< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Voici les générations des fils de Noé, Sem, Cham et Japheth: car il leur naquit des fils après le déluge.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
Les fils de Japheth sont: Gomer, Magog, Madaï, Javan, Thubal, Mosoch et Thiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
Les fils de Gomer: Ascenez, Riphath et Thogorma.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
Et les fils de Javan: Elisa, Tharsis, Cetthim et Dodanim.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
C’est par eux que furent divisées les îles des nations dans leurs pays, chacun selon sa langue et ses familles dans leurs nations.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
Les fils de Cham: Chus, Mesraïm, Phuth et Chanaan.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
Les fils de Chus: Saba, Hévila, Sabatha, Regma et Sabatacha. Les fils de Regma: Saba et Dadan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
Or Chus engendra Nemrod; c’est lui qui commença à être puissant sur la terre.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
C’était un fort chasseur devant le Seigneur. De là est venu le proverbe: Comme Nemrod, fort chasseur devant le Seigneur.
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
Le commencement de son royaume fut Babylone, Arach, Achad et Chalanné, dans la terre de Sennaar.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
De ce pays sortit Assur qui bâtit Ninive, les rues de cette ville et Chalé,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
Et aussi Résen entre Ninive et Chalé: c’est la grande ville.
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
Quant à Mesraïm, il engendra Ludim, Anamim, Laabim, Nephthuim,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
Phétrusim et Chasluim, d’où sont sortis les Philistins et les Caphtorins.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
Chanaan engendra Sidon, son premier-né, l’Héthéen,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
Le Jébuséen, l’Amorrhéen, le Gergéséen,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
L’Hévéen, l’Aracéen, le Sinéen,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
L’Aradien, le Samaréen et l’Amathéen: et après cela se sont dispersés les peuples des Chananéens.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
Et les limites des Chananéens furent depuis Sidon en venant à Gérara, jusqu’à Gaza; et en venant à Sodome, Gomorrhe, Adama et Séboïm, jusqu’à Lésa.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
Ce sont là les enfants de Cham selon leur parenté, leurs langues, leurs générations, leurs pays et leurs nations.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
De Sem aussi, père de tous les enfants d’Héber et frère aîné de Japheth, naquirent des fils.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
Les fils de Sem sont: Elam, Assur, Arphaxad, Lud et Aram.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
Les fils d’Aram: Us, Hul, Géther et Mes.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
Or Arphaxad engendra Salé, dont est né Héber.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
À Héber naquirent deux fils: le nom de l’un fut Phaleg, parce qu’en ses jours la terre fut divisée; et le nom de son frère, Jectan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
Lequel Jectan engendra Elmodad, Saleph, Asarmoth, Jaré,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
Aduram, Uzal, Décla,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
Ebal, Abimaël, Saba,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
Ophir, Hévila et Jobab: tous ceux-là sont les fils de Jectan.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
Et leur habitation s’étendit de Messa jusqu’à Séphar, montagne qui est à l’orient.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
Voilà les fils de Sem, selon leur parenté, leurs langues, leurs pays et leurs nations.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
Et voilà les familles de Noé, selon leurs peuples et leurs nations. C’est par elles qu’ont été divisées toutes les nations sur la terre après le déluge.

< Genesis 10 >