< Genesis 11 >
1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
And the earth was of one tongue, and of the same speech.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
And when they removed from the east, they found a plain in the land of Sennaar, and dwelt in it.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
And each one said to his neighbour: Come, let us make brick, and bake them with fire. And they had brick instead of stones, and slime instead of mortar.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
And they said: Come, let us make a city and a tower, the top whereof may reach to heaven: and let us make our name famous before we be scattered abroad into all lands.
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
And the Lord came down to see the city and the tower, which the children of Adam were building.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
And he said: Behold, it is one people, and all have one tongue: and they have begun to do this, neither will they leave off from their designs, till they accomplish them in deed.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Come ye, therefore, let us go down, and there confound their tongue, that they may not understand one another’s speech.
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
And so the Lord scattered them from that place into all lands, and they ceased to build the city.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
And therefore the name thereof was called Babel, because there the language of the whole earth was confounded: and from thence the Lord scattered them abroad upon the face of all countries.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
These are the generations of Sem: Sem was a hundred years old when he begot Arphaxad, two years after the flood.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Sem lived after he begot Arphaxad, five hundred years, and begot sons and daughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
And Arphaxad lived thirty-five years, and begot Sale.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Arphaxad lived after he begot Sale, three hundred and three years; and begot sons and daughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
Sale also lived thirty years, and begot Heber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Sale lived after he begot Heber, four hundred and three years; and begot sons and daughters.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
And Heber lived thirty-four years, and begot Phaleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Heber lived after he begot Phaleg, four hundred and thirty years: and begot sons and daughters.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
Phaleg also lived thirty years, and begot Reu.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Phaleg lived after he begot Reu, two hundred and nine years, and begot sons and daughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
And Reu lived thirty-two years, and begot Sarug.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Reu lived after he begot Sarug, two hundred and seven years, and begot sons and daughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
And Sarug lived thirty years, and begot Nachor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Sarug lived after he begot Nachor, two hundred years: and begot sons and daughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
And Nachor lived nine and twenty years, and begot Thare.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Nachor lived after he begot Thare, a hundred and nineteen years: and begot sons and daughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
And Thare lived seventy years, and begot Abram, and Nachor, and Aran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
And these are the generations of Thare: Thare begot Abram, Nachor, and Aran. And Aran begot Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
And Aran died before Thare his father, in the land of his nativity in Ur of the Chaldees.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
And Abram and Nachor married wives: the name of Abram’s wife was Sarai: and the name of Nachor’s wife, Melcha, the daughter of Aran, father of Melcha, and father of Jescha.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
And Sarai was barren, and had no children.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
And Thare took Abram, his son, and Lot the son of Aran, his son’s son, and Sarai his daughter in law, the wife of Abram his son, and brought them out of Ur of the Chaldees, to go into the land of Chanaan: and they came as far as Haran, and dwelt there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
And the days of Thare were two hundred and five years, and he died in Haran.