< Genesis 11 >

1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
And all the earth was one lip, and there was one language to all.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
And it came to pass as they moved from the east, they found a plain in the land of Senaar, and they lived there.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
And a man said to his neighbor, Come, let us make bricks and bake them with fire. And the brick was to them for stone, and their mortar was bitumen.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
And they said, Come, let us build to ourselves a city and tower, whose top shall be to heaven, and let us make to ourselves a name, before we are scattered abroad upon the face of all the earth.
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
And the Lord came down to see the city and the tower, which the sons of men built.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
And the Lord said, Behold, [there is] one race, and one lip of all, and they have begun to do this, and now nothing shall fail from them of all that they may have undertaken to do.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Come, and having gone down let us there confound their tongue, that they may not understand each the voice of his neighbor.
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
And the Lord scattered them thence over the face of all the earth, and they left off building the city and the tower.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
On this account its name was called Confusion, because there the Lord confounded the languages of all the earth, and thence the Lord scattered them upon the face of all the earth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
And these [are] the generations of Sem: and Sem was a hundred years old when he begot Arphaxad, the second year after the flood.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Sem lived, after he had begotten Arphaxad, five hundred years, and begot sons and daughters, and died.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
And Arphaxad lived a hundred and thirty-five years, and begot Cainan.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Arphaxad lived after he had begotten Cainan, four hundred years, and begot sons and daughters, and died. And Cainan lived a hundred and thirty years and begot Sala; and Canaan lived after he had begotten Sala, three hundred and thirty years, and begot sons and daughters, and died.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
And Sala lived an hundred and thirty years, and begot Heber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Sala lived after he had begotten Heber, three hundred and thirty years, and begot sons and daughters, and died.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
And Heber lived an hundred and thirty-four years, and begot Phaleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Heber lived after he had begotten Phaleg two hundred and seventy years, and begot sons and daughters, and died.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
And Phaleg lived and hundred and thirty years, and begot Ragau.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Phaleg lived after he had begotten Ragau, two hundred and nine years, and begot sons and daughters, and died.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
And Ragau lived and hundred thirty and two years, and begot Seruch.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Raau lived after he had begotten Seruch, two hundred and seven years, and begot sons and daughters, and died.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
And Seruch lived a hundred and thirty years, and begot Nachor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Seruch lived after he had begotten Nachor, two hundred years, and begot sons and daughters, and died.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
And Nachor lived a hundred and seventy-nine years, and begot Tharrha.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Nachor lived after he had begotten Tharrha, an hundred and twenty-five years, and begot sons and daughters, and he died.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
And Tharrha lived seventy years, and begot Abram, and Nachor, and Arrhan.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
And these [are] the generations of Tharrha. Tharrha begot Abram and Nachor, and Arrhan; and Arrhan begot Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
And Arrhan died in the presence of Tharrha his father, in the land in which he was born, in the country of the Chaldees.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
And Abram and Nachor took to themselves wives, the name of the wife of Abram was Sara, and the name of the wife of Nachor, Malcha, daughter of Arrhan, and he was the father of Malcha, the father of Jescha.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
And Sara was barren, and did not bear children.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
And Tharrha took Abram his son, and Lot the son Arrhan, the son of his son, and Sara his daughter-in-law, the wife of Abram his son, and led them forth out of the land of the Chaldees, to go into the land of Chanaan, and they came as far as Charrhan, and he lived there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
And all the days of Tharrha in the land of Charrhan were two hundred and five years, and Tharrha died in Charrhan.

< Genesis 11 >