< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
And these [are] the generations of the sons of Noah, Shem, Ham, and Japheth: and sons are born to them after the flood.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
Sons of Japheth [are] Gomer, and Magog, and Madai, and Javan, and Tubal, and Meshech, and Tiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
And sons of Gomer [are] Ashkenaz, and Riphath, and Togarmah.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
And sons of Javan [are] Elishah, and Tarshish, Kittim, and Dodanim.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
By these the islands of the nations have been parted in their lands, each by his tongue, by their families, in their nations.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
And sons of Ham [are] Cush, and Mitzraim, and Phut, and Canaan.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
And sons of Cush [are] Seba, and Havilah, and Sabtah, and Raamah, and Sabtechah; and sons of Raamah [are] Sheba and Dedan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
And Cush has begotten Nimrod;
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
he has begun to be a hero in the land; he has been a hero in hunting before YHWH; therefore it is said, “As Nimrod the hero [in] hunting before YHWH.”
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
And the first part of his kingdom is Babel, and Erech, and Accad, and Calneh, in the land of Shinar;
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
from that land he has gone out to Asshur, and builds Nineveh, even the broad places of the city, and Calah,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
and Resen, between Nineveh and Calah; it [is] the great city.
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
And Mitzraim has begotten the Ludim, and the Anamim, and the Lehabim, and the Naphtuhim,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
and the Pathrusim, and the Casluhim (from where have come out Philistim), and the Caphtorim.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
And Canaan has begotten Sidon his firstborn, and Heth,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
and the Jebusite, and the Amorite, and the Girgashite,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
and the Hivite, and the Arkite, and the Sinite,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
and the Arvadite, and the Zemarite, and the Hamathite; and afterward the families of the Canaanite have been scattered.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
And the border of the Canaanite is from Sidon, [in] your coming toward Gerar, to Gaza; [in] your coming toward Sodom, and Gomorrah, and Admah, and Zeboim, to Lasha.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
These [are] sons of Ham, by their families, by their tongues, in their lands, in their nations.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
As for Shem, father of all sons of Eber, the older brother of Japheth, he has also begotten.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
Sons of Shem [are] Elam, and Asshur, and Arphaxad, and Lud, and Aram.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
And sons of Aram [are] Uz, and Hul, and Gether, and Mash.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
And Arphaxad has begotten Salah, and Salah has begotten Eber.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
And two sons have been born to Eber; the name of the first [is] Peleg (for in his days the earth has been divided), and his brother’s name [is] Joktan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
And Joktan has begotten Almodad, and Sheleph, and Hazarmaveth, and Jerah,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
and Hadoram, and Uzal, and Diklah,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
and Obal, and Abimael, and Sheba,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
and Ophir, and Havilah, and Jobab; all these [are] sons of Joktan;
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
and their dwelling is from Mesha, [in] your coming toward Sephar, a mountain of the east.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
These [are] sons of Shem, by their families, by their tongues, in their lands, by their nations.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
These [are] families of the sons of Noah, by their generations, in their nations, and by these the nations have been parted in the earth after the flood.

< Genesis 10 >