< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Tito jsou pak rodové synů Noé, Sema, Chama a Jáfeta, jimž se tito synové zrodili po potopě.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
Synové Jáfetovi: Gomer a Magog, a Madai, a Javan, a Tubal, a Mešech, a Tiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
Synové pak Gomerovi: Ascenez, Rifat, a Togorma.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
Synové pak Javanovi: Elisa a Tarsis, Cetim a Dodanim.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
Od těch rozděleni jsou ostrovové národů po krajinách jejich, každý podlé jazyku svého, vedlé čeledi své, v národech svých.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
Synové pak Chamovi: Chus a Mizraim a Put a Kanán.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
A synové Chusovi: Sába, Evila, a Sabata, a Regma, a Sabatacha. Synové pak Regmovi: Sába a Dedan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
Zplodil také Chus Nimroda; onť jest počal býti mocným na zemi.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
To byl silný lovec před Hospodinem; protož se říká: Jako Nimrod silný lovec před Hospodinem.
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
Počátek pak jeho království byl Babylon a Erech, Achad a Chalne, v zemi Sinear.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
Z země té vyšel do Assur, kdežto vystavěl Ninive, a Rohobot město, a Chále,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
A Rezen mezi Ninive a mezi Chále; toť jest město veliké.
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
Mizraim pak zplodil Ludim a Anamim, a Laabim, a Neftuim,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
A Fetruzim, a Chasluim, (odkudž pošli Filistinští) a Kafturim.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
Kanán pak zplodil Sidona prvorozeného svého, a Het,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
A Jebuzea, a Amorea, a Gergezea,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
A Hevea, a Aracea, a Sinea,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
A Aradia, a Samarea, a Amatea; a potom odtud rozprostřely se čeledi Kananejských.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
A bylo pomezí Kananejských od Sidonu, když jdeš k Gerar až do Gázy; a odtud když jdeš k Sodomě a Gomoře, a Adama a Seboim až do Lázy.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
Ti jsou synové Chamovi po čeledech svých, vedlé jazyků svých, po krajinách svých, v národech svých.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
Semovi také, otci všech synů Heber, bratru Jáfeta staršího zrozeni jsou synové.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
A tito jsou synové Semovi: Elam, a Assur, a Arfaxad, a Lud, a Aram.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
Synové pak Aramovi: Hus, a Hul, a Geter, a Mas.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
Potom Arfaxad zplodil Sále; a Sále zplodil Hebera.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
Heberovi také narodili se dva synové; jméno jednoho Peleg, proto že za dnů jeho rozdělena byla země, a jméno bratra jeho Jektan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
Jektan pak zplodil Elmodada, a Salefa, a Azarmota, a Járe,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
A Adoráma, a Uzala, a Dikla,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
A Obale, a Abimahele, a Sebai,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
A Ofira, a Evila, a Jobaba; všickni ti jsou synové Jektanovi.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
A bylo bydlení jejich od Mesa, když jdeš k Sefar hoře na východ slunce.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
Tiť jsou synové Semovi po čeledech svých, vedlé jazyků svých, po krajinách svých, v národech svých.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
Ty jsou čeledi synů Noé po rodech svých, v národech svých; a od těch rozdělili se národové na zemi po potopě.

< Genesis 10 >