations of Shem: Shem [is] a son of one hundred years, and begets Arphaxad two years after the flood.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Shem lives after his begetting Arphaxad five hundred years, and begets sons and daughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
And Arphaxad has lived thirty-five years [[or one hundred and thirty-five years]], and begets Salah.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Arphaxad lives after his begetting Salah four hundred and three years [[or four hundred and thirty years]], and begets sons and daughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
And Salah has lived thirty years [[or one hundred and thirty years]], and begets Eber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Salah lives after his begetting Eber four hundred and three years [[or three hundred and thirty years]], and begets sons and daughters.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
And Eber lives thirty-four years [[or one hundred and thirty-four years]], and begets Peleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Eber lives after his begetting Peleg four hundred and thirty years [[or three hundred and seventy years]], and begets sons and daughters.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
And Peleg lives thirty years [[or one hundred and thirty years]], and begets Reu.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Peleg lives after his begetting Reu two hundred and nine years, and begets sons and daughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
And Reu lives thirty-two years [[or one hundred and thirty-two years]], and begets Serug.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Reu lives after his begetting Serug two hundred and seven years, and begets sons and daughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
And Serug lives thirty years [[or one hundred and thirty years]], and begets Nahor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Serug lives after his begetting Nahor two hundred years, and begets sons and daughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
And Nahor lives twenty-nine years [[or seventy-nine years]], and begets Terah.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Nahor lives after his begetting Terah one hundred and nineteen years [[or one hundred and twenty-nine years]], and begets sons and daughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
And Terah lives seventy years, and begets Abram, Nahor, and Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
And these [are] the generations of Terah: Terah has begotten Abram, Nahor, and Haran; and Haran has begotten Lot;
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
and Haran dies in the presence of Terah his father, in the land of his birth, in Ur of the Chaldees.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
And Abram and Nahor take to themselves wives; the name of Abram’s wife [is] Sarai, and the name of Nahor’s wife [is] Milcah, daughter of Haran, father of Milcah, and father of Iscah.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
And Sarai is barren—she has no child.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
And Terah takes his son Abram, and Lot, son of Haran, his son’s son, and his daughter-in-law Sarai, wife of his son Abram, and they go out with them from Ur of the Chaldees, to go toward the land of Canaan; and they come to Haran, and dwell there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
And the days of Terah are two hundred and five years, and Terah dies in Haran.