< Genesis 11 >
1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
Then the whole earth was of one language and one speache.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
And as they went from the East, they found a plaine in the land of Shinar, and there they abode.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
And they said one to another, Come, let vs make bricke, and burne it in the fire. So they had bricke for stone, and slime had they in steade of morter.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
Also they said, Goe to, let vs builde vs a citie and a towre, whose top may reache vnto the heauen, that we may get vs a name, lest we be scattered vpon the whole earth.
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
But the Lord came downe, to see the citie and towre, which the sonnes of men builded.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
And the Lord said, Beholde, the people is one, and they all haue one language, and this they begin to doe, neither can they now be stopped from whatsoeuer they haue imagined to do.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Come on, let vs goe downe, and there confound their language, that euery one perceiue not anothers speache.
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
So ye Lord scattered them from thence vpon all the earth, and they left off to build the citie.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
Therefore the name of it was called Babel, because the Lord did there confounde the language of all the earth: from thence then did the Lord scatter them vpon all the earth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
These are the generations of Shem: Shem was an hundreth yeere olde, and begate Arpachshad two yeere after the flood.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Shem liued, after he begate Arpachshad, fiue hundreth yeeres, and begate sonnes and daughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
Also Arpachshad liued fiue and thirtie yeeres, and begate Shelah.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Arpachshad liued, after he begate Shelah, foure hundreth and three yeeres, and begate sonnes and daughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
And Shelah liued thirtie yeeres, and begat Eber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
So Shelah liued, after he begat Eber, foure hundreth and three yeeres, and begat sonnes and daughters.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
Likewise Eber liued foure and thirtie yeres, and begate Peleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
So Eber liued, after he begate Peleg, foure hundreth and thirtie yeeres, and begate sonnes and daughters
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
And Peleg liued thirtie yeeres, and begate Reu.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Peleg liued, after he begate Reu, two hundreth and nine yeeres, and begate sonnes and daughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
Also Reu liued two and thirtie yeeres, and begate Serug.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
So Reu liued, after he begate Serug, two hundreth and seuen yeeres, and begate sonnes and daughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
Moreouer Serug liued thirtie yeeres, and begate Nahor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Serug liued, after he begate Nahor, two hundreth yeeres, and begate sonnes and daughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
And Nahor liued nine and twentie yeeres, and begate Terah.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
So Nahor liued, after he begate Terah, an hundreth and nineteene yeeres, and begat sonnes and daughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
So Terah liued seuentie yeeres, and begate Abram, Nahor, and Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
Nowe these are the generations of Terah: Terah begate Abram, Nahor, and Haran: and Haran begate Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
Then Haran died before Terah his father in the land of his natiuitie, in Vr of the Caldees.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
So Abram and Nahor tooke them wiues. The name of Abrams wife was Sarai, and the name of Nahors wife Milcah, the daughter of Haran, the father of Milcah, and the father of Iscah.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
But Sarai was barren, and had no childe.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
Then Terah tooke Abram his sonne, and Lot the sonne of Haran, his sonnes sonne, and Sarai his daughter in lawe, his sonne Abrams wife: and they departed together from Vr of the Caldees, to goe into the land of Canaan, and they came to Haran, and dwelt there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
So the dayes of Terah were two hundreth and fiue yeeres, and Terah died in Haran.