< Genesis 11 >
1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
And the whole earth was of one language, and of one kind of words.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
And it came to pass, as they journeyed toward the east, that they found a plain in the land of Shinar, and they dwelt there.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
And they said to one another, Go to, let us make bricks, and burn them thoroughly. And thus the brick served them for stone, and slime served them for mortar.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
And they said, Go to, let us build ourselves a city, and a tower, the top of which may reach unto heaven; and let us make ourselves a name, lest we be scattered abroad upon the face of the whole earth.
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
And the Lord came down to see the city and the tower, which the children of man were building.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
And the Lord said, Behold, it is one people, and they have all one language, and this is the first thing they undertake to do; and now shall they not be restrained in all which they have imagined to do?
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Go to, let us go down, and confound there their language, that they may not understand one another's speech.
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
So the Lord scattered them abroad from there over the face of all the earth; and they left off to build the city.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
Therefore is the name of it called Babel, because the Lord did there confound the language of all the earth; and from there did the Lord scatter them abroad over the face of all the earth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
These are the generations of Shem: Shem, when a hundred years old, begat Arpachshad, two years after the flood.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Shem lived after he had begotten Arpachshad five hundred years; and begat sons and daughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
And Arpachshad lived five and thirty years, and begat Shelach.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Arpachshad lived after he had begotten Shelach four hundred and three years; and begat sons and daughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
And Shelach lived thirty years, and begat Eber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Shelach lived after he had begotten Eber four hundred and three years; and begat sons and daughters.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
And Eber lived four and thirty years, and begat Peleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Eber lived after he had begotten Peleg four hundred and thirty years; and begat sons and daughters.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
And Peleg lived thirty years, and begat Reu.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Peleg lived after he had begotten Reu two hundred and nine years; and begat sons and daughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
And Reu lived two and thirty years, and begat Serug.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Reu lived after he had begotten Serug two hundred and seven years; and begat sons and daughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
And Serug lived thirty years, and begat Nachor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Serug lived after he had begotten Nachor two hundred years; and begat sons and daughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
And Nachor lived nine and twenty years, and begat Terach.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Nachor lived after he had begotten Terach a hundred and nineteen years; and begat sons and daughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
And Terach lived seventy years, and begat Abram, Nachor, and Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
Now these are the generations of Terach: Terach begat Abram, Nachor, and Haran; and Haran begat Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
And Haran died before his father Terach in the land of his nativity, in Ur of the Chaldees.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
And Abram and Nachor took themselves wives; the name of Abram's wife was Sarai; and the name of Nachor's wife was Milcah, the daughter of Haran, the father of Milcah, and the father of Yiscah.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
But Sarai was barren; she had no child.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
And Terach took Abram his son, and Lot, the son of Haran, his son's son, and Sarai his daughter-in-law, the wife of his son Abram; and they went forth with them from Ur of the Chaldees, to go into the land of Canaan; and they came unto Charan, and dwelt there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
And the days of Terach were two hundred and five years; and Terach died in Charan.