< Genesis 11 >

1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
And the whole earth had one language, and the same words.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
And it came to pass as they journeyed from the east, that they found a plain in the land of Shinar, and dwelt there.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
And they said one to another, Come on, let us make bricks, and burn [them] thoroughly. And they had brick for stone, and they had asphalt for mortar.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
And they said, Come on, let us build ourselves a city and a tower, the top of which [may reach] to the heavens; and let us make ourselves a name, lest we be scattered over the face of the whole earth.
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
And Jehovah came down to see the city and the tower which the children of men built.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
And Jehovah said, Behold, the people is one, and have all one language; and this have they begun to do. And now will they be hindered in nothing that they meditate doing.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Come, let us go down, and there confound their language, that they may not understand one another's speech.
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
And Jehovah scattered them thence over the face of the whole earth. And they left off building the city.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
Therefore was its name called Babel; because Jehovah there confounded the language of the whole earth. And Jehovah scattered them thence over the face of the whole earth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
These are the generations of Shem. Shem was a hundred years old, and begot Arphaxad two years after the flood.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Shem lived after he had begotten Arphaxad five hundred years, and begot sons and daughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
And Arphaxad lived thirty-five years, and begot Shelah.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Arphaxad lived after he had begotten Shelah four hundred and three years, and begot sons and daughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
And Shelah lived thirty years, and begot Eber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Shelah lived after he had begotten Eber four hundred and three years, and begot sons and daughters.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
And Eber lived thirty-four years, and begot Peleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Eber lived after he had begotten Peleg four hundred and thirty years, and begot sons and daughters.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
And Peleg lived thirty years, and begot Reu.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Peleg lived after he had begotten Reu two hundred and nine years, and begot sons and daughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
And Reu lived thirty-two years, and begot Serug.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Reu lived after he had begotten Serug two hundred and seven years, and begot sons and daughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
And Serug lived thirty years, and begot Nahor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Serug lived after he had begotten Nahor two hundred years, and begot sons and daughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
And Nahor lived twenty-nine years, and begot Terah.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And Nahor lived after he had begotten Terah a hundred and nineteen years, and begot sons and daughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
And Terah lived seventy years, and begot Abram, Nahor, and Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
And these are the generations of Terah: Terah begot Abram, Nahor, and Haran; and Haran begot Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
And Haran died before the face of his father Terah in the land of his nativity at Ur of the Chaldeans.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
And Abram and Nahor took wives: the name of Abram's wife was Sarai; and the name of Nahor's wife, Milcah, a daughter of Haran, the father of Milcah and the father of Iscah.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
And Sarai was barren: she had no child.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
And Terah took Abram his son, and Lot the son of Haran his son's son, and Sarai his daughter-in-law, his son Abram's wife; and they went forth together out of Ur of the Chaldeans, to go into the land of Canaan, and came as far as Haran, and dwelt there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
And the days of Terah were two hundred and five years; and Terah died in Haran.

< Genesis 11 >