< Genesis 11 >

1 Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
Now the whole world had one language and a common form of speech.
2 Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
And as people journeyed eastward, they found a plain in the land of Shinar and settled there.
3 Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
And they said to one another, “Come, let us make bricks and bake them thoroughly.” So they used brick instead of stone, and tar instead of mortar.
4 Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
“Come,” they said, “let us build for ourselves a city with a tower that reaches to the heavens, that we may make a name for ourselves and not be scattered over the face of all the earth.”
5 Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
Then the LORD came down to see the city and the tower that the sons of men were building.
6 Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
And the LORD said, “If they have begun to do this as one people speaking the same language, then nothing they devise will be beyond them.
7 Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
Come, let Us go down and confuse their language, so that they will not understand one another’s speech.”
8 Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
So the LORD scattered them from there over the face of all the earth, and they stopped building the city.
9 Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
That is why it is called Babel, for there the LORD confused the language of the whole world, and from that place the LORD scattered them over the face of all the earth.
10 Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
This is the account of Shem. Two years after the flood, when Shem was 100 years old, he became the father of Arphaxad.
11 Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Arphaxad, Shem lived 500 years and had other sons and daughters.
12 Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
When Arphaxad was 35 years old, he became the father of Shelah.
13 Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Shelah, Arphaxad lived 403 years and had other sons and daughters.
14 Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
When Shelah was 30 years old, he became the father of Eber.
15 Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Eber, Shelah lived 403 years and had other sons and daughters.
16 Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
When Eber was 34 years old, he became the father of Peleg.
17 Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Peleg, Eber lived 430 years and had other sons and daughters.
18 Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
When Peleg was 30 years old, he became the father of Reu.
19 Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Reu, Peleg lived 209 years and had other sons and daughters.
20 Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
When Reu was 32 years old, he became the father of Serug.
21 Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Serug, Reu lived 207 years and had other sons and daughters.
22 Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
When Serug was 30 years old, he became the father of Nahor.
23 Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Nahor, Serug lived 200 years and had other sons and daughters.
24 Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
When Nahor was 29 years old, he became the father of Terah.
25 Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
And after he had become the father of Terah, Nahor lived 119 years and had other sons and daughters.
26 Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
When Terah was 70 years old, he became the father of Abram, Nahor, and Haran.
27 Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
This is the account of Terah. Terah became the father of Abram, Nahor, and Haran. And Haran became the father of Lot.
28 Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
During his father Terah’s lifetime, Haran died in his native land, in Ur of the Chaldeans.
29 Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
And Abram and Nahor took wives for themselves. Abram’s wife was named Sarai, and Nahor’s wife was named Milcah; she was the daughter of Haran, who was the father of both Milcah and Iscah.
30 Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
But Sarai was barren; she had no children.
31 Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
And Terah took his son Abram, his grandson Lot son of Haran, and his daughter-in-law Sarai the wife of Abram, and they set out from Ur of the Chaldeans for the land of Canaan. But when they arrived in Haran, they settled there.
32 Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.
Terah lived 205 years, and he died in Haran.

< Genesis 11 >