< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Njalo lezi yizizukulwana zamadodana kaNowa: UShemu, uHamu loJafethi. Kwasekuzalwa amadodana kubo emva kukazamcolo.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
Amadodana kaJafethi: UGomeri loMagogi loMadayi loJavani loThubhali loMesheki loTirasi.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
Lamadodana kaGomeri: UAshikenazi loRifathi loTogarma.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
Lamadodana kaJavani: UElisha loTarshishi, amaKiti lamaDodani.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
Kwehlukaniswa kusukela kubo izihlenge zezizwe emazweni abo, ngulowo lalowo ngokolimi lwakhe, langokosendo lwabo, ezizweni zabo.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
Lamadodana kaHamu: UKushi loMizirayimi loPuti loKhanani.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
Lamadodana kaKushi: USeba loHavila loSabitha loRama loSabitheka. Lamadodana kaRahama: UShebha loDedani.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
UKushi wasezala uNimrodi; yena waqala ukuba liqhawe emhlabeni.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
Yena waba ngumzingeli olamandla phambi kweNkosi; ngakho kuthiwa: NjengoNimrodi, umzingeli olamandla phambi kweNkosi.
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
Lokuqala kombuso wakhe yiBabeli leEreki leAkadi leKaline elizweni leShinari.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
Kwaphuma kulelolizwe uAshuri, wasesakha iNineve leRehobothi-Ire leKala,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
leReseni phakathi kweNineve leKala; lo ngumuzi omkhulu.
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
UMizirayimi wasezala amaLudi lamaAnami lamaLehabi lamaNafethuhi
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
lamaPatrusi lamaKaseluhi - lapho okwavela khona amaFilisti - lamaKafitori.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
UKhanani wasezala uSidoni izibulo lakhe, loHethi,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
lomJebusi lomAmori lomGirigashi
17 Ahivi, Aariki, Asini,
lomHivi lomArki lomSini
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
lomArvadi lomZemari lomHamathi; lemva kwalokho usendo lwamaKhanani lwahlakazeka.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
Umngcele wamaKhanani wasusukela eSidoni usiya eGerari uze ufike eGaza, usiya eSodoma leGomora leAdima leZeboyimi kuze kufike eLasha.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
La ngamadodana kaHamu, ngokosendo lwawo, langendimi zawo, emazweni awo, ezizweni zawo.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
UShemu laye wasezalelwa amadodana; unguyise wamadodana wonke akaEberi, umfowabo kaJafethi, omkhulu.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
Amadodana kaShemu: UElamu loAshuri loArpakishadi loLudi loAramu.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
Lamadodana kaAramu: U-Uzi loHuli loGetheri loMashi.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
UArpakishadi wasezala uShela; uShela wasezala uEberi.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
Kwasekuzalelwa uEberi amadodana amabili, ibizo lomunye nguPelegi, ngoba ensukwini zayo umhlaba wehlukaniswa; lebizo lomfowabo nguJokithani.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
UJokithani wasezala uAlimodadi loShelefi loHazamavethi loJera
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
loHadoramu loUzali loDikila
28 Obali, Abimaeli, Seba,
loObali loAbhimayeli loShebha
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
loOfiri loHavila loJobabi; bonke labo ngamadodana kaJokithani.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
Indawo yokuhlala kwabo isukela eMesha lapho usiya eSefari, intaba yempumalanga.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
La ngamadodana kaShemu, ngokosendo lwabo langendimi zabo, emazweni abo ngokwezizwe zabo.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
Lolu lusendo lwamadodana kaNowa ngezizukulwana zawo ezizweni zawo; kwasekusehlukaniswa kulaba izizwe emhlabeni emva kukazamcolo.

< Genesis 10 >